< Oweruza 5 >

1 “Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:
I u taj dan pjeva Devora i Varak sin Avinejemov govoreæi:
2 “Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli; ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu, tamandani Yehova:
Blagosiljajte Gospoda što uèini osvetu u Izrailju i što narod dragovoljno prista.
3 “Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu! Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova, Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.
Èujte carevi, slušajte knezovi; ja, ja æu Gospodu pjevati, popijevaæu Gospodu Bogu Izrailjevu.
4 “Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri, pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu, dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka nigwetsa madzi.
Gospode! kad si slazio sa Sira, kad si išao iz polja Edomskoga, zemlja se tresijaše, i nebesa kapahu, oblaci kapahu vodom.
5 Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova, Mulungu wa Israeli.
Brda se rastapahu pred Gospodom; taj Sinaj pred Gospodom Bogom Izrailjevijem.
6 “Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati, pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa; alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.
Za vremena Samegara sina Anatova, za vremena Jailjina nesta putova, i koji iðahu stazama, iðahu krivijem putovima.
7 Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi mpaka pamene iwe Debora unafika; unafika ngati mayi ku Israeli.
Nesta sela u Izrailju, nesta ih, dokle ne nastah ja, Devora, dokle ne nastah majka Izrailju.
8 Pamene anasankha milungu ina, nkhondo inabwera ku zipata za mzinda, ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.
On izabra nove bogove, tada rat bijaše na vratima; viðaše li se štit ili koplje meðu èetrdeset tisuæa u Izrailju?
9 Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli, uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu. Tamandani Yehova!
Srce se moje privilo k upraviteljima Izrailjevijem, koji dragovoljno pristaše izmeðu naroda. Blagosiljajte Gospoda.
10 “Inu okwera pa abulu oyera, okhala pa zishalo, ndi inu oyenda pa msewu, yankhulani.
Koji jašete na bijelijem magaricama, koji sjedite u sudu i koji hodite po putovima, pripovijedajte.
11 Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta; kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana; akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli. “Choncho anthu a Yehova anasonkhana ku zipata za mzinda.
Prestala je praska streljaèka na mjestima gdje se voda crpe; ondje neka pripovijedaju pravdu Gospodnju, pravdu k selima njegovijem u Izrailju; tada æe narod Gospodnji slaziti na vrata.
12 Anati, ‘Tsogolera ndiwe, Debora, tsogolera; tsogolera ndiwe, tsogolera, imba nyimbo. Iwe Baraki! nyamuka Tsogolera akapolo ako, iwe mwana wa Abinoamu.’
Ustani, ustani, Devoro; ustani, ustani, zapjevaj pjesmu; ustani, Varaèe, vodi u ropstvo roblje svoje, sine Avinejemov.
13 “Kenaka anthu okhulupirika anatsatira atsogoleri awo; anthu a Yehova anapita kukamenyera Yehova nkhondo kulimbana ndi adani amphamvu.
Sada æe potlaèeni obladati silnima iz naroda; Gospod mi dade da vladam silnima.
14 Anakalowa mʼchigwa kuchokera ku Efereimu; akutsatira iwe Benjamini ndi abale ako. Akulu a ankhondo anachokera ku Makiri, ndipo onyamula ndodo ya udindo anachokera ku Zebuloni.
Iz Jefrema izide korijen njihov na Amalike; za tobom bješe Venijamin s narodom tvojim; od Mahira izidoše koji postavljaju zakone, a od Zavulona pisari.
15 Olamulira a Isakara anali pamodzi ndi Debora; inde, anthu ochokera ku Isakara anatsatanso Baraki, ndipo anathamangira ku chigwa akumutsatira. Koma pakati pa mafuko a Rubeni panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuchita.
I knezovi Isaharovi biše s Devorom, Isahar kao i Varak bi poslan u dolinu s ljudima koje voðaše. U dijelu Ruvimovu bijahu ljudi visokih misli.
16 Chifukwa chiyani munangokhala ku makola a nkhosa nʼkumangomvetsera zitoliro zoyitanira nkhosa? Pakati pa anthu a fuko la Rubeni panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuti achite.
Što si sjedio meðu torovima slušajuæi kako bleje stada? U dijelu Ruvimovu bijahu ljudi visokih misli.
17 Agiliyadi anatsala pa tsidya la Yorodani. Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu afuko la Dani anatsarira mʼsitima za pa madzi? Aseri anali pa gombe la Nyanja; anangokhala mʼmadooko mwawo.
Galad osta s onu stranu Jordana; a Dan što se zabavi kod laða? Asir zašto sjede na brijegu morskom i u krševima svojim osta?
18 Azebuloni ndi anthu amene anayika moyo wawo mʼzoopsa. Nawonso anthu a fuko la Nafutali anayika miyoyo yawo pa chiswe pomenya nkhondo pamwamba pa mapiri.
Zavulon je narod koji dade dušu svoju na smrt, tako i Neftalim, na visokom polju.
19 “Mafumu anabwera, anachita nkhondo; mafumu Akanaani anachita nkhondo ku Tanaki pafupi ndi madzi a ku Megido, koma sanatengeko zofunkha zasiliva.
Doðoše carevi, biše se; biše se carevi Hananski u Tanahu na vodi Megidskoj; ali ni mrve srebra ne dobiše.
20 Ngakhalenso nyenyezi zakumwamba zinachita nkhondo, zinathira nkhondo Sisera, zikuyenda mʼnjira zake.
S neba se vojeva, zvijezde s mjesta svojih vojevaše na Sisaru.
21 Mtsinje wa Kisoni unawakokolola, chigumula cha mtsinje wa Kisoni chinawakokolola. Mtima wanga, yenda mwamphamvu, limbika!
Potok Kison odnese ih, potok Kadimin, potok Kison; pogazila si, dušo moja, snažno.
22 Ndipo ziboda za ngʼombe zazimuna zinachita phokoso lalikulu, akavalo ali pa liwiro, akuthamanga kwambiri.
Tada izotpadaše konjma kopita od tjeranja junaka njihovijeh.
23 Mngelo wa Yehova anati ‘Tembererani Merozi.’ ‘Tembererani nzika zake mwaukali, chifukwa sanabwere kudzathandiza Yehova, kulimbana ndi adani ake amphamvu.’
Proklinjite Miroz, reèe anðeo Gospodnji, proklinjite stanovnike njegove; jer ne doðoše u pomoæ Gospodu, u pomoæ Gospodu s junacima.
24 “Akhale wodala kupambana akazi onse, Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni; inde mwa akazi onse okhala mʼdziko, akhale wodala iyeyu.
Da je blagoslovena mimo žene Jailja žena Evera Kenejina; mimo žene u šatorima da je blagoslovena.
25 Munthu uja anapempha madzi akumwa, koma iye anamupatsa mkaka; anamupatsa chambiko mʼchikho cha wolemekezeka.
Zaiska vode, mlijeka mu dade, u gospodskoj zdjeli donese mu povlaku.
26 Anatenga chikhomo cha tenti mʼdzanja lake, anatenganso nyundo ndi dzanja lake lamanja. Ndipo anakhoma nacho Sisera, anamuphwanya mutu wake, ndi kumubowola mu litsipa mwake.
Lijevom rukom maši se za kolac a desnom za malj kovaèki, i udari Sisaru, razmrska mu glavu; probode i probi mu slijepe oèi.
27 Anathifukira ku mapazi a mkaziyo nagwa, anagwa; iye anagona pamenepo. Anagwera pa mapazi a mkaziyo, iye anagwa; pamene anagwera, pamenepo anaferapo.
Meðu noge njezine savi se, pade, leža; meðu noge njezine savi se, pade; gdje se savi, ondje pade mrtav.
28 “Amayi ake a Sisera anasuzumira pa zenera; nafuwula mokweza kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani galeta lake lachedwa kufika? Nʼchifukwa chiyani phokoso la magaleta ake silikumveka?’
S prozora gledaše majka Sisarina, i kroz rešetku vikaše: što se tako dugo ne vraæaju kola njegova? što se tako polako mièu toèkovi kola njegovijeh?
29 Amayi ake anzeru kwambiri anamuyankha, ndithudi, mwiniwake anadziyankha yekha kuti,
Najmudrije izmeðu dvorkinja njezinijeh odgovarahu joj, a i sama odgovaraše sebi:
30 ‘Kodi iwo sakufunafuna zofunkha kuti agawane; akugawana wankhondo aliyense mtsikana mmodzi kapena awiri. Sisera akumupatsa zofunkha: zovala zonyikidwa mu utoto, zoti ndizivala mʼkhosi zovala zopeta zonyika mu utoto, ndi zopeta zomavala mʼkhosi?’
Nijesu li našli? ne dijele li plijen? po jednu djevojku, po dvije djevojke na svakoga. Plijen šaren Sisari, plijen šaren, vezen; šaren, vezen s obje strane, oko vrata onima koji zaplijeniše.
31 “Choncho Yehova! adani anu onse awonongeke, koma iwo amene amakukondani inu akhale ngati dzuwa pamene lituluka ndi mphamvu zake.” Ndipo dziko linakhala pa mtendere zaka makumi anayi.
Tako da izginu svi neprijatelji tvoji, Gospode; a koji te ljube da budu kao sunce kad izlazi u sili svojoj. I zemlja bi mirna èetrdeset godina.

< Oweruza 5 >