< Levitiko 22 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spak to Moises, and seide, Speke thou to Aaron and to hise sones,
2 “Uza Aaroni ndi ana ake kuti azilemekeza zinthu zopatulika zimene Aisraeli azipereka kwa Ine, kuti asayipitse dzina langa loyera. Ine ndine Yehova.
that thei be war of these thingis of the sones of Israel, whiche thingis ben halewid; and that they defoule not the name of thingis halewid to me, whiche thingis thei offren; Y am the Lord.
3 “Uwawuze kuti ngati wina aliyense mwa zidzukulu zawo mʼmibado yonse imene ikubwera adzayandikira zinthu zopatulika zimene ana a Israeli apereka kwa Yehova, ali wodetsedwa, ameneyo achotsedwe pamaso pa Yehova. Ine ndine Yehova.
Seie thou to hem, and to the aftir comeris of hem, Ech man of youre kynrede, `which man neiyeth to tho thingis that ben halewid, and whiche thingis the sones of Israel offreden to the Lord, in `which man is vnclennesse, schal perische bifor the Lord; Y am the Lord.
4 “Munthu aliyense mwa zidzukulu za Aaroni amene ali ndi khate kapena amatulutsa zoyipa mʼthupi mwake, asadye zinthu zopatulika mpaka atayeretsedwa. Wansembe angakhale wodetsedwa atakhudzana ndi chinthu chimene chadetsedwa ndi chinthu chakufa kapena kukhudza munthu amene wataya umuna,
A man of the seed of Aaron, `which man is leprouse, ethir suffrith `fletyng out of seed, schal not ete of these thingis, that ben halewid to me, til he be heelid. He that touchith an vncleene thing on a deed bodi, and fro whom the seed as of leccherie goith out, and which touchith a crepynge beeste,
5 kapena kukhudza chilichonse chokwawa chomwe chimadetsa munthu, kapena kukhudza munthu amene angamudetse, kapenanso kukhudza kanthu kena kalikonse kodetsedwa.
and what euer vncleene thing, whos touchyng is foul,
6 Tsono ngati wansembe angakhudze chilichonse mwa zimenezi ndiye kuti adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Asadye chopereka chilichonse chopatulika mpaka atasamba thupi lake lonse.
schal be vncleene `til to euentid, and he schal not ete these thingis, that ben halewid to me; but whanne he hath waische his fleisch in watir,
7 Munthuyo adzakhala woyeretsedwa pamene dzuwa lalowa, ndipo angathe kudya chopereka chopatulikacho popeza ndi chakudya chake.
and the sunne hath go doun, thanne he schal be clensid, and schal ete halewid thingis, for it is his mete.
8 Wansembe sayenera kudya chinthu chofa chokha kapena chojiwa ndi chirombo kuopa kuti angadzidetse ndi chakudyacho. Ine ndine Yehova.
He schal not ete a thing deed bi it silf, and takun of a beeste, nethir he schal be defoulid in tho; Y am the Lord.
9 “‘Choncho ansembe azisunga malamulo angawa kuti asapezeke wolakwa ndi kufa chifukwa chopeputsa malamulowa. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.
Thei schulen kepe myn heestis, that thei be not suget to synne, and die in the seyntuarye, whanne thei han defoulid it; Y am the Lord that halewe you.
10 “‘Aliyense amene si wabanja la wansembe, kaya ndi mlendo wa wansembe, kapena wantchito wake, asadye chopereka chopatulika.
Ech alien schal not ete of thingis halewid; the hyne which is a straunger, and the hirid man of the preest, schulen not ete of tho. Sotheli these seruauntis,
11 Koma kapolo amene wagulidwa ndi ndalama kapena kubadwira mʼbanja la wansembe angathe kudya chakudya cha wansembeyo.
whom the preest hath bouyt, and which is a borun seruaunt of his hows, schulen ete of tho.
12 Mwana wamkazi wa wansembe amene wakwatiwa ndi munthu amene si wansembe, asadyeko nsembe zopatulikazo.
If the `douyter of the preest is weddid to ony of the puple, sche schal not ete of these thingis that ben halewid, and of the firste fruytis;
13 Koma mwana wamkazi wa wansembe amene ali wamasiye kapena wosudzulidwa, ndipo alibe mwana, komanso anabwerera ku nyumba ya abambo ake monga pa nthawi ya utsikana wake, angathe kudya chakudya cha abambo ake. Mlendo asadye chakudya chopatulika.
sotheli if sche is a widewe, ether forsakun, and turneth ayen with out fre children to `the hows of hir fadir, sche schal be susteyned bi the metis of hir fadir, as a damysel was wont; ech alien hath not power to ete of tho.
14 “‘Ngati munthu wina aliyense adya chopereka chopatulika mosadziwa, munthuyo amubwezere wansembe chinthu chopatulikacho ndipo awonjezerepo limodzi la magawo asanu a chinthucho.
He that etith bi ignoraunce of halewid thingis, schal adde the fyuethe part with that that he eet, and `schal yyue to the preest in seyntuarie,
15 Choncho ansembe asayipitse zopereka zopatulika za Aisraeli zimene apereka kwa Yehova
and thei schulen not defoule the halewid thingis of the sones of Israel, whiche thei offren to the Lord,
16 ndipo asachimwitse ndi kupalamulitsa Aisraeli powalola kudya zakudya zawo zopatulika. Ine ndine Yehova amene ndimawayeretsa.’”
lest perauenture thei suffren the wickidnesse of her trespas, whanne thei han ete halewid thingis; Y am the Lord that `halewe hem.
17 Yehova anawuza Mose kuti,
The Lord spak to Moises, and seide,
18 “Yankhula ndi Aaroni, ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse, ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati wina aliyense wa inu, Mwisraeli kapena mlendo amene akukhala mu Israeli abwera ndi mphatso ya nsembe yopsereza kwa Yehova, kupereka chimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu,
Speke thou to Aaron and to hise sones, and to alle the sones of Israel, and thou schalt seie to hem, A man of the hous of Israel and of comelyngis that dwellen at hem, which offrith his offryng to the Lord, and ethir paieth avowis, ethir offrith bi his fre wille, what euer thing he offrith in to brent sacrifice of the Lord, that it be offrid bi you,
19 ndiye kuti abwere ndi ngʼombe yayimuna, nkhosa yayimuna kapena mbuzi yayimuna. Izi zikhale zopanda chilema kuti zilandiridwe.
it schal be a male without wem, of oxen, and of scheep, and of geet; if it hath a wem,
20 Musapereke nyama iliyonse yokhala ndi chilema chifukwa sidzalandiridwa mʼmalo mwanu.
ye schulen not offre, nether it schal be acceptable.
21 Pamene wina aliyense abweretsa ngʼombe kapena nkhosa kuti ikhale nsembe yachiyanjano kwa Yehova, kukwaniritsa zimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu, nyamayo iyenera kukhala yangwiro ndi yopanda chilema kuti ilandiridwe.
A man that offrith a sacrifice of pesyble thingis to the Lord, and ethir paieth auowis, ethir offrith bi fre wille, as wel of oxun as of scheep, he schal offre a beeste without wem, that it be acceptable; ech wem schal not be ther ynne.
22 Musapereke kwa Yehova nyama zakhungu, zovulala kapena zolumala, kapena nyama zimene zikutulutsa mafinya mʼthupi mwake, kapena zimene zili ndi nthenda yonyerenyetsa, kapena zimene zili ndi mphere. Nyama zotere musaziyike pa guwa kuti zikhale nsembe yopsereza kwa Yehova.
If it is blynd, if it is brokun, if it hath a scar, if it hath whelkis, ether scabbe, ethir drie scabbe, ye schulen not offre tho beestis to the Lord, nether ye schulen brenne of tho beestis on the auter of the Lord.
23 Koma mungathe kupereka ngʼombe yayimuna kapena nkhosa imene ili ndi chiwalo chachitali kapena chachifupi kukhala nsembe yaufulu. Koma simungayipereke ngati nsembe yoperekera zimene munalumbirira chifukwa sidzalandiridwa.
A man may offre wilfuli an oxe and scheep, whanne the eere and tail ben kit of; but avow may not be paied of these beestis.
24 Nyama iliyonse imene mavalo ake ndi onyuka kapena ophwanyika, ongʼambika kapena oduka, musamayipereke kwa Yehova mʼdziko lanu.
Ye schulen not offre to the Lord ony beeste, whose priuy membris ben brokun, ethir brisid, ether kit, and takun awey, and outerli ye schulen not do these thingis in youre lond.
25 Ndipo musalandire nyama zotere kuchokera kwa mlendo ndi kuzipereka kukhala zakudya za Mulungu wanu. Zimenezi sizidzalandiridwa mʼmalo mwanu chifukwa zili ndi chilema ndipo ndi zolumala.’”
Of `the hond of an alien ye schulen not offre looues to youre God, and what euer other thing he wole yyue, for alle thingis ben corrupt and defoulid; ye schulen not resseyue tho.
26 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spak to Moises,
27 “Pamene mwana wangʼombe, mwana wankhosa kapena mwana wambuzi wabadwa, akhale ndi make kwa masiku asanu ndi awiri. Kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu mpaka mʼtsogolo mwake, angathe kulandiridwa kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
and seide, Whanne an oxe, scheep and goet ben brouyt forth `of the modris wombe, in seuene daies tho schulen be vnder `the tete of her modir; sotheli in the eiyte dai, and fro thennus forth, tho moun be offrid to the Lord,
28 Musaphe ngʼombe kapena nkhosa pamodzi ndi mwana wake tsiku limodzi. Muyidye pa tsiku lomwelo; musasiyeko ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
whether thilke is a cow, whether `thilke is a scheep; tho schulen not be offrid in o dai with her fruytis.
29 “Pamene mupereka nsembe yoyamika kwa Yehova, muyipereke mwakufuna kwanu mu njira yoti ilandiridwe mʼmalo mwanu.
If ye offren to the Lord a sacrifice for the doyng of thankyngis, that it mai be plesaunt,
30 Muyidye pa tsiku lomwelo, wosasiyako ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
ye schulen ete it in the same dai in which it is offrid; ony thing schal not leeue in the morewtid of the tother dai; Y am the Lord.
31 “Choncho sungani malamulo anga ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.
Kepe ye myn heestis, and do ye tho; Y am the Lord.
32 Musanyoze dzina langa loyera. Koma lilemekezedwe pakati pa Aisraeli. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani
Defoule ye not myn hooli name, that Y be halewid in the myddis of the sones of Israel; Y am the Lord, that halewe you, and ledde you out of the lond of Egipt,
33 ndipo ndine amene ndinakutulutsani mu Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.”
that Y schulde be to you in to God; Y am the Lord.

< Levitiko 22 >