< Maliro 3 >

1 Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
Ja sam èovjek koji vidjeh muku od pruta gnjeva njegova.
2 Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
Odvede me i opravi me u tamu a ne na vidjelo.
3 zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
Samo se na me obraæa, obraæa ruku svoju po vas dan.
4 Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
Uèini, te mi ostarje tijelo i koža, potr kosti moje.
5 Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
Zazida me, i optoèi me žuèju i mukom.
6 Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
Posadi me u tamu kao umrle odavna.
7 Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
Ogradi me da ne izaðem, i metnu na me teške okove.
8 Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
Kad vièem i vapijem, odbija molitvu moju.
9 Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
Zagradi putove moje tesanijem kamenom, i prevrati staze moje.
10 Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
Posta mi kao medvjed u zasjedi, kao lav u potaji.
11 Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
Pomete putove moje, i razdrije me, i uništi me.
12 Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
Nateže luk svoj, i metnu me strijeli za biljegu.
13 Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
Ustrijeli me u bubrege strijelama iz tula svojega.
14 Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
Postah potsmijeh svemu narodu svojemu i pjesma njihova po vas dan.
15 Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
Nasiti me gorèinom, opoji me pelenom.
16 Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
Polomi mi zube kamenjem, uvali me u pepeo.
17 Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
Udaljio si dušu moju od mira, zaboravih dobro.
18 Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
I rekoh: propade sila moja i nadanje moje od Gospoda.
19 Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
Opomeni se muke moje i jada mojega, pelena i žuèi.
20 Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
Duša se moja opominje bez prestanka, i poništila se u meni.
21 Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
Ali ovo napominjem srcu svojemu, te se nadam:
22 Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
Milost je Gospodnja što ne izgibosmo sasvijem, jer milosrða njegova nije nestalo.
23 Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
Ponavlja se svako jutro; velika je vjera tvoja.
24 Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
Gospod je dio moj, govori duša moja; zato æu se u njega uzdati.
25 Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
Dobar je Gospod onima koji ga èekaju, duši, koja ga traži.
26 nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
Dobro je mirno èekati spasenje Gospodnje.
27 Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
Dobro je èovjeku nositi jaram za mladosti svoje.
28 Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
Sam æe sjedjeti i muèati, jer Bog metnu breme na nj.
29 Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
Metnuæe usta svoja u prah, eda bi bilo nadanja.
30 Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
Podmetnuæe obraz svoj onome koji ga bije, biæe sit sramote.
31 Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
Jer Gospod ne odbacuje za svagda.
32 Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
Jer ako i ucvijeli, opet æe se i smilovati radi mnoštva milosti svoje.
33 Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
Jer ne muèi iz srca svojega ni cvijeli sinova èovjeèjih.
34 Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
Kad gaze nogama sve sužnje na zemlji,
35 kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
Kad izvræu pravicu èovjeku pred višnjim,
36 kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
Kad èine krivo èovjeku u parnici njegovoj, ne vidi li Gospod?
37 Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
Ko je rekao što i zbilo se, a Gospod da nije zapovjedio?
38 Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
Ne dolaze li i zla i dobra iz usta višnjega?
39 Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
Zašto se tuži èovjek živ, èovjek na kar za grijehe svoje?
40 Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
Pretražimo i razgledajmo pute svoje, i povratimo se ka Gospodu.
41 Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
Podignimo srce svoje i ruke k Bogu na nebesima.
42 “Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
Zgriješismo i nepokorni bismo; ti ne praštaš.
43 “Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
Obastro si se gnjevom, i goniš nas, ubijaš i ne žališ.
44 Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
Obastro si se oblakom da ne prodre molitva.
45 Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
Naèinio si od nas smetlište i odmet usred tijeh naroda.
46 “Adani anthu atitsekulira pakamwa.
Razvaljuju usta svoja na nas svi neprijatelji naši.
47 Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
Strah i jama zadesi nas, pustošenje i zatiranje.
48 Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
Potoci teku iz oèiju mojih radi pogibli kæeri naroda mojega.
49 Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
Oèi moje liju suze bez prestanka, jer nema odmora,
50 mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
Dokle Gospod ne pogleda i ne vidi s neba.
51 Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
Oko moje muèi mi dušu radi svijeh kæeri grada mojega.
52 Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
Tjeraju me jednako kao pticu neprijatelji moji ni za što.
53 Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
Svališe u jamu život moj i nabacaše kamenje na me.
54 madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
Doðe mi voda svrh glave; rekoh: pogiboh!
55 Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
Prizivah ime tvoje, Gospode, iz jame najdublje.
56 Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
Ti èu glas moj; ne zatiskuj uha svojega od uzdisanja mojega, od vike moje.
57 Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
Pristupao si kad te prizivah, i govorio si: ne boj se.
58 Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
Raspravljao si, Gospode, parbu duše moje, i izbavljao si život moj.
59 Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
Vidiš, Gospode, nepravdu koja mi se èini; raspravi parbu moju.
60 Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
Vidiš svu osvetu njihovu, sve što mi misle.
61 Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
Èuješ rug njihov, Gospode, sve što mi misle,
62 manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
Što govore oni koji ustaju na me i što namišljaju protiv mene po vas dan.
63 Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
Vidi, kad sjedaju i kad ustaju, ja sam im pjesma.
64 Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
Plati im, Gospode, po djelima ruku njihovijeh.
65 Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
Podaj im uporno srce, prokletstvo svoje.
66 Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.
Goni ih gnjevom, i istrijebi ih ispod nebesa Gospodnjih.

< Maliro 3 >