< Marko 1 >

1 Chiyambi cha Uthenga Wabwino wa Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu,
The beginning of the evangel of Yahushua the Messiah, the Son of YHWH;
2 monga zalembedwera mʼbuku la mneneri Yesaya: “Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu, amene adzakonza njira yanu,”
As it is written in the prophets, Behold, I send my messenger before thy face, which shall prepare thy way before thee.
3 “Mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.’”
The voice of one crying in the wilderness, Prepare ye the way of YHWH, make his paths straight.
4 Ndipo Yohane anabwera mʼmadera a mʼchipululu nabatiza, ndi kulalikira za ubatizo wa kutembenuka mtima ndi wa chikhululukiro cha machimo.
John did baptize in the wilderness, and preach the baptism of repentance for the remission of sins.
5 Madera onse a ku Yudeya ndi anthu onse a ku Yerusalemu anatuluka napita kwa iye. Akavomereza machimo awo, amawabatiza mu mtsinje wa Yorodani.
And there went out unto him all the land of Judaea, and they of Jerusalem, and were all baptized of him in the river of Jordan, confessing their sins.
6 Yohane amavala zovala zopangidwa ndi ubweya wangamira, ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake, ndipo amadya dzombe ndi uchi wamthengo.
And John was clothed with camel's hair, and with a girdle of a skin about his loins; and he did eat locusts and wild honey;
7 Ndipo uthenga wake unali uwu: “Pambuyo panga pakubwera wina wondiposa ine mphamvu. Ine si woyenera kuwerama ndi kumasula zingwe za nsapato zake.
And preached, saying, There cometh one mightier than I after me, the latchet of whose shoes I am not worthy to stoop down and unloose.
8 Ine ndikubatizani ndi madzi, koma Iye adzakubatizani ndi Mzimu Woyera.”
I indeed have baptized you with water: but he shall baptize you with the Holy Spirit.
9 Pa nthawi imeneyo Yesu anabwera kuchokera ku Nazareti wa ku Galileya ndipo anabatizidwa ndi Yohane mu mtsinje wa Yorodani.
And it came to pass in those days, that Yahushua came from Nazareth of Galilee, and was baptized of John in Jordan.
10 Pamene Yesu ankatuluka mʼmadzi, anaona kumwamba kukutsekuka ndipo Mzimu Woyera akutsikira pa Iye ngati nkhunda.
And straightway coming up out of the water, he saw the heavens opened, and the Spirit like a dove descending upon him:
11 Ndipo Mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndipo ndikondwera nawe.”
And there came a voice from heaven, saying, Thou art my beloved Son, in whom I am well pleased.
12 Nthawi yomweyo Mzimu Woyera anamutumiza Iye ku chipululu,
And immediately the Spirit driveth him into the wilderness.
13 ndipo anali mʼchipululumo masiku makumi anayi, akuyesedwa ndi Satana. Anali pakati pa nyama zakuthengo; ndipo angelo anamutumikira.
And he was there in the wilderness forty days, tempted of Satan; and was with the wild beasts; and the angels ministered unto him.
14 Yohane atamutsekera mʼndende, Yesu anapita ku Galileya nalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu nati,
Now after that John was put in prison, Yahushua came into Galilee, preaching the gospel of the kingdom of YHWH,
15 “Nthawi yafika, ufumu wa Mulungu wayandikira. Tembenukani mtima ndi kukhulupirira Uthenga Wabwino!”
And saying, The time is fulfilled, and the kingdom of YHWH is at hand: repent ye, and believe the gospel.
16 Pamene Yesu ankayenda mʼmbali mwa nyanja ya Galileya, anaona Simoni ndi mʼbale wake Andreya akuponya khoka mʼnyanja, popeza anali asodzi.
Now as he walked by the sea of Galilee, he saw Simon and Andrew his brother casting a net into the sea: for they were fishers.
17 Yesu anati, “Bwerani, tsateni Ine, ndipo ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
And Yahushua said unto them, Come ye after me, and I will make you to become fishers of men.
18 Nthawi yomweyo anasiya makoka awo namutsata Iye.
And straightway they forsook their nets, and followed him.
19 Atapita patsogolo pangʼono, anaona Yakobo ndi mʼbale wake Yohane ana a Zebedayo, ali mʼbwato akukonza makoka awo.
And when he had gone a little further thence, he saw James the son of Zebedee, and John his brother, who also were in the ship mending their nets.
20 Mosataya nthawi anawayitana, ndipo anasiya abambo awo Zebedayo ndi anyamata aganyu ali mʼbwatomo, namutsata Iye.
And straightway he called them: and they left their father Zebedee in the ship with the hired servants, and went after him.
21 Iwo anapita ku Kaperenawo, ndipo tsiku la Sabata litafika, Yesu analowa mʼsunagoge nayamba kuphunzitsa.
And they went into Capernaum; and straightway on the Sabbath day he entered into the synagogue, and taught.
22 Anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake, chifukwa anawaphunzitsa ngati munthu amene anali ndi ulamuliro, osati ngati aphunzitsi amalamulo.
And they were astonished at his doctrine: for he taught them as one that had authority, and not as the scribes.
23 Pomwepo munthu wina mʼsunagogemo amene anali wogwidwa ndi mzimu woyipa anafuwula kuti,
And there was in their synagogue a man with an unclean spirit; and he cried out,
24 “Mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”
Saying, Let us alone; what have we to do with thee, thou Yahushua of Nazareth? art thou come to destroy us? I know thee who thou art, the Holy One of YHWH.
25 Yesu anadzudzula chiwandacho mwamphamvu nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye!”
And Yahushua rebuked him, saying, Hold thy peace, and come out of him.
26 Mzimu woyipawo unamugwedeza mwamphamvu ndipo unatuluka mwa iye ukufuwula.
And when the unclean spirit had torn him, and cried with a loud voice, he came out of him.
27 Anthu anadabwa kwambiri kotero kuti anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Ichi nʼchiyani? Chiphunzitso chatsopano ndi ulamuliro! Iye akulamula, ngakhale mizimu yoyipa ikumumvera.”
And they were all amazed, insomuch that they questioned among themselves, saying, What thing is this? what new doctrine is this? for with authority commandeth he even the unclean spirits, and they do obey him.
28 Mbiri yake inafalikira kudera lonse la Galileya mofulumira.
And immediately his fame spread abroad throughout all the region round about Galilee.
29 Atangochoka mu sunagoge, Yesu pamodzi ndi Yakobo ndi Yohane anakalowa mʼnyumba ya Simoni ndi Andreya.
And forthwith, when they were come out of the synagogue, they entered into the house of Simon and Andrew, with James and John.
30 Mpongozi wa Simoni anali chigonere akudwala malungo, ndipo anamuwuza Yesu za iye.
But Simon's wife's mother lay sick of a fever, and anon they tell him of her.
31 Ndipo Yesu anapita kwa iye, namugwira dzanja namuthandiza kudzuka. Malungo anachoka ndipo anayamba kuwatumikira.
And he came and took her by the hand, and lifted her up; and immediately the fever left her, and she ministered unto them.
32 Madzulo omwewo dzuwa litalowa anthu anabweretsa kwa Yesu anthu onse odwala ndi ogwidwa ndi ziwanda.
And at even, when the sun did set, they brought unto him all that were diseased, and them that were possessed with devils.
33 Anthu onse a mʼmudzimo anasonkhana pa khomo,
And all the city was gathered together at the door.
34 Yesu anachiritsa ambiri amene anali ndi matenda osiyanasiyana, komanso anatulutsa ziwanda zambiri, ndipo sanalole kuti ziwandazo ziyankhule chifukwa zinkamudziwa Iye.
And he healed many that were sick of divers diseases, and cast out many devils; and suffered not the devils to speak, because they knew him.
35 Mmamawa, kukanali kamdima, Yesu anadzuka, nachoka pa nyumbapo kupita kumalo kwa yekha, kumene anakapemphera.
And in the morning, rising up a great while before day, he went out, and departed into a solitary place, and there prayed.
36 Simoni ndi anzake anapita kokamufunafuna Iye,
And Simon and they that were with him followed after him.
37 ndipo atamupeza, anamuwuza kuti, “Aliyense akukufunani!”
And when they had found him, they said unto him, All men seek for thee.
38 Yesu anayakha kuti, “Tiyeni tipite kwina ku midzi ya pafupi kuti ndikalalikirenso kumeneko. Ichi ndi chifukwa chimene ndinabwerera.”
And he said unto them, Let us go into the next towns, that I may preach there also: for therefore came I forth.
39 Potero anayendayenda mu Galileya, kulalikira mʼmasunagoge awo ndi kutulutsa ziwanda.
And he preached in their synagogues throughout all Galilee, and cast out devils.
40 Munthu wakhate anabwera kwa Iye, nagwada, namupempha kuti, “Ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
And there came a leper to him, beseeching him, and kneeling down to him, and saying unto him, If thou wilt, thou canst make me clean.
41 Yesu pomva naye chifundo, anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!”
And Yahushua, moved with compassion, put forth his hand, and touched him, and saith unto him, I will; be thou clean.
42 Nthawi yomweyo khate linachoka ndipo anachiritsidwa.
And as soon as he had spoken, immediately the leprosy departed from him, and he was cleansed.
43 Nthawi yomweyo Yesu anamuwuza kuti apite koma anamuchenjeza kuti,
And he straitly charged him, and forthwith sent him away;
44 “Wonetsetsa kuti usawuze aliyense za zimenezi. Koma pita, kadzionetse wekha kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose analamulira zotsimikizira kuyeretsedwa kwanu, ngati umboni kwa iwo.”
And saith unto him, See thou say nothing to any man: but go thy way, shew thyself to the priest, and offer for thy cleansing those things which Moses commanded, for a testimony unto them.
45 Mʼmalo mwake anapita nayamba kuyankhula momasuka, nafalitsa mbiriyo. Zotsatira zake, Yesu sanathe kulowa mʼmudzi moonekera, koma anakhala kunja kumalo kopanda anthu. Komabe anthu amabwera kwa Iye kuchokera kulikonse.
But he went out, and began to publish it much, and to blaze abroad the matter, insomuch that Yahushua could no more openly enter into the city, but was without in desert places: and they came to him from every quarter.

< Marko 1 >