< Oweruza 9 >

1 Abimeleki mwana wa Yeru-Baala anapita ku Sekemu kwa abale a amayi ake ndi kukawawuza iwowo ndi fuko lonse la banja la abambo a amayi ake kuti,
I Avimeleh sin Jerovalov otide u Sihem k braæi matere svoje i reèe njima i svemu rodu otaèkoga doma matere svoje govoreæi:
2 “Funsani nzika zonse za ku Sekemu kuno, ‘Chabwino ndi chiyani kwa inu kuti ana onse makumi asanu ndi awiri a Yeru-Baala azikulamulirani, kapena kuti azikulamulirani ndi munthu mmodzi basi?’ Kumbukirani kuti ine ndine mʼbale wanu weniweni.”
Kažite svijem Sihemljanima: šta vam je bolje, da su vam gospodari sedamdeset ljudi, svi sinovi Jerovalovi, ili da vam je gospodar jedan èovjek? I opominjite se da sam ja kost vaša i tijelo vaše.
3 Abale a amayi akewo anamuyankhulira mawu amenewa kwa nzika zonse za ku Sekemu, ndipo mitima ya anthu onse inali pa Abimeleki chifukwa anati, “Uyu ndi mʼbale wathu,”
Tada rekoše braæa matere njegove za nj svijem Sihemljanima sve te rijeèi, i srce njihovo privi se k Avimelehu, jer rekoše: naš je brat.
4 Tsono anamupatsa ndalama zasiliva 70 za mʼnyumba ya chipembedzo ya Baala Beriti. Ndi ndalama zimenezi Abimeleki analemba anthu achabechabe ndi osasamala kuti azimutsatira.
I dadoše mu sedamdeset sikala srebra iz doma Val-Veritova, za koje najmi Avimeleh ljudi praznova i skitnica, te iðahu za njim.
5 Anapita ku Ofiri ku mudzi kwa abambo ake ndipo anapha abale ake makumi asanu ndi awiri, ana a Yeru-Baala pa mwala umodzi. Koma Yotamu yemwe anali wamngʼono mwa onsewo anapulumuka chifukwa anabisala.
I doðe u kuæu oca svojega u Ofru, i pobi braæu svoju, sinove Jerovalove, sedamdeset ljudi, na jednom kamenu; ali osta Jotam najmlaði sin Jerovalov, jer se sakri.
6 Tsono nzika za ku Sekemu ndi za ku Beti-Milo zinapita kukasonkhana ku mtengo wa thundu pafupi ndi chipilala cha ku Sekemu kuti akalonge Abimeleki ufumu.
Tada se skupiše svi Sihemljani i sav dom Milov, i otidoše i postaviše Avimeleha carem kod hrasta koji stoji u Sihemu.
7 Yotamu atamva izi anapita kukayima pamwamba pa phiri la Gerizimu ndipo anafuwula nati, “Tandimverani inu anthu a ku Sekemu, kuti Mulungu akumvereninso.
A kad to javiše Jotamu, otide i stade navrh gore Garizina, i podigavši glas svoj povika i reèe im: èujte me, Sihemljani, tako vas Bog èuo!
8 Tsiku lina mitengo inapita kukadzoza mfumu yawo. Tsono mitengoyo inati kwa mtengo wa olivi, ‘Iwe ukhale mfumu yathu.’”
Išla drveta da pomažu sebi cara, pa rekoše maslini: budi nam car.
9 “Koma mtengo wa olivi uja unayankha kuti, ‘Kodi ndisiye mafuta angawa amene amalemekezera nawo milungu ndi anthu omwe, kuti ndizikalamulira mitengo?’”
A maslina im reèe: zar ja da ostavim pretilinu svoju, kojom se èast èini Bogu i ljudima, pa da idem da tumaram za druga drveta?
10 Apo mitengo inawuza mtengo wa mkuyu kuti, “Bwera ndiwe ukhale mfumu yathu.”
Potom rekoše drveta smokvi: hodi ti, budi nam car.
11 Koma mtengo wa mkuyu unayankha kuti, “Kodi ndisiye chipatso changa chokoma ndi chozunachi kuti ndizikalamulira mitengo?”
A smokva im reèe: zar ja da ostavim slast svoju i krasni rod svoj, pa da idem da tumaram za druga drveta?
12 Kenaka mitengo ija inawuza mtengo wamphesa kuti, “Bwera ndiwe kuti ukhale mfumu yathu.”
Tada rekoše drveta vinovoj lozi: hodi ti, budi nam car.
13 Koma mtengo wamphesa unayankha kuti, “Kodi ine ndisiye vinyo wangayu, amene amasangalatsa milungu ndi anthu omwe kuti ndizikalamulira mitengo?”
A loza im reèe: zar ja da ostavim vino svoje, koje veseli Boga i ljude, pa da idem da tumaram za druga drveta?
14 Pomaliza mitengo yonse inawuza mkandankhuku kuti, “Bwera ndipo ukhale mfumu yathu.”
Tada sva drveta rekoše trnu: hodi ti, budi nam car.
15 Mkandankhuku uja unayankha kuti, “Ngati mukufunadi kuti mudzoze ine kuti ndikhale mfumu yanu, bwerani mudzabisale mu mthunzi mwangamu, koma ngati simutero, moto utuluka kwa ine ndi kupsereza mikungudza ya ku Lebanoni.”
A trn odgovori drvetima: ako doista hoæete mene da pomažete sebi za cara, hodite sklonite se u hlad moj; ako li neæete, neka izide oganj iz trna i spali kedre Livanske.
16 Yotamu anatinso, “Kodi mukuti munaonetsadi kuona mtima ndi kukhulupirika podzoza Abimeleki kukhala mfumu? Kodi mukuti munachitira ulemu Yeru-Baala ndi banja lake poganizira ntchito zimene anachita?
Tako sada, jeste li pravo i pošteno radili postavivši Avimeleha carem? i jeste li dobro uèinili Jerovalu i domu njegovu? i jeste li mu uèinili kako vas je zadužio?
17 Kodi suja abambo anga anakumenyerani nkhondo ndi kuyika moyo wawo pa chiswe kuti akupulumutseni mʼmanja mwa Amidiyani?
Jer je otac moj vojevao za vas i nije mario za život svoj, i izbavio vas je iz ruku Madijanskih.
18 Koma lero inu mwawukira banja la abambo anga. Mwapha ana ake 70 pa mwala umodzi, ndiponso mwalonga ufumu Abimeleki, mwana wa mdzakazi wake kuti akhale wolamulira anthu a ku Sekemu chifukwa ndi mʼbale wanu.
A vi danas ustaste na dom oca mojega, i pobiste sinove njegove, sedamdeset ljudi, na jednom kamenu, i postaviste carem Avimeleha, sina sluškinje njegove, nad Sihemljanima zato što je brat vaš.
19 Tsono ngati mukuti zimene mwachitira Yeru-Baala ndi banja lake mwazichita moona mtima ndiponso mokhulupirika, ndiye mukondwere ndi Abimeleki, nayenso akondwere nanu!
Ako ste pravo i pošteno radili danas prema Jerovalu i njegovu domu, veselite se s Avimeleha i on neka se veseli s vas.
20 Koma ngati sichoncho moto utuluke mwa Abimeleki ndi kupsereza anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndipo moto utulukenso mwa anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndi kupsereza Abimeleki!”
Ako li nijeste, neka izide oganj od Avimeleha i spali Sihemljane i dom Milov, i neka izide oganj od Sihemljana i od doma Milova i spali Avimeleha.
21 Kenaka Yotamu anathawira ku Beeri nakakhala komweko chifukwa ankaopa Abimeleki mʼbale wake.
Tada pobježe Jotam, i pobjegav doðe u Vir, i ondje osta bojeæi se Avimeleha brata svojega.
22 Abimeleki atalamulira Israeli zaka zitatu,
I vlada Avimeleh Izrailjem tri godine.
23 Mulungu anayika chidani pakati pa Abimelekiyo ndi anthu a ku Sekemu, motero kuti anthu a ku Sekemu anawukira Abimeleki.
Ali Bog pusti zlu volju meðu Avimeleha i meðu Sihemljane; i Sihemljani iznevjeriše Avimeleha,
24 Mulungu anachita zimenezi kuti zoyipa zimene anachitira ana aamuna 70 a Yeru-Baala aja zimubwerere, ndi kuti magazi awo akhale pa Abimeleki mʼbale wawo ndi pa anthu a ku Sekemu amene anamulimbikitsa mtima kuti aphe abale akewo.
Da bi se osvetila nepravda uèinjena na sedamdeset sinova Jerovalovijeh, i krv njihova da bi došla na Avimeleha brata njihova, koji ih ubi, i na Sihemljane, koji ukrijepiše ruku njegovu da ubije braæu svoju.
25 Choncho anthu a ku Sekemu anayika anthu omubisalira pamwamba pa mapiri. Tsono iwo ankalanda anthu odutsa mʼnjira imeneyo zinthu zawo ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
I Sihemljani pometaše mu zasjede po vrhovima gorskim, pa plijenjahu sve koji prolažahu mimo njih onijem putem. I bi javljeno Avimelehu.
26 Gaali mwana wa Ebedi anasamukira ku Sekemu ndi abale ake, ndipo anthu a ku Sekemuko anamukhulupirira iye.
Potom doðe Gal sin Evedov sa svojom braæom, i uljezoše u Sihem, i Sihemljani se pouzdaše u nj.
27 Anthuwo anapita ku munda kukathyola mphesa ndi kuzifinya, ndipo anachita chikondwerero mʼnyumba ya milungu yawo. Anthuwo akudya ndi kumwa, ankatemberera Abimeleki.
I izašavši u polje braše vinograde svoje i gaziše grožðe, i veseliše se; i uðoše u kuæu boga svojega, i jedoše i piše, i psovaše Avimeleha.
28 Ndipo Gaali mwana wa Ebedi anati “Kodi Abimeleki ndi ndani, ndipo nʼchifukwa chiyani akutilamulira ife Asekemu? Kodi iyeyu si mwana wa Yeru-Baala ndipo womuthandiza wake si Zebuli? Tiyeni titumikire anthu a ku Hamori, kholo la fuko la Sekemu! Nanga nʼchifukwa chiyani tikutumikira Abimeleki?
I Gal sin Evedov reèe: ko je Avimeleh i šta je Sihem, da mu služimo? Nije li sin Jerovalov? a Zevul nije li njegov pristav? Služite sinovima Emora oca Sihemova. A što bismo služili tomu?
29 Anthu a mu mzindawo akanakhala pansi pa ulamuliro wanga, ndikanamuchotsa Abimelekiyu. Ndikanamuwuza Abimeleki kuti, ‘Wonjeza ankhondo ako ndipo ubwere tidzamenyane!’”
O kad bi taj narod bio pod mojom rukom, da smetnem Avimeleha! I reèe Avimelehu: prikupi vojsku svoju, i izidi.
30 Zebuli amene ankalamulira mzindawo atamva zimene Gaali mwana wa Ebadi ananena, anakwiya kwambiri.
A kad èu Zevul, upravitelj gradski, rijeèi Gala sina Evedova, razgnjevi se vrlo.
31 Anatumiza amithenga kwa Abimeleki, kukanena kuti, “Gaali mwana wa Ebedi ndi abale ake abwera ku Sekemu ndipo akuwutsa mitima ya anthu a mu mzindawo kuti akuwukireni inu.
I posla tajno poslanike k Avimelehu i poruèi mu: evo Gal sin Evedov i braæa mu doðoše u Sihem, i evo pobuniše grad na te.
32 Nʼchifukwa chake usiku womwe uno inu ndi anthu anu mupite, mukabisale mʼminda.
Nego ustani noæu ti i narod što je s tobom, i zasjedi u polju.
33 Mmawa dzuwa likutuluka, mudzuke ndi kukathira nkhondo mzindawo. Gaali ndi anthu amene ali naye akamadzabwera kuti alimbane ndi inu, inu mudzathane nawo monga mmene mungachitire.”
A ujutru kad sunce ograne, digni se i udari na grad; i evo on i narod koji je s njim izaæi æe preda te, pa uèini s njim što ti može ruka.
34 Choncho Abimeleki ndi ankhondo ake onse anadzuka usiku nakabisalira mzinda wa Sekemu mʼmagulu anayi.
I Avimeleh usta noæu i sav narod što bješe s njim; i zasjedoše Sihemu u èetiri èete.
35 Gaali mwana wa Ebedi anatuluka nakayima pa khomo pa chipata cha mzinda pamene Abimeleki ndi ankhondo ake anatuluka ku malo kumene anabisala kuja.
A Gal sin Evedov izide i stade pred vratima gradskim; a Avimeleh i narod što bješe s njim izide iz zasjede.
36 Gaaliyo atawaona, anawuza Zebuli kuti, “Taona anthu akutsika kuchoka pamwamba pa mapiri.” Koma Zebuli anayankha kuti, “Zimene mukuonazo ndi zithunzi za mapiri chabe osati anthu.”
A Gal vidjev narod reèe Zevulu: eno narod slazi svrh gore. A Zevul mu odgovori: od sjena gorskoga èine ti se ljudi.
37 Koma Gaaliyo anayankhulanso kuti, “Taona anthu akutsika kuchokera pakati pa phiri, ndipo gulu lina likubwera kuchokera ku mtengo wa thundu wa owombeza mawula.”
Opet progovori Gal i reèe: eno narod slazi s visa, i èeta jedna ide putem k šumi Meonenimskoj.
38 Ndipo Zebuli anamufunsa iye kuti, “Pakamwa pako paja pali kuti tsopano, iwe amene umanena kuti, Abimeleki ndaninso kuti ife timutumikire? Kodi amenewa si anthu aja umawanyozawa? Tsopano tuluka ukamenyane nawo.”
A Zevul mu reèe: gdje su ti sada usta, kojima si govorio: ko je Avimeleh da mu služimo? Nije li to onaj narod koji si prezirao? Izidi sada, i bij se s njim.
39 Choncho Gaaliyo anatuluka akutsogolera anthu a ku Sekemu kukamenyana ndi Abimeleki.
I izide Gal pred Sihemljanima, i pobi se s Avimelehom.
40 Koma Abimeleki anamuthamangitsa ndipo Gaala anathawa. Ambiri a ankhondo ake anagwa napwetekeka njira yonse mpaka ku chipata cha mzinda.
Ali Avimeleh ga potjera, i on pobježe od njega; i padoše mnogi pobijeni do samijeh vrata gradskih.
41 Abimeleki anakhala ku Aruma, ndipo Zebuli anathamangitsa Gaali pamodzi ndi abale ake, kuwatulutsa mu Sekemu.
I Avimeleh osta u Arumi; a Zevul istjera Gala i braæu njegovu, te ne mogahu sjedeti u Sihemu.
42 Mmawa mwake anthu a ku Sekemu anapangana zopita ku minda, ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
A sjutradan izide narod u polje, i bi javljeno Avimelehu.
43 Tsono Abimeleki anatenga anthu ake, nawagawa magulu atatu ndi kukabisala mʼminda. Ataona anthu akutuluka mu mzindawo, iye anapita kukalimbana nawo ndipo onsewo anawapha.
A on uze narod svoj i razdijeli ga u tri èete, i namjesti ih u zasjedu u polju; i kad vidje gdje narod izlazi iz grada, skoèi na njih i pobi ih.
44 Abimeleki pamodzi ndi magulu ake anathamangira kutsogolo nakawakhalira pa chipata cha mzinda. Ndipo magulu awiri ena aja anathamangira anthu amene anali mʼminda ndi kuwapha onse.
Jer Avimeleh i èeta koja bijaše s njim udariše i stadoše kod vrata gradskih; a druge dvije èete udariše na sve one koji bijahu u polju, i pobiše ih.
45 Abimeleki anawuthira nkhondo mzindawo tsiku lonse. Kenaka anawulanda ndi kupha nzika zonse za mu mzindamo. Anawuwonongeratu mzindawo nawuwaza mchere.
I Avimeleh bijaše grad vas onaj dan, i uze ga, i pobi narod koji bješe u njemu, i raskopa grad, i posija so po njemu.
46 Anthu a mu nsanja ya Sekemu atamva zimenezi, anakalowa mu linga la nyumba yopembedzeramo Baala-Beriti.
A kad to èuše koji bijahu u kuli Sihemskoj, uðoše u kulu kuæe boga Verita.
47 Abimeleki anamva kuti anthu ena asonkhana kumeneko.
I bi javljeno Avimelehu da su se ondje skupili svi koji bijahu u kuli Sihemskoj.
48 Choncho Abimeleki pamodzi ndi anthu ake onse anapita ku phiri la Zalimoni. Kumeneko anatenga nkhwangwa nadula nthambi za mitengo. Ananyamula nthambi zija pa phewa pake. Tsono anawuza anthu aja kuti, “Zimene mwaona ine ndikuchita, inunso mufulumire kuchita monga ndachitiramu.”
Tada Avimeleh izide na goru Salmon, on i sav narod što bješe s njim; i uzev Avimeleh sjekiru u ruku otsijeèe granu od drveta i podiže je i metnu je na rame, i reèe narodu koji bijaše s njim: što vidjeste da sam ja uèinio, brzo èinite kao ja.
49 Tsono aliyense anadula nthambi zake, natsatira Abimeleki. Anakawunjika nthambi zija pa linga paja, kenaka ndi kuliyatsa moto. Choncho anthu onse a ku nsanja ya Sekemu anafa. Analipo anthu pafupifupi 1,000, amuna ndi akazi.
I svaki iz naroda otsijeèe sebi granu, i poðoše za Avimelehom i pometaše grane oko kule, i zapališe njima grad; i izgiboše svi koji bijahu u kuli Sihemskoj, oko tisuæu ljudi i žena.
50 Kenaka Abimeleki anapita ku Tebezi. Anakawuzungulira mzindawo ndi kuwulanda.
Potom otide Avimeleh na Teves, i stade u oko kod Tevesa, i uze ga.
51 Koma mu mzindamo munali nsanja yolimba. Anthu onse a mu mzindamo amuna ndi akazi anathawira mu nsanjayo, nadzitsekera mʼkati. Ndipo anakwera ku denga la nsanjayo.
A bijaše tvrda kula usred grada, i u nju pobjegoše svi ljudi i žene i svi graðani, i zatvorivši se popeše se na krov od kule.
52 Abimeleki anapita ku nsanjayo nathira nkhondo. Anafika pafupi ndi chitseko cha nsanja ija kuti ayitenthe.
A Avimeleh doðe do kule i udari na nju, i doðe do vrata od kule da je zapali ognjem.
53 Koma mkazi wina anaponya mwala wa mphero pa mutu wa Abimeleki ndi kuswa chibade cha mutuwo.
Ali jedna žena baci komad žrvnja na glavu Avimelehu i razbi mu glavu.
54 Mwamsanga Abimeleki anayitana mnyamata womunyamulira zida za nkhondo namuwuza kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuti anthu asadzanene kuti, ‘Mkazi ndiye anamupha.’” Choncho wantchito wake anamubayadi mpaka kutulukira kunja lupangalo ndipo anafa.
A on brže viknu momka koji mu nošaše oružje, i reèe mu: izvadi maè svoj i ubij me, da ne reku za me: žena ga je ubila. I probode ga sluga njegov, te umrije.
55 Aisraeli ataona kuti Abimeleki wafa, anapita kwawo.
A kad vidješe Izrailjci gdje pogibe Avimeleh, otidoše svaki u svoje mjesto.
56 Mmenemu ndi mmene Mulungu analipsirira tchimo la Abimeleki limene anachitira abambo ake pakupha abale ake 70 aja.
Tako plati Bog Avimelehu za zlo koje je uèinio ocu svojemu ubivši sedamdeset braæe svoje.
57 Mulungu anawalanganso anthu a ku Sekemu chifukwa cha kuyipa kwawo konse. Ndipo matemberero a Yotamu mwana wa Yeru-Baala anawagweradi.
I sve zlo ljudi Sihemljana povrati Bog na njihove glave, i steèe im se kletva Jotama sina Jerovalova.

< Oweruza 9 >