< Oweruza 14 >

1 Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti.
I siðe Samson u Tamnat, i vidje ondje jednu djevojku izmeðu kæeri Filistejskih.
2 Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”
I vrativši se kaza ocu svojemu i materi svojoj govoreæi: vidjeh djevojku u Tamnatu izmeðu kæeri Filistejskih; oženite me njom.
3 Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?” Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.”
A otac i mati rekoše mu: zar nema djevojke meðu kæerima tvoje braæe u svem narodu mom, da ideš da se oženiš izmeðu Filisteja neobrezanijeh? A Samson odgovori ocu svojemu: njom me oženi, jer mi je ona omiljela.
4 (Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli).
A otac i mati njegova ne znadijahu da je to od Gospoda, i da traži zadjevicu s Filistejima; jer u ono vrijeme Filisteji vladahu sinovima Izrailjevijem.
5 Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye.
I tako side Samson s ocem svojim i s materom svojom u Tamnat, i kad doðoše do vinograda Tamnatskih, gle, mlad lav rièuæi sukobi ga.
6 Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo.
I duh Gospodnji side na nj, te rastrže lava kao jare nemajuæi ništa u ruci: i ne kaza ocu ni materi šta je uèinio.
7 Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.
I tako došavši govori s djevojkom, i ona omilje Samsonu.
8 Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake.
A poslije nekoliko dana iduæi opet da je odvede, svrne da vidi mrtvoga lava; a gle, u mrtvom lavu roj pèela i med.
9 Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.
I izvadi ga u ruku, i poðe putem jeduæi; i kad doðe k ocu i materi, dade im te jedoše; ali im ne reèe da je iz mrtvoga lava izvadio med.
10 Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata.
I tako doðe otac njegov k onoj djevojci, i Samson uèini ondje veselje, jer tako èinjahu momci.
11 Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.
I kad ga vidješe Filisteji, izabraše trideset druga da budu s njim.
12 Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero.
I reèe im Samson: ja æu vam zagonenuti zagonetku, pa ako mi je odgonenete za sedam dana dok je veselje i pogodite, daæu vam trideset košulja i tridesetore sveèane haljine.
13 Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.” Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”
Ako li ne odgonenete, vi æete dati meni trideset košulja i tridesetore sveèane haljine. A oni mu rekoše: zagoneni zagonetku svoju, da èujemo.
14 Iye anati, “Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake; ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.” Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.
Tada im reèe: od onoga koji jede izide jelo, i od ljutoga izide slatko. I ne mogoše odgonenuti zagonetke tri dana.
15 Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”
I sedmi dan rekoše ženi Samsonovoj: nagovori muža svojega da nam kaže zagonetku, ili æemo spaliti ognjem tebe i dom oca tvojega. Jeste li nas zato pozvali da nam uzmete imanje? je li tako?
16 Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.” Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?”
I stade plakati žena Samsonova pred njim govoreæi: ti mrziš na me, i ti me ne ljubiš; zagonenuo si zagonetku sinovima naroda mojega, a neæeš meni da je kažeš. A on joj reèe: gle, ni ocu svojemu ni materi svojoj nijesam je kazao, a tebi da je kažem?
17 Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.
I ona plaka pred njim za sedam dana dokle trajaše veselje. A sedmi dan kaza joj, jer bješe navalila na nj; a ona kaza zagonetku sinovima naroda svojega.
18 Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti, “Chozuna nʼchiyani choposa uchi? Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?” Samsoni anawawuza kuti, “Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono, simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”
Tada mu rekoše ljudi grada onoga sedmi dan dok sunce ne zaðe: šta je slaðe od meda, i šta je ljuæe od lava? A on im reèe: da nijeste orali na mojoj junici, ne biste pogodili moje zagonetke.
19 Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu.
I doðe na nj duh Gospodnji, te siðe u Askalon, i pobi ondje trideset ljudi, i uze odijelo s njih i dade sveèane haljine onima koji odgonenuše zagonetku; i rasrdi se vrlo i otide kuæi oca svojega.
20 Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.
A žena Samsonova udade se za druga njegova, s kojim se bijaše udružio.

< Oweruza 14 >