< Levitiko 12 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
And the Lord spak to Moises, `and seide, Speke thou to the sones of Israel,
2 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Mkazi akakhala woyembekezera, nabala mwana wa mwamuna, mkaziyo adzakhala wodetsedwa kwa masiku asanu ndi awiri, ngati pa masiku ake akusamba.
and thou schalt seie to hem, If a womman, whanne sche hath resseyued seed, childith a knaue child, sche schal be vnclene bi seuene daies bi the daies of departyng of corrupt blood, that renneth bi monethis;
3 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, mwanayo achite mdulidwe.
and the yong child schal be circumsidid in the eiytithe dai.
4 Mkaziyo adikire masiku ena 33 kuti ayeretsedwe ku matenda ake. Asakhudze kanthu kalikonse koyera kapena kulowa mʼmalo wopatulika mpaka masiku a kuyeretsedwa kwake atatha.
Sotheli sche schal dwelle thre and thretti daies in the blood of hir purifiyng; sche schal not touche ony hooli thing, nethir sche schal entre in to the seyntuarie, til the daies of her clensing be fillid.
5 Ngati abala mwana wamkazi, adzakhala wodetsedwa kwa masabata awiri, monga zikhalira pa nthawi yake yosamba. Ndipo mkaziyo adikire masiku ena 66, kuti ayeretsedwe ku matenda akewo.
Sotheli if sche childith a female, sche schal be vnclene twei woukis, bi the custom of flowyng of vnclene blood, and `thre scoor and sixe daies sche schal dwelle in the blood of her clensyng.
6 “‘Masiku ake wodziyeretsa akatha, kaya ndi a mwana wamwamuna kapena a mwana wamkazi, abwere kwa wansembe ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi pa khomo la tenti ya msonkhano kuti ikhale nsembe yopsereza. Abwerenso ndi chiwunda cha nkhunda kapena njiwa kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.
And whanne the daies of hir clensyng, for a sone, ether for a douytir, ben fillid, sche schal brynge a lomb of o yeer in to brent sacrifice, and a `bryd of a culuer, ethir a turtle, for synne, to the dore of the tabernacle of witnessyng;
7 Wansembeyo apereke zimenezi pamaso pa Yehova pochita mwambo wopepesera mkaziyo. Ndipo mkaziyo adzakhala woyeretsedwa ku msambo wake. “‘Amenewa ndiwo malamulo a mkazi amene wabala mwana wamwamuna kapena wamkazi.
and sche schal yyue to the preest, which schal offre tho bifor the Lord, and schal preye for hir, and so sche schal be clensid fro the fowyng of hir blood. This is the lawe of a womman childynge a male, ethir a female.
8 Ngati mkaziyo sangathe kupeza mwana wankhosa, abwere ndi njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri: imodzi ikhale ya nsembe yopsereza ndipo inayo ikhale ya nsembe yopepesera machimo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera wa mkaziyo ndipo adzayeretsedwa.’”
That if hir hond fyndith not, nethir may offre a lomb, sche schal take twei turtlis, ethir twei `briddis of culueres, oon in to brent sacrifice, and the tother for synne; and the preest schal preye for hir, and so sche schal be clensid.

< Levitiko 12 >