< Oweruza 6 >

1 Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, choncho Yehova anawapereka mʼmanja mwa Amidiyani kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
Forsothe the sones of Israel diden yuel in the `siyt of the Lord, and he bitook hem in the hond of Madian seuene yeer.
2 Amidiyani anapondereza Aisraeli. Tsono chifukwa cha Amidiyaniwa, Aisraeli anakonza malo obisalamo mʼmapiri ndi mʼmapanga. Anamanganso malinga.
And thei weren oppressid of hem greetly; and `thei maden dichis, and dennes to hem silf in hillis, and strongeste places to fiyte ayen.
3 Aisraeli amati akadzala mbewu, Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena akummawa amabwera ndi kudzawathira nkhondo.
And whanne Israel hadde sowe, Madian stiede, and Amalech, and othere of the `naciouns of the eest;
4 Iwo anamanga misasa mʼdzikomo ndi kuwononga zokolola zawo zonse mpaka ku Gaza, ndipo sanawasiyireko chamoyo chilichonse Aisraeliwo, kaya nkhosa kapena ngʼombe ndi bulu yemwe.
and thei settiden tentis at the sones of Israel, and wastiden alle thingis `as tho weren in eerbis, ethir grene corn, `til to the entryng of Gaza, and outirli thei leften not in Israel ony thing perteynynge to lijf, not scheep, not oxun, not assis.
5 Iwo ankabwera ndi zoweta zawo ndi matenti awo omwe. Ankabwera ambiri ngati dzombe, motero kuti kunali kovuta kuwawerenga anthuwo ndi ngamira zawo. Tsono iwo ankabwera ndi kuwononga dziko lonse.
For thei and alle her flockis camen with her tabernaclis, and at the licnesse of locustus thei filliden alle thingis, and a multitude of men and of camels was with out noumbre, and wastiden what euer thing thei touchiden.
6 Aisraeli anasauka chifukwa cha Amidiyani ndipo analirira kwa Yehova kuti awathandize.
And Israel was `maad low greetli in the siyt of Madian.
7 Pamene Aisraeli analirira kwa Yehova chifukwa cha Amidiyaniwo,
And Israel criede to the Lord, `and axyde help ayens Madianytis; and he sente to hem a man,
8 Iye anawatumizira mneneri amene anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndine amene ndinakutsogolerani kuchokera ku Igupto. Ndinakutulutsani mʼdziko la ukapolo.
a profete, and he spak, The Lord God of Israel seith these thingis, Y made you to stie fro Egipt, and Y ledde you out of the hows of seruage,
9 Ine ndinakupulumutsani ku ulamuliro wa Igupto komanso mʼmanja mwa amene amakuzunzani. Ndinawathamangitsa adani anu inu mukufika, ndikukupatsani dziko lawo.’
and Y delyueride you fro the hond of Egipcians, and of alle enemyes that turmentiden you; and Y castide hem out at youre entryng, and Y yaf to you `the lond of hem;
10 Ndipo ndinakuwuzani kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu; musapembedze Milungu ya Aamori amene mukukhala mʼdziko lawo.’ Koma inu simunandimvere.”
and Y seide, Y am `youre Lord God; drede ye not the goddis of Ammorreis, in whose lond ye dwellen; and ye nolden here my vois.
11 Tsiku lina mngelo wa Yehova anabwera ku Ofura ndi kukhala pansi pa tsinde pa mtengo wa thundu umene unali wa Yowasi Mwabiezeri. Tsono Gideoni, mwana wake nʼkuti pa nthawiyo akupuntha tirigu mʼmalo ofinyira mphesa mowabisalira Amidiyani.
Forsothe an aungel of the Lord cam, and sat undur an ook, that was in Effra, and perteynede to Joas, fadir of the meinee of Ezri. And whanne Gedeon, `his sone, threischide out, and purgide wheetis in a pressour,
12 Tsono mngelo wa Yehova uja anamuonekera Gideoni nati kwa iye, “Yehova ali nawe, iwe munthu wamphamvu ndi wolimba mtima.”
that he schulde fle Madian, an aungel of the Lord apperide to hym, and seide, The Lord be with thee, thou strongeste of men.
13 Gideoni anayankha, “Koma mbuye wanga, ngati Yehova ali nafedi, nʼchifukwa chiyani zonsezi zationekera? Nanga ntchito zake zodabwitsa zimene makolo athu anatiwuza pamene anati, ‘Yehova anatitulutsa ku dziko la Igupto,’ zili kuti? Koma tsopano Yehova watitaya ndi kutipereka mʼmanja mwa Amidiyani.”
And Gedeon seide to hym, My lord, Y biseche, if the Lord is with vs, whi therfor han alle these yuels take vs? Where ben the merueils of hym, whiche oure fadris telden, and seiden, The Lord ledde vs out of Egipt? `Now forsothe he hath forsake vs, and hath bitake vs in the hond of Madian.
14 Yehova anamuyangʼana namuwuza kuti, “Pita ndi mphamvu zomwe uli nazo, ukapulumutse Aisraeli mʼmanja mwa Amidiyani. Kodi si ndine amene ndakutuma?”
And the Lord bihelde to hym, and seide, Go thou in this strengthe of thee, and thou schalt delyuere Israel fro the hond of Madian; wite thou, that Y sente thee.
15 Koma Gideoni anafunsa kuti, “Kodi Ambuye anga ine ndingapulumutse bwanji Israeli? Mbumba yanga ndi yopanda mphamvu mu fuko la Manase, ndiponso ine ndine wamngʼono kwambiri mʼbanja mwa abambo anga.”
Which Gedeon answeride, and seide, My lord, Y biseche, in what thing schal Y delyuere Israel? Lo! my meynee is the loweste in Manasses, and Y am the leeste in the hows of my fadir.
16 Yehova anamuyankha kuti, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo Amidiyaniwo udzawagonjetsa ngati munthu mmodzi.”
And the Lord seide to hym, Y schal be with thee, and thou schalt smyte Madian as o man.
17 Gideoni anati, “Ngati tsopano mwandikomera mtima, ndionetseni chizindikiro kusonyeza kuti ndinudi mukuyankhula ndi ine.
And Gedeon seide, If Y haue foundun grace bifor thee, yyue to me a signe, that thou, that spekist to me, art sente of Goddis part;
18 Chonde musachoke msanga mpaka nditabwerera kwa inu ndi chopereka changa cha chakudya kudzachipereka kwa inu.” Ndipo Yehova anamuwuza kuti, “Ine ndikudikira mpaka utabweranso.”
go thou not `awei fro hennus, til Y turne ayen to thee, and brynge sacrifice, and offre to thee. Whiche answeride, Y schal abide thi comyng.
19 Gideoni analowa mʼnyumba, ndipo anakakonza mwana wambuzi, nakonzanso makeke wopanda yisiti a ufa wa makilogalamu khumi. Nayika nyamayo mʼdengu ndipo msuzi wake anawuthira mu mʼphika. Anabwera nazo ndi kukazipereka kwa mngelo uja pa tsinde pa mtengo wa thundu paja.
And so Gedeon entride, and sethide a kide, and took therf looues of a buyschel of mell, and fleischis in a panyere; and he sente the broth of fleischis in a pot, and bar alle thingis vndur an ook, and offride to hym.
20 Mngelo wa Mulungu anamuwuza iye kuti, “Tenga nyamayi pamodzi ndi makekewa, uziyike pa mwala uwu ndi kuthirapo msuziwu.” Ndipo Gideoni anatero.
To whom the aungel of the Lord seide, Take thou the fleischis, and therf looues, and putte on that stoon, and schede the broth aboue. And whanne he hadde do so,
21 Mngelo wa Yehova anatenga msonga ya ndodo imene inali mʼmanja mwake nakhudza nayo nyama ndi makeke aja. Nthawi yomweyo moto unabuka pa thanthwepo ndi kupsereza nyama yonse ndi makeke aja. Ndipo mngelo wa Yehova sanaonekenso.
the aungel of the Lord helde forth the `ende of the yerde which he helde in the hond, and he touchide the fleischis, and the therf looues; and fier stiede fro the stoon, and wastide the fleischis, and therf looues. Forsothe the aungel of the Lord vanyschide fro hise iyen.
22 Apo Gideoni anazindikira kuti analidi mngelo wa Ambuye, ndipo anati, “Kalanga ine Yehova Wamphamvuzonse! Ine ndaona mngelo wa Yehova ndi maso!”
And Gedeon siy that he was `an aungel of the Lord, and seide, Lord God, alas to me, for Y siy the aungel of the Lord face to face.
23 Koma Yehova anamuwuza kuti, “Mtendere ukhale ndi iwe! Usachite mantha, sufa ayi.”
And the Lord seide to hym, Pees be with thee; drede thou not, thou schalt not die.
24 Choncho Gideoni anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo analitcha kuti, Yehova ndiye mtendere. Kufikira lero lino guwali lilipo ku Ofura wa Mwabiezeri.
Therfor Gedeon bildide there an auter to the Lord, and he clepide it the Pees of the Lord, `til in to present dai. And whanne he was yit in Effra, which is of the meynee of Ezri, the Lord seide to hym in that nyyt,
25 Usiku womwewo Yehova anati kwa Gideoni, “Tenga ngʼombe ya mphongo ya abambo ako, ngʼombe ina yachiwiri ya zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ugwetse guwa la Baala limene abambo ako ali nalo, ndi kugwetsanso fano la Asera limene lili pafupi pake.
Take thou `the bole of thy fadir, and anothir bole of seuene yeer, and thou schalt distrie the auter of Baal, which is thi fadris, and kitte thou doun the wode, which is aboute the auter;
26 Kenaka umangire Yehova Mulungu wako guwa lansembe ndi miyala yoyala bwino pamwamba pa chiwunda chimenecho. Utenge ngʼombe ya mphongo yachiwiri ija ndipo uyipereke ngati nsembe yopsereza pogwiritsa ntchito mitengo ya fano la Asera imene udule ngati nkhunizo.”
and thou schalt bilde an auter to thi Lord God in the hiynesse of this stoon, on which thou puttidist sacrifice bifore; and thou schalt take the secounde bole, and thou schalt offre brent sacrifice on the heep of trees, whiche thou kittidist doun of the wode.
27 Choncho Gideoni anatenga antchito ake khumi nachita monga Yehova anamuwuzira. Ndipo popeza ankaopa anthu a pa banja lake ndiponso anthu a mʼmudzimo sanachite zimenezi masana koma usiku.
Therfore Gedeon took ten men of hise seruauntis, and dide as the Lord comaundide to hym. Sotheli Gedeon dredde the hows of his fadir, and the men of that citee, and nolde do bi dai, but fillide alle thingis bi nyyt.
28 Anthu a mu mzindamo atadzuka mʼmamawa anangoona guwa la Baala litagwetsedwa ndi fano la Asera limene linali pamwamba pake litadulidwa ndiponso ngʼombe yamphongo yachiwiri ija itaperekedwa ngati nsembe yopsereza pa guwa limene linamangidwa lija.
And whanne men of that citee hadde rise eerly, thei sien the auter of Baal distried, and the wode kit doun, and the tothir bole put on the auter, that was bildid thanne.
29 Iwo anafunsana wina ndi mnzake, “Wachita zimenezi ndani?” Atafufuza ndi kufunsafunsa, analingalira kuti, “Gideoni mwana wa Yowasi ndiye wachita zimenezi.”
And thei seiden togidere, Who hath do this? And whanne thei enqueriden the doer of the deed, it was seid, Gedeon, the sone of Joas, dide alle these thingis.
30 Ndipo anthuwo anawuza Yowasi kuti, “Tulutsa mwana wako, ayenera kufa chifukwa wagumula guwa lansembe la Baala ndipo wadula fano la Asera lomwe linali pamwamba pake.”
And thei seiden to Joas, Brynge forth thi sone hidur, that he die, for he distriede the auter of Baal, and kittide doun the wode.
31 Koma Yowasi anawuza anthu amene anamuzungulirawo kuti, “Kodi inu mukuti mukhale woyankhulira Baala mlandu? Kodi ndinu amene mukuti mumupulumutse? Amene akufuna kumumenyera nkhondo Baala akhala atafa pofika mmawa! Ngati Baalayo ndi mulungudi, musiyeni adzimenyere yekha nkhondo popeza munthu wina wamugwetsera guwa lansembe lake.”
To whiche he answeride, Whether ye ben the venieris of Baal, that ye fiyte for hym? he that is aduersarie of hym, die, bifor that the `liyt of the morew dai come; if he is God, venge he hym silf of hym that castide doun his auter.
32 Choncho tsiku limenelo Gideoni anatchedwa, Yeru-Baala, kutanthauza kuti, “Baala alimbana naye, popeza anagwetsa guwa lake la nsembe.”
Fro that dai Gedeon was clepid Gerobaal, for Joas hadde seid, Baal take veniaunce of hym that castide doun his auter.
33 Tsopano Amidiyani, Amaleki ndi anthu ena akummawa anasonkhana ndipo atawoloka Yorodani anakamanga zinthando za nkhondo ku chigwa cha Yezireeli.
Therfor al Madian, and Amalech, and the puplis of the eest weren gadirid to gidere, and passiden Jordan, and settiden tentis in the valey of Jezrael.
34 Ndipo Mzimu wa Yehova unatsikira pa Gideoni, ndipo anayimba lipenga kuyitana Abiezeri kuti amutsatire iye.
Forsothe the spirit of the Lord clothide Gedeon; `and he sownede with a clarioun, and clepide to gidere the hows of Abiezer, that it schulde sue hym.
35 Iye anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Manase kuti akamenye nkhondo ndipo Amanase anayitanidwanso kuti amutsate. Anatumanso amithenga kwa Aseri, Azebuloni ndi Anafutali, ndipo onsewo anapita kukakumana naye.
And he sente messangeris in to al Manasses, and he suede Gedeon; and he sente othere messangeris in to Aser, and Zabulon, and Neptalym, whiche camen to hym.
36 Gideoni anati kwa Mulungu, “Ngati mudzapulumutsa Israeli ndi dzanja langa monga mwalonjezeramu,
And Gedeon seide to the Lord, If thou makist saaf Israel bi myn hond, as thou hast spoke,
37 onani, ine ndiyala ubweya wankhosa pa malo opunthira tirigu. Ngati mame adzagwera pa ubweya wankhosa pokhapa, pa nthaka ponse pakhala powuma, ndiye ndidziwa kuti mudzapulumutsadi Israeli ndi dzanja langa monga mwanenera.”
Y schal putte this flees of wolle in the corn floor; if dew is in the flees aloone, and drynesse is in al the erthe, Y schal wite, that thou schalt delyuere Israel bi myn hond, as thou hast spoke.
38 Ndipo zimenezi zinachitikadi. Gideoni atadzuka mʼmamawa ndi kuwufinya ubweya uja, anafinya madzi odzaza mtsuko.
And it was don so. And he roos bi nyyt, and whanne the flees was wrongun out, he fillide a pot with deew;
39 Kenaka Gideoni anati kwa Mulungu, “Musandikwiyire. Mundilole ndiyankhule kamodzi kokhaka. Ndiyeseko kamodzi kokha ndi ubweyawu kuti pa ubweya pokhapa pakhale powuma koma pa nthaka ponse pakhale ponyowa ndi mame.”
and he seide eft to the Lord, Thi strong veniaunce be not wrooth ayens me, if Y asaie, `that is, axe a signe, yit onys, and seke a signe in the flees; Y preye, that the flees aloone be drie, and al the erthe be moist with deew.
40 Ndipo Mulungu anachita zomwezo usiku umenewo. Pa ubweya pokha panali powuma, koma pa nthaka ponse panagwa mame.
And the Lord dide in that nyyt, as Gedeon axide; and drynesse was in the flees aloone, and deew was in al the erthe.

< Oweruza 6 >