< Oweruza 7 >

1 Yeru-Baala (Gideoni) ndi anthu ake onse anadzuka mʼmamawa nakamanga misasa pambali pa kasupe ku Harodi. Misasa ya Amidiyani inali mʼchigwa kumpoto kwa phiri la More.
Therfor Jerobaal, which also Gedeon, roos bi nyyt, and al the puple with hym, and cam to the welle which is clepid Arad. Sotheli the tentis of Madian weren in the valey, at the north coost of the hiy hil.
2 Yehova anati kwa Gideoni, “Anthu uli nawowa andichulukira kwambiri kuti ndigonjetse Amidiyani chifukwa Aisraeli angamadzitukumule pamaso panga ndi kumanena kuti, ‘Tadzipulumutsa ndi mphamvu zathu.’
And the Lord seide to Gedeon, Myche puple is with thee, and Madian schal not be bitakun in to the hondis `ther of, lest Israel haue glorie ayens me, and seie, Y am delyuerid bi my strengthis.
3 Tsono lengeza kwa anthu kuti, ‘Aliyense amene akuchita mantha ndi kunjenjemera abwerere kwawo, ndipo achoke kuno ku phiri la Giliyadi.’” Choncho anthu 22,000 anachoka, ndipo anatsalira anthu 10,000.
Speke thou to the puple, and preche thou, while alle men heren, He that is ferdful `in herte, and dredeful `with outforth, turne ayen. And thei yeden awei fro the hil of Galaad, and two and twenti thousynde of men turniden ayen fro the puple; and oneli ten thousynde dwelliden.
4 Koma Yehova anawuza Gideoni kuti, “Anthuwa achulukabe. Uwatenge upite nawo ku mtsinje ndipo ndikawayesa kumeneko mʼmalo mwako. Ndikadzanena kuti, ‘Uyu apite nawe’ adzapita nawe; koma ndikanena kuti ‘Uyu asapite nawe,’ sadzapita nawe.”
And the Lord seide to Gedeon, Yet the puple is myche; lede thou hem to the watris, and there Y schal preue hem, and he go, of whom Y schal seye, that he go; turne he ayen, whom Y schal forbede to go.
5 Choncho Gideoni anatenga anthuwo ndi kupita nawo ku madzi. Kumeneko Yehova anamuwuza kuti, “Amene amwe madzi mokhathira ndi manja ngati galu uwayike pawokha, ndipo amene amwe atagwada pansi uwayikenso pawokha.”
And whanne the puple hadde go doun to watris, the Lord seide to Gedeon, Thou schalt departe hem bi hem silf, that lapen watris with hond and tunge, as doggis ben wont to lape; sotheli thei, that drynken with knees bowid, schulen be in the tothir part.
6 Ndipo anthu 300 anamwa mokhathira, pamene ena onse anagwada pansi pakumwa.
And so the noumbre of hem, that lapiden watris bi hond castynge to the mouth, was thre hundrid men; forsothe al the tothir multitude drank knelynge.
7 Yehova anati kwa Gideoni, “Ndi anthu 300 amene anamwa madzi mokhathira ndi manja awo ndidzakupulumutsani ndipo ndidzapereka Amidiyani mʼmanja mwanu. Koma anthu ena onse apite ku nyumba kwawo.”
And the Lord seide to Gedeon, In thre hundrid men, that lapiden watris, Y schal delyuere you, and Y schal bitake Madian in thin hond; but al the tothir multitude turne ayen in to her place.
8 Choncho analola anthu ena onse kuti apite ku nyumba zawo kupatula anthu 300 osankhika aja. Iwowa anatenga zakudya ndi malipenga a anthuwo. Ndipo misasa ya ankhondo Amidiyani inali kumunsi kwa chigwa.
And so whanne thei hadden take meetis and trumpis for the noumbre, he comaundide al the tothir multitude to go to her tabernaclis; and he, with thre hundrid men, yaf hym silf to batel. Sothely the tentis of Madian weren bynethe in the valey.
9 Usiku umenewo Yehova anati kwa Gideoni, “Dzuka, pita kachite nkhondo ku misasayo, chifukwa ndayipereka mʼmanja mwako.
In the same nyyt the Lord seyde to hym, Ryse thou, and go doun in to `the castels of Madian, for Y haue bitake hem in thin hond;
10 Ngati ukuopa, upite ku msasako ndi Pura wantchito wako,
sotheli if thou dredist to go aloon, Phara, thi child, go doun with thee.
11 ndipo ukamvere zimene akunena ndipo pambuyo pake udzalimba mtima ndi kupita kukayithira nkhondo misasayo.” Choncho iye ndi wantchito wake Pura anapita kumbali ina ya msasawo kumene kunali ankhondo.
And whanne thou schalt here what thei speken, thanne thin hondis schulen be coumfortid, and thou schalt do down sikerere to the tentis of enemyes. Therfor he yede doun, and Phara, his child, in to the part of tentis, where the watchis of armed men weren.
12 Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena onse akummawa anadzaza chigwa chonse ngati dzombe. Ngamira zawo zinali zambiri zosawerengeka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
Forsothe Madian, and Amalech, and alle the puplis of the eest layen spred in the valey, as the multitude of locustis; sotheli the camelis weren vnnoumbrable, as grauel that liggith in the `brenke of the see.
13 Gideoni atafika anangomva munthu wina akuwuza mnzake maloto ake kuti, “Ine ndinalota nditaona dengu la buledi wa barele likugubuduzika kupita ku misasa ya Amidiyani. Litafika linawomba tenti moti inagwa ndi kuphwasukaphwasuka.”
And whanne Gedeon hadde come, a man tolde a dreem to his neiybore, and telde bi this maner that, that he hadde seyn, I siy a dreem, and it semyde to me, that as `o loof of barly bakun vndur the aischis was walewid, and cam doun in to the tentis of Madian; and whanne it hadde come to a tabernacle, it smoot and distriede `that tabernacle, and made euene outirly to the erthe.
14 Ndipo mnzakeyo anamuyankha kuti, “Iyi ndi nkhondo ya Gideoni mwana wa Yowasi, wa ku Israeli. Mulungu wapereka Amidiyani pamodzi ndi ankhondo ake onse mʼdzanja mwake.”
That man answeride, to whom he spak, This is noon other thing, no but the swerd of Gedeon, `sone of Joas, a man of Israel; for the Lord hath bitake Madian and alle `tentis therof in to the hondis of Gedeon.
15 Gideoni atamva za malotowo ndi kumasulira kwake, anapembedza Mulungu. Kenaka anabwerera ku msasa wa Israeli nawawuza kuti, “Dzukani popeza Yehova wapereka msasa wa Midiyani mʼmanja mwanu.”
And whanne Gedeon had herd the dreem, and `the interpretyng therof, he worschypide the Lord, and turnede ayen to the tentis of Israel, and seide, Ryse ye; for the Lord hath bitake in to oure hondis the tentis of Madian.
16 Anawagawa anthu 300 aja magulu atatu, nawapatsa malipenga mʼmanja mwawo ndi mbiya zimene mʼkati mwake munali nsakali zoyaka.
And he departide thre hundrid men in to thre partis, and he yaf trumpis in her hondis, and voyde pottis, and laumpis in the myddis of the pottis.
17 Anawuza anthuwo kuti, “Muzikayangʼana ine ndi kuchita zimene ndizikachita. Ndikakafika kumalire a msasa, mukachite zomwe ndikachita ine.
And he seide to hem, Do ye this thing which ye seen me do; Y schal entre in to a part of the tentis, and sue ye that, that Y do.
18 Ndikadzaliza lipenga ndi onse amene ali ndi ine, inunso mukalize malipenga kumbali zonse za misasa yonse ndi kufuwula kuti, ‘Lupanga la Yehova ndi la Gideoni.’”
Whanne the trumpe in myn hond schal sowne, sowne ye also `bi the cumpas of tentis, and crye ye togidere, To the Lord and to Gedeon.
19 Choncho Gideoni pamodzi ndi amuna 100 omwe anali nawo anafika ku malire a msasa pakati pa usiku, alonda atangosinthana kumene. Iwo analiza malipenga awo ndi kuphwanya mbiya zimene zinali mʼmanja mwawo.
And Gedeon entride, and thre hundrid men that weren with hym, `in to a part of the tentis, whanne the watchis of mydnyyt bigunnen; and whanne the keperis weren reysid, thei bigunnen to sowne with trumpis, and to bete togidere the pottis among hem silf.
20 Magulu awiri ena aja anayimbanso malipenga ndi kuswa mbiya zawo. Aliyense ananyamula nsakali ya moto ku dzanja lamanzere ndi lipenga ku dzanja lamanja ndipo anafuwula kuti, “Lupanga la Yehova ndi la Gideoni.”
And whanne thei sowneden in thre places bi cumpas, and hadden broke the pottis, thei helden laumpis in the left hondis, and sownynge trumpis in the riyt hondis; and thei crieden, The swerd of the Lord and of Gedeon; and stoden alle in her place,
21 Aliyense anayima pa malo pake kuzungulira misasa. Ankhondo a mʼmisasa muja anadzuka nayamba kuthawa akufuwula.
`bi the cumpas of the tentis of enemyes. And so alle `the tentis weren troblid; and thei crieden, and yelliden, and fledden;
22 Anthu 300 aja ataliza malipenga, Yehova anawasokoneza ankhondo a Midiyani aja motero kuti ankamenyana okhaokha. Ankhondowo anathawira ku Beti-Sita cha ku Zerera mpaka ku malire a Abeli-Mehola pafupi ndi Tabati.
and neuertheles the thre hundrid men contynueden, sownynge with trumpis. And the Lord sente swerd in alle the castels, and thei killiden hem silf bi deeth ech other;
23 Aisraeli a fuko la Nafutali, fuko la Aseri, ndi fuko lonse la Manase anayitanidwa, ndipo iwo anathamangitsa Amidiyaniwo.
and thei fledden `til to Bethsecha, and bi the side, fro Elmonla in to Thebbath. Sotheli men of Israel crieden togidere, of Neptalym, and of Aser, and of alle Manasses, and pursueden Madian; and the Lord yaf victorie to the puple of Israel in that day.
24 Gideoni anatumiza amithenga ku dziko lonse la ku mapiri la Efereimu kukanena kuti, “Tsikani mumenyane ndi Amidiyani ndipo mulande madooko awo owolokera mpaka ku Beti-Bara.” Choncho anthu onse a fuko la Efereimu anasonkhana ndipo analanda madooko awo owolokera mpaka ku Betibaala.
And Gedeon sente messangeris in to al the hil of Effraym, and seide, Come ye doun ayens the comyng of Madian, and ocupie ye the watris `til to Bethbera and Jordan. And al Effraym criede, and bifore ocupide the watris and Jordan `til to Bethbera.
25 Iwo anagwiranso atsogoleri awiri a nkhondo a Amidiyani, Orebu ndi Zeebu. Anapha Orebu ku thanthwe la Orebu, koma Zeebu anamuphera ku malo ofinyira mphesa ku Zeebu pothamangitsa Amidiyani. Mitu ya Orebu ndi Zeebu anabwera nayo kwa Gideoni kutsidya kwa Yorodani.
And Effraym killide twei men of Madian, Oreb and Zeb; he killide Oreb in the ston of Oreb, forsothe `he killide Zeb in the pressour of Zeb; and `thei pursueden Madian, and baren the heedis of Oreb and of Zeb to Gedeon, ouer the flodis of Jordan.

< Oweruza 7 >