< Maliro 4 >

1 Haa! Golide wathimbirira, golide wosalala wasinthikiratu! Amwazamwaza miyala yokongola ya kumalo opatulika pamphambano ponse pa mzinda.
Kako potamnje zlato, promijeni se èisto zlato? kamenje je od svetinje razmetnuto po uglovima svijeh ulica.
2 Haa! Ana a Ziyoni amtengowapatali amene kale anali ngati golide, tsopano ali ngati miphika ya dothi, ntchito ya owumba mbiya!
Dragi sinovi Sionski, cijenjeni kao najèistije zlato, kako se cijene zemljani sudovi, kao djelo ruku lonèarevijeh!
3 Ngakhale nkhandwe zimapereka bere kuyamwitsa ana ake, koma anthu anga asanduka ankhanza ngati nthiwatiwa mʼchipululu.
I zvijeri istièu sise svoje i doje mlad svoju, a kæi naroda mojega posta nemilostiva kao noj u pustinji.
4 Lilime la mwana lakangamira kukhosi chifukwa cha ludzu, ana akupempha chakudya, koma palibe amene akuwapatsa.
Jezik djetetu koje sisa prionu za grlo od žeði; djeca ištu hljeba, a nema nikoga da im lomi.
5 Iwo amene kale ankadya zonona akupemphetsa mʼmisewu ya mu mzinda. Iwo amene kale ankavala zokongola tsopano akugona pa phulusa.
Koji jeðahu poslastice, ginu na ulicama; koji odrastoše u skerletu, valjaju se po bunjištu.
6 Kuyipa kwa anthu anga kunali kwakukulu kuposa anthu a ku Sodomu, amene anawonongedwa mʼkamphindi kochepa popanda owathandiza.
I kar koji dopade kæeri naroda mojega veæi je od propasti koja dopade Sodomu, koji se zatr u èasu i ruke se ne zabaviše oko njega.
7 Akalonga ake anali owala koposa chisanu chowundana ndi oyera kuposa mkaka. Matupi awo anali ofiira kuposa miyala ya rubi, maonekedwe awo ngati miyala ya safiro.
Nazireji njezini bjehu èistiji od snijega, bjelji od mlijeka; tijelo im bješe crvenije od dragoga kamenja, glatki kao safir.
8 Koma tsopano maonekedwe awo ndi akuda kuposa mwaye; palibe angawazindikire mʼmisewu ya mu mzinda. Khungu lawo lachita makwinyamakwinya pa mafupa awo; lawuma gwaa ngati nkhuni.
A sada im je lice crnje od uglja, ne poznaju se na ulicama; koža im se prilijepila za kosti, osušila se kao drvo.
9 Amene anaphedwa ndi lupanga aliko bwino kuposa amene anafa ndi njala; chifukwa chosowa chakudya cha mʼmunda iwowa ankafowoka ndi njala mpaka kufa.
Bolje bi onima koji su pobijeni maèem nego onima koji mru od gladi, koji izdišu ubijeni od nestašice roda zemaljskoga.
10 Amayi achifundo afika pophika ana awo enieni, ndiwo anali chakudya chawo pamene anthu anga anali kuwonongeka.
Svojim rukama žene žalostive kuhaše djecu svoju, ona im biše hrana u pogibli kæeri naroda mojega.
11 Yehova wakwaniritsa ukali wake; wagwetsa pansi mkwiyo wake woopsa. Ndipo wayatsa moto mʼZiyoni kuti uwononge maziko ake.
Navrši Gospod gnjev svoj, izli žestoki gnjev svoj, i raspali oganj na Sionu, koji mu proždrije temelje.
12 Mafumu a pa dziko lapansi sanakhulupirire, kapena wina aliyense wokhala pa dziko lonse, kuti adani kapena ankhondo akhoza kulowa pa zipata za Yerusalemu.
Ne bi vjerovali carevi zemaljski i svi stanovnici po vasiljenoj da æe neprijatelj i protivnik uæi na vrata Jerusalimska.
13 Koma izi zinachitika chifukwa cha kuchimwa kwa aneneri ake ndi mphulupulu za ansembe ake, amene ankapha anthu osalakwa pakati pawo.
Ali bi za grijehe proroka njegovijeh i za bezakonja sveštenika njegovijeh, koji proljevahu krv pravednièku usred njega.
14 Tsopano akungoyendayenda mʼmisewu ya mu mzinda ngati anthu osaona. Iwo ndi odetsedwa kwambiri ndi magazi palibe yemwe angayerekeze nʼkukhudza komwe chovala chawo.
Lutahu kao slijepci po ulicama, kaljajuæi se krvlju, koje ne mogahu da se ne dotièu haljinama svojim.
15 Anthu akuwafuwulira kuti, “Chokani! Inu anthu odetsedwa!” “Chokani! Chokani! Musatikhudze ife!” Akamathawa ndi kumangoyendayenda, pakati pa anthu a mitundu yonse amati, “Asakhalenso ndi ife.”
Otstupite, neèisti, vièu im, otstupite, otstupite, ne dodijevajte se nièega. I odlaze i skitaju se; i meðu narodima se govori: neæe se više staniti.
16 Yehova mwini wake wawabalalitsa; Iye sakuwalabadiranso. Ansembe sakulandira ulemu, akuluakulu sakuwachitira chifundo.
Gnjev Gospodnji rasija ih, neæe više pogledati na njih; ne poštuju sveštenika, nijesu žalostivi na starce.
17 Ndiponso maso athu atopa nʼkuyangʼana, chithandizo chosabwera nʼkomwe, kuchokera pa nsanja zathu tinadikirira mtundu wa anthu umene sukanatipulumutsa.
Veæ nam oèi išèilješe izgledajuæi pomoæ zaludnu; èekasmo narod koji ne može izbaviti.
18 Anthu ankalondola mapazi athu, choncho sitikanayenda mʼmisewu yathu mu mzinda. Chimaliziro chathu chinali pafupi, masiku athu anali owerengeka, chifukwa chimaliziro chathu chinali chitafika.
Vrebaju nam korake, da ne možemo hoditi po ulicama svojim, približi se kraj naš, navršiše se dani naši, doðe kraj naš.
19 Otilondola akuthamanga kwambiri kuposa ziwombankhanga mu mlengalenga; anatithamangitsa mpaka ku mapiri ndi kutibisalira mʼchipululu.
Koji nas goniše, bijahu lakši od orlova nebeskih, po gorama nas goniše, u pustinji nam zasjedaše.
20 Wodzozedwa wa Yehova, mpweya wathu wotipatsa moyo, anakodwa mʼmisampha yawo. Tinaganiza kuti tidzakhala pansi pa mthunzi wake pakati pa mitundu ya anthu.
Disanje nozdara naših, pomazanik Gospodnji, za kojega govorasmo: da æemo živjeti pod sjenom njegovijem meðu narodima, uhvati se u jame njihove.
21 Kondwera ndi kusangalala, mwana wamkazi wa Edomu. Iwe amene umakhala mʼdziko la Uzi. Koma iwenso chikho chidzakupeza; udzaledzera mpaka kukhala maliseche.
Raduj se i veseli se, kæeri Edomska, koja živiš u zemlji Uzu! doæi æe do tebe èaša, opiæeš se, i otkriæeš se.
22 Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, chilango chako chidzatha; Iye sadzatalikitsa nthawi yako ya ukapolo. Koma Yehova adzalanga machimo ako, iwe mwana wamkazi wa Edomu, ndi kuyika poyera mphulupulu zako.
Svrši se kar za bezakonje tvoje, kæeri Sionska; neæe te više voditi u ropstvo; pohodiæe tvoje bezakonje, kæeri Edomska, otkriæe grijehe tvoje.

< Maliro 4 >