< Luka 2 >

1 Mʼmasiku amenewo Kaisara Augusto anapereka lamulo kuti kalembera achitike mʼdziko lonse la Aroma.
And it came to pass in those days, that there went out a decree from Caesar Augustus, that all the world should be taxed.
2 (Uyu ndi kalembera woyamba amene anachitika pamene Kureniyo anali bwanamkubwa wa Siriya).
(And this taxing was first made when Cyrenius was governor of Syria.)
3 Ndipo aliyense anapita ku mzinda wa kwawo kukalembetsa.
And all went to be taxed, every one into his own city.
4 Choncho Yosefe anachoka ku Nazareti ku Galileya kupita ku Yudeya, ku Betelehemu ku mudzi wa Davide, chifukwa anali wa banja ndi fuko la Davide.
And Joseph also went up from Galilee, out of the city of Nazareth, into Judaea, unto the city of David, which is called Bethlehem; (because he was of the house and lineage of David: )
5 Iye anapita kumeneko kukalembetsa pamodzi ndi Mariya, amene anapalana naye ubwenzi kuti akwatirane ndipo anali woyembekezera.
To be taxed with Mary his espoused wife, being great with child.
6 Ali kumeneko, nthawi inakwana yakuti mwana abadwe,
And so it was, that, while they were there, the days were accomplished that she should be delivered.
7 ndipo anabereka mwana wake woyamba, wamwamuna. Iye anamukulunga mʼnsalu ndi kumuyika modyera ngʼombe, chifukwa kunalibe malo mʼnyumba ya alendo.
And she brought forth her firstborn son, and wrapped him in swaddling clothes, and laid him in a manger; because there was no room for them in the inn.
8 Ndipo kunali abusa amene amakhala ku dera lomwelo, kuyangʼanira ziweto zawo usiku.
And there were in the same country shepherds abiding in the field, keeping watch over their flock by night.
9 Mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iwo ndipo ulemerero wa Ambuye unawala mowazungulira. Iwo anachita mantha.
And, lo, the angel of YHWH came upon them, and the glory of YHWH shone round about them: and they were sore afraid.
10 Koma mngeloyo anawawuza kuti, “Musachite mantha. Ine ndakubweretserani Uthenga Wabwino wachimwemwe chachikulu umene udzakhala wa anthu onse.
And the angel said unto them, Fear not: for, behold, I bring you good tidings of great joy, which shall be to all people.
11 Lero mʼmudzi wa Davide wakubwadwirani Mpulumutsi; Iye ndi Khristu Ambuye.
For unto you is born this day in the city of David a Saviour, which is the Messiah the Sovereign.
12 Ichi chidzakhala chizindikiro kwa inu: mukapeza mwana wakhanda wokutidwa ndi nsalu atagona modyera ngʼombe.”
And this shall be a sign unto you; Ye shall find the babe wrapped in swaddling clothes, lying in a manger.
13 Mwadzidzidzi gulu lalikulu la angelo linaonekera pamodzi ndi mngeloyo, kuyamika Mulungu ndi kumati,
And suddenly there was with the angel a multitude of the heavenly host praising YHWH, and saying,
14 “Ulemerero kwa Mulungu mmwambamwamba, ndi mtendere kwa anthu pa dziko lapansi amene Iye akondwera nawo.”
Glory to YHWH in the highest, and on earth peace, good will toward men.
15 Angelowo atabwerera kumwamba, abusawo anati kwa wina ndi mnzake, “Tiyeni ku Betelehemu tikaone zinthu zomwe zachitika, zimene Ambuye atiwuza ife.”
And it came to pass, as the angels were gone away from them into heaven, the shepherds said one to another, Let us now go even unto Bethlehem, and see this thing which is come to pass, which YHWH hath made known unto us.
16 Ndipo iwo anafulumira nyamuka nakapeza Mariya ndi Yosefe ndi mwana wakhanda, amene anagona modyera ngʼombe.
And they came with haste, and found Mary, and Joseph, and the babe lying in a manger.
17 Pamene anamuona Iye, iwo anafotokoza zomwe anawuzidwa za mwanayo,
And when they had seen it, they made known abroad the saying which was told them concerning this child.
18 ndipo onse amene anamva zimene abusawa ananena anadabwa.
And all they that heard it wondered at those things which were told them by the shepherds.
19 Koma Mariya anasunga zonsezi mu mtima mwake ndi kumazilingalira.
But Mary kept all these things, and pondered them in her heart.
20 Abusa anabwerera, akulemekeza ndi kuyamika Mulungu chifukwa cha zonse anazimva ndi kuziona, zomwe zinali monga anawuzidwira ndi angelo aja.
And the shepherds returned, glorifying and praising YHWH for all the things that they had heard and seen, as it was told unto them.
21 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, tsiku loti amuchite mdulidwe anamutcha Yesu, dzina limene mngelo anamupatsa asanabadwe.
And when eight days were accomplished for the circumcising of the child, his name was called Yahushua, which was so named of the angel before he was conceived in the womb.
22 Nthawi yoyeretsedwa kwawo itatha, monga mwa lamulo la Mose, Yosefe ndi Mariya anapita naye ku Yerusalemu kukamupereka kwa Ambuye.
And when the days of her purification according to the law of Moses were accomplished, they brought him to Jerusalem, to present him to YHWH;
23 (Monga mmene zinalembedwera mu lamulo la Ambuye kuti, “Muzikapereka kwa Ambuye mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa”),
(As it is written in the law of YHWH, Every male that openeth the womb shall be called holy to YHWH; )
24 ndi kupereka nsembe posunga zimene zinanenedwa mulamulo la Ambuye: “Njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri.”
And to offer a sacrifice according to that which is said in the law of YHWH, A pair of turtledoves, or two young pigeons.
25 Ndipo taonani, mu Yerusalemu munali munthu wotchedwa Simeoni, amene anali wolungama ndi wodzipereka. Iye ankadikira chitonthozo cha Israeli, ndipo Mzimu Woyera anali pa iye.
And, behold, there was a man in Jerusalem, whose name was Simeon; and the same man was just and devout, waiting for the consolation of Israel: and the Holy Spirit was upon him.
26 Mzimu Woyera anamuwululira kuti sadzafa asanaone Khristu wa Ambuye.
And it was revealed unto him by the Holy Spirit, that he should not see death, before he had seen YHWH 's Messiah.
27 Motsogozedwa ndi Mzimu Woyera, iye anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Makolo ake a Yesu atabwera naye kuti achite naye mwambo malingana ndi malamulo,
And he came by the Spirit into the temple: and when the parents brought in the child Yahushua, to do for him after the custom of the law,
28 Simeoni anamunyamula mʼmanja mwake nayamika Mulungu, nati:
Then took he him up in his arms, and blessed YHWH, and said,
29 “Ambuye waulamuliro, monga munalonjeza, tsopano lolani kuti mtumiki wanu apite mu mtendere.
YHWH, now lettest thou thy servant depart in peace, according to thy word:
30 Pakuti maso anga aona chipulumutso chanu,
For mine eyes have seen thy salvation,
31 chimene Inu munakonza pamaso pa anthu onse,
Which thou hast prepared before the face of all people;
32 kuwala kowunikira anthu a mitundu ina ndi kwa ulemerero kwa anthu anu Aisraeli.”
A light to lighten the Gentiles, and the glory of thy people Israel.
33 Abambo ndi amayi a Mwanayo anadabwa chifukwa cha zimene zinanenedwa za Iye.
And Joseph and his mother marvelled at those things which were spoken of him.
34 Kenaka Simeoni anawadalitsa ndipo anati kwa Mariya amayi ake: “Mwana uyu wakonzedwa kukhala kugwa ndi kudzuka kwa ambiri mu Israeli, ndi kukhala chizindikiro chimene adzayankhula motsutsana nacho,
And Simeon blessed them, and said unto Mary his mother, Behold, this child is set for the fall and rising again of many in Israel; and for a sign which shall be spoken against;
35 kotero kuti malingaliro a mitima ya ambiri adzawululidwa. Ndipo lupanga lidzabaya moyo wakonso.”
(Yea, a sword shall pierce through thy own soul also, ) that the thoughts of many hearts may be revealed.
36 Panalinso mneneri wamkazi, dzina lake Ana, mwana wa Fanuelo, wa fuko la Aseri. Anali wokalamba kwambiri; anakhala ndi mwamuna wake zaka zisanu ndi ziwiri atakwatiwa,
And there was one Anna, a prophetess, the daughter of Phanuel, of the tribe of Aser: she was of a great age, and had lived with an husband seven years from her virginity;
37 ndipo kenaka anakhala wamasiye mpaka pamene anali ndi zaka 84. Iye sanachoke mʼNyumba ya Mulungu koma ankapembedza usiku ndi usana, kusala kudya ndi kupemphera.
And she was a widow of about fourscore and four years, which departed not from the temple, but served YHWH with fastings and prayers night and day.
38 Pa nthawiyo pamene ankapita kwa iwo, iye anayamika Mulungu ndi kuyankhula za Mwanayo kwa onse amene ankayembekezera chipulumutso cha Yerusalemu.
And she coming in that instant gave thanks likewise unto YHWH, and spake of him to all them that looked for redemption in Jerusalem.
39 Yosefe ndi Mariya atachita zonse zimene zinkafunikira ndi lamulo la Ambuye, anabwerera ku Galileya ku mudzi wa Nazareti.
And when they had performed all things according to the law of YHWH, they returned into Galilee, to their own city Nazareth.
40 Ndipo Mwanayo anakula nakhala wamphamvu; Iye anadzazidwa ndi nzeru, ndipo chisomo cha Mulungu chinali pa Iye.
And the child grew, and waxed strong in spirit, filled with wisdom: and the grace of YHWH was upon him.
41 Chaka chilichonse makolo ake ankapita ku Yerusalemu ku phwando la Paska.
Now his parents went to Jerusalem every year at the feast of the passover.
42 Iye ali ndi zaka khumi ndi ziwiri, anapita ku phwando, monga mwa mwambo.
And when he was twelve years old, they went up to Jerusalem after the custom of the feast.
43 Phwando litatha, pamene makolo ake ankabwerera kwawo, mnyamata Yesu anatsalira ku Yerusalemu, koma iwo sanadziwe zimenezi.
And when they had fulfilled the days, as they returned, the child Yahushua tarried behind in Jerusalem; and Joseph and his mother knew not of it.
44 Poganiza kuti anali nawo mʼgulu lawo, anayenda tsiku limodzi. Kenaka anayamba kumufunafuna pakati pa abale awo ndi anzawo.
But they, supposing him to have been in the company, went a day's journey; and they sought him among their kinsfolk and acquaintance.
45 Atalephera kumupeza, anabwerera ku Yerusalemu kukamufuna.
And when they found him not, they turned back again to Jerusalem, seeking him.
46 Patatha masiku atatu anamupeza ali mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, atakhala pakati pa aphunzitsi, akumvetsera ndi kuwafunsa mafunso.
And it came to pass, that after three days they found him in the temple, sitting in the midst of the doctors, both hearing them, and asking them questions.
47 Aliyense amene anamumva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake ndi mayankho ake.
And all that heard him were astonished at his understanding and answers.
48 Makolo ake atamuona, anadabwa. Amayi ake anati kwa Iye, “Mwanawe, watichitira zimenezi chifukwa chiyani? Abambo ako ndi ine takhala tili ndi nkhawa kukufunafuna Iwe.”
And when they saw him, they were amazed: and his mother said unto him, Son, why hast thou thus dealt with us? behold, thy father and I have sought thee sorrowing.
49 Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumandifunafuna? Kodi simukudziwa kuti ndikuyenera kukhala mʼnyumba ya Atate anga?”
And he said unto them, How is it that ye sought me? knew ye not that I must be about my Father's business?
50 Koma iwo sanazindikire chomwe Iye amatanthauza.
And they understood not the saying which he spake unto them.
51 Kenaka anapita nawo ku Nazareti ndipo anawamvera iwo. Koma amayi ake anasunga zinthu zonsezi mu mtima mwawo.
And he went down with them, and came to Nazareth, and was subject unto them: but his mother kept all these sayings in her heart.
52 Ndipo Yesu anakula mu nzeru, msinkhu ndi chisomo cha Mulungu ndi anthu.
And Yahushua increased in wisdom and stature, and in favour with YHWH and man.

< Luka 2 >