< Levitiko 1 >

1 Yehova anayitana Mose mu tenti ya msonkhano. Iye anati,
Forsothe the Lord clepide Moyses, and spak to him fro the tabernacle of witnessyng, `and seide,
2 “Aliyense wa inu ngati abwera ndi nsembe kwa Yehova kuchokera pa ziweto zake, choperekacho chikhale ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi.
Speke thou to the sones of Israel, and thou schalt seie to hem, A man of you, that offrith to the Lord a sacrifice of beestis, that is, of oxun and of scheep, and offrith slayn sacrifices, if his offryng is brent sacrifice,
3 “‘Ngati munthu apereka nsembe yopsereza ya ngʼombe, ikhale yayimuna yopanda chilema. Aziyipereka pa khomo la tenti ya msonkhano, kuti Yehova alandire.
and of the droue of oxun, he schal offre a male beeste without wem at the dore of the tabernacle of witnessyng, to make the Lord plesid to hym.
4 Munthuyo asanjike dzanja lake pa mutu pa nsembe yopserezayo, ndipo idzalandiridwa kuti ikhale yopepesera machimo ake.
And he schal sette hondis on the heed of the sacrifice, and it schal be acceptable, and profityng in to clensyng of hym.
5 Pambuyo pake aphe ngʼombeyo pamaso pa Yehova, ndipo ansembe, ana a Aaroni, atenge magazi ake ndi kuwawaza mbali zonse za guwa lansembe limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
And he schal offre a calf bifor the Lord, and the sones of Aaron, preestis, schulen offre the blood ther of, and thei schulen schede bi the cumpas of the auter, which is bifor the dore of the tabernacle.
6 Munthuyo asende nsembe yopserezayo ndi kuyidula nthulinthuli.
And whanne the skyn of the sacrifice is drawun awei, thei schulen kitte the membris in to gobetis;
7 Ndipo ana a Aaroni, wansembe uja asonkhe moto pa guwa ndi kuyalapo nkhuni pa motopo.
and thei schulen put vndur in the auter fier, and thei schulen make an heep of wode bifore; and thei schulen ordeyne aboue
8 Kenaka ana a Aaroni, wansembe uja, ayike nthuli za nyamayo, mutu wake pamodzi ndi mafuta omwe pa nkhuni zimene zili paguwapo.
`the trees tho thingis that ben kit, that is, the heed, and alle thingis that cleuen to the mawe,
9 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe awotche nyama yonse paguwapo. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chowotcha pa moto, cha fungo lokomera Yehova.
whanne the entrailis and feet ben waischid with watir; and the preest schal brenne tho on the auter, in to brent sacrifice, and swete odour to the Lord.
10 “‘Koma ngati chopereka cha nsembe yopserezayo ndi nkhosa kapena mbuzi kuchokera pa ziweto zake, munthuyo apereke yayimuna yopanda chilema.
That if the offryng is of litle beestis, a brent sacrifice of scheep, ethir of geet, he schal offre a male beeste with out wem,
11 Ayiphere kumpoto kwa guwa, pamaso pa Yehova, ndipo ana a Aaroni amene ndi ansembe, awaze magazi ake mbali zonse za guwalo.
and he schal offre at the side of the auter that biholdith to the north, bifore the Lord. Sotheli the sones of Aaron schulen schede the blood therof on the auter `bi cumpas,
12 Kenaka ayidule nyamayo nthulinthuli, ndipo wansembe ayike nthulizo pa guwa, atengenso mutu ndi mafuta omwe, ndipo ayike zonsezi pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa.
and thei schulen departe the membris, the heed, and alle thingis that cleuen to the mawe, and thei schulen putte on the trees, vndur whiche the fier schal be set;
13 Munthuyo atsuke zamʼkati mwa nyamayo pamodzi ndi miyendo yake yomwe, ndipo wansembe abwere nazo zonse ndi kuzitentha pa guwa. Iyi ndi nsembe yopsereza, chopereka chotentha pa moto, fungo lokomera Yehova.
sotheli thei schulen waische in watir the entrailis and feet; and the preest schal brenne alle thingis offrid on the auter, in to brent sacrifice, and swettest odour to the Lord.
14 “‘Koma ngati chopereka kwa Yehova ndi nsembe yopsereza ya mbalame, ndiye ikhale njiwa kapena mawunda.
Forsothe if the offryng of brent sacrifice to the Lord is of briddis, of turtlis, and of culuer briddis,
15 Wansembe abwere nayo ku guwa, ayidule mutu moyipotola ndi kutentha mutuwo pa guwa. Magazi ake awathire pansi kuti ayenderere pambali pa guwa.
the preest schal offre it at the auter; and whanne the heed is writhun to the necke, and the place of the wounde is brokun, he schal make the blood renne doun on the brenke of the auter.
16 Iye achotse chithokomiro pamodzi ndi nthenga zake zomwe ndi kuzitaya ku malo wotayirako phulusa, kummawa kwa guwalo.
Sotheli he schal caste forth the litil bladdir of the throte, and fetheris bisidis the auter, at the eest coost, in the place in which the aischis ben wont to be sched out;
17 Kenaka ayingʼambe pakati, koma asachotse mapiko. Ndipo wansembe ayiwotche pa nkhuni zimene zikuyaka pa guwa. Imeneyi ndi nsembe yopsereza, yowotcha pa moto ndiponso ya fungo lokomera Yehova.
and he schal breke the wyngis therof, and he schal not kerue, nether he schal departe it with yrun; and he schal brenne it on the auter, whanne fier is set vndur the trees; it is a brent sacrifice, and an offryng of swete odour to the Lord.

< Levitiko 1 >