< Levitiko 8 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spak to Moises, and seide, Take thou Aaron with hise sones,
2 “Tenga Aaroni ndi ana ake, zovala zawo, mafuta wodzozera, ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo, nkhosa ziwiri zazimuna ndi dengu la buledi wopanda yisiti,
`the clothes of hem, and the oile of anoyntyng, a calf for synne, twei rammes, a panyere with therf looues;
3 ndipo usonkhanitse gulu la anthu pa khomo la tenti ya msonkhano.”
and thou schalt gedere al the cumpanye to the dore of the tabernacle.
4 Mose anachita zomwe Yehova anamulamula ndipo gulu la anthu linasonkhana pa khomo la tenti ya msonkhano.
Moises dide as the Lord comaundide; and whanne al the company was gaderid bifor the yatis of the tabernacle, he seide,
5 Mose anawuza gulu la anthuwo kuti, “Izi ndi zimene Yehova walamulira kuti zichitike.”
This is the word which the Lord comaundid to be don.
6 Pamenepo Mose anabwera ndi Aaroni ndi ana ake nawasambitsa ndi madzi.
And anoon Moises offride Aaron and hise sones; and whanne he hadde waischun hem,
7 Anamuveka Aaroni mwinjiro, ndi kumumanga lamba mʼchiwuno. Anamuvekanso mkanjo wa efodi ndi efodiyo. Anamangira lamba efodiyo amene analukidwa mwaluso uja, motero efodiyo analimba mʼchiwunomo.
he clothide the bischop with a lynnun schirte, `and girdide `the bischop with a girdil, and clothide with a coote of iacynt, and `puttide the cloth on the schuldris aboue,
8 Anamuvekanso chovala chapachifuwa ndipo mʼchovalacho anayikamo Urimu ndi Tumimu.
which cloth on the schuldris he boond with a girdil, and `dresside to the racional, wherynne doctryn and truthe was.
9 Kenaka anamuveka Aaroniyo nduwira kumutu ndipo patsogolo pa nduwirayo anayikapo duwa lagolide, chizindikiro chopatulika monga momwe Yehova analamulira Mose.
And Moises hilide the heed with a mytre, and `settide theronne, ayens the forhed, the goldun plate halewid in halewyng, as the Lord comaundide to hym.
10 Pamenepo Mose anatenga mafuta wodzozera nadzoza tenti ya msonkhano pamodzi ndi zonse zimene zinali mʼmenemo, ndipo potero anazipatula.
He took also the oile of anoyntyng, with which he anoyntide the tabernacle with al his purtenaunce;
11 Anawaza mafuta ena pa guwa kasanu ndi kawiri, nalidzoza guwalo pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso beseni ndi tsinde lake, nazipatula.
and whanne he hadde halewid and hadde spreynt the auter seuen sithes, he anoyntide it, and halewide with oile alle the vessels therof, and the `greet waischyng vessel with his foundement.
12 Anathira mafuta wodzozera ena pamutu pa Aaroni ndipo anamudzoza ndi kumupatula.
Which oile he schedde on `the heed of Aaron, and anoyntide hym, and halewide.
13 Kenaka anabwera ndi ana a Aaroni. Anawaveka minjiro, ndi kuwamanga malamba mʼchiwuno ndi kuwaveka nduwira kumutu monga momwe Yehova analamulira Mose.
And he clothide with lynnun cootis, and girdide with girdils `his sones offrid, and settide on mytris, as the Lord comaundide.
14 Kenaka Mose anabwera ndi ngʼombe yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, ndipo Aaroni ndi ana ake anasanjika manja awo pamutu pa ngʼombeyo.
He offeride also a calf for synne; and whanne Aaron and hise sones hadden put her hondis on `that calf,
15 Mose anapha ngʼombeyo, ndi kutenga magazi ena angʼombeyo ndi kupaka ndi chala chake pa nyanga zaguwa lansembe, naliyeretsa. Magazi otsalawo anawakhuthulira pa tsinde laguwalo. Motero anachita mwambo wopepesera machimo.
he offride it, and drow up blood; and whanne the fyngur was dippid, he touchide the corneris of the auter bi cumpas; whanne the auter was clensid and halewid, he schedde the `residue blood at the `foundement therof.
16 Mose anatenganso mafuta onse okuta matumbo, mafuta ophimba chiwindi, ndiponso impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta ake, nazitentha pa guwapo.
Sotheli he brent on the auter the ynnere fatnesse that was on the entrails, and the calle of the mawe, and the twei litle reynes with her litle fatnessis;
17 Koma nyama yangʼombeyo, chikopa chake ndi matumbo ake anaziwotcha kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
and he brente without the castels the calf, with the skyn, fleischis, and dung, as the Lord comaundide.
18 Kenaka anabwera ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopsereza, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
He offride also a ram in to brent sacrifice; and whanne Aaron and hise sones hadden set her hondis on the heed therof,
19 Ndipo Mose anapha nkhosayo ndi kuwaza magazi ake mbali zonse zaguwalo.
he offride it, and schedde the blood therof bi the cumpas of the auter.
20 Anayidula nkhosayo nthulinthuli ndipo anatentha mutu wake, nthulizo ndi mafuta.
And he kittide thilke ram in to gobetis, and brente with fier the heed therof, and membris,
21 Anatsuka matumbo ake ndi miyendo yake, ndi kutentha nkhosa yonseyo pa guwa lansembe kuti ikhale nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yachakudya yoperekedwa kwa Yehova monga Yehovayo analamulira Mose.
and ynnere fatnesse, whanne the entrails and feet weren waischun bifore; and he brente al the ram togidere on the auter, for it was the brent sacrifice of swettiste odour to the Lord, as the Lord comaundide to hym.
22 Kenaka Mose anapereka nkhosa yayimuna ina pamwambo wodzoza ansembe, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
He offride also the secounde ram, in to the halewyng of preestis; and Aaron and hise sones puttiden her hondis on the heed therof.
23 Mose anayipha nkhosayo ndipo anatenga magazi ake ena ndi kupaka ndewere za khutu la kudzanja lamanja la Aaroni, pa chala chake chachikulu cha kudzanja lamanja, ndi pa chala chake chachikulu cha phazi lakumanja.
And whanne Moises hadde offrid the ram, he took of the blood, and touchide the laste part of the riyt eere of Aaron, and the thombe of his riyt hond, in lijk maner and of the foot.
24 Pambuyo pake Mose anabwera ndi ana aamuna a Aaroni ndi kupaka magazi pa ndewere za makutu awo akumanja, pa zala zawo zazikulu za dzanja lamanja, ndiponso pa zala zawo zazikulu za kuphazi lakumanja. Kenaka iye anawaza magazi otsalawo mbali zonse za guwalo.
He offride also `the sones of Aaron. And whanne he hadde touchid of the blood of the ram offrid the laste part of `the riyt eeris of alle, and `the thombis of the riyt hond and foot, he schedde the `tothir blood on the auter bi cumpas.
25 Anatenganso mafuta ake, mafuta a ku mchira wake, mafuta okuta matumbo, mafuta okuta chiwindi, impsyo zonse ziwiri ndi mafuta ake ndiponso ntchafu yakumanja.
Sotheli he departide the ynnere fatnesse, and the taile, and al the fatnesse that hilith the entrails, and the calle of the mawe, and the twey reynes with her fatnessis and with the riyt schuldur.
26 Ndipo mʼdengu la buledi wopanda yisiti limene linali pamaso pa Yehova, anatengamo buledi mmodzi, buledi mmodzi wokhala ndi mafuta a olivi, ndi buledi wopyapyala mmodzi. Zonsezi anaziyika pa mafuta aja ndi pa ntchafu ya ku dzanja lamanja ija.
Forsothe he took of the panyere of therf looues, that was bifor the Lord, looues without sour dow, and a cake spreynt with oile, and he puttide looues first sodun in watir and aftirward fried in oile on the ynnere fatnesse, and the riyt schuldur; and bitook alle thingis togidere to Aaron,
27 Mose anapereka zonsezi mʼmanja mwa Aaroni ndi ana ake amene anazipereka kwa Yehova kuti zikhale nsembe yoweyula.
and to hise sones. And aftir that thei `reisiden tho bifore the Lord,
28 Kenaka Mose anazitenga mʼmanja mwawo ndipo anazipsereza pa guwa lansembe pamwamba penipeni pamodzi ndi nsembe yopsereza ija kuti ikhale nsembe yopereka pamwambo wodzoza ansembe, kuti ipereke fungo lokoma, chopereka chachakudya kwa Yehova.
eft `he brente tho takun of her hondis, on the auter of brent sacrifice, for it was the offryng of halewyng, in to the odour of swetnesse of sacrifice `into his part to the Lord.
29 Mose anatenga chidale cha nkhosa yayimuna, chomwe ndi gawo lake pamwambo wodzoza ansembe, ndipo anachiweyula pamaso pa Yehova kuti chikhale nsembe yoweyula monga momwe Yehova analamulira Mose.
He took also the brest of the ram of consecracioun in to his part, and reiside it bifor the Lord, as the Lord comaundide to hym.
30 Kenaka Mose anatenga mafuta wodzozera ansembe ndi magazi amene anali pa guwa nawaza pa Aaroni ndi zovala zake ndiponso ana ake aja ndi zovala zawo. Motero Mose anapatula Aaroni ndi zovala zake, ndiponso ana ake ndi zovala zawo.
And he took the oynement, and blood that was in the auter, and `spreynte on Aaron, and hise clothis, and on `the sones of hym, and on her clothis.
31 Mose anawuza Aaroni ndi ana ake kuti, “Phikani nyamayo pa khomo la tenti ya msonkhano, ndipo mudyere pomwepo pamodzi ndi buledi amene ali mʼdengu la zopereka za pamwambo wodzoza ansembe monga Yehova analamulira kuti, ‘Aaroni ndi ana ake azidya zimenezi.’
And whanne he hadde halewid hem in her clothing, he comaundide to hem, and seide, Sethe ye fleischis bifor the `yatis of the tabernacle, and there ete ye tho; also ete ye the looues of halewyng, that ben put in the panyere, as God comaundide to me, `and seide, Aaron and hise sones schulen ete tho looues;
32 Ndipo nyama ndi buledi zotsalazo, muziwotche.
sotheli whateuer thing is residue of the fleisch and looues, fier schal waste.
33 Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano kwa masiku asanu ndi awiri mpaka masiku amwambo wokudzozani unsembe atatha, pakuti mwambowu ndi wa masiku asanu ndi awiri.
Also ye schulen not go out of the dore of the tabernacle in seuene daies, til to the day in which the tyme of youre halewyng schal be fillid; for the halewyng is endid in seuene dayes,
34 Zimene zachitika lerozi analamula ndi Yehova kuti zichitike ngati nsembe yopepesera machimo anu.
as it is doon in present tyme, that the riytfulnesse of sacrifice were fillid.
35 Muzikhala pa khomo la tenti ya msonkhano usana ndi usiku kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo muzichita zimene Yehova wakulamulani kuti musafe, pakuti zimenezi ndi zomwe Yehova wandilamulira.”
Ye schulen dwelle dai and nyyt in the tabernacle, and ye schulen kepe the kepyngis of the Lord, that ye die not; for so it is comaundid to me.
36 Choncho Aaroni ndi ana ake anachita zonse zimene Yehova analamula kudzera mwa Mose.
And Aaron and hise sones diden alle thingis, whiche the Lord spak bi the hond of Moises.

< Levitiko 8 >