< Oweruza 11 >

1 Yefita wa ku Giliyadi anali wankhondo wa mphamvu. Iyeyu amayi ake anali mkazi wachiwerewere, ndipo abambo ake anali Giliyadi.
A Jeftaj od Galada bijaše hrabar junak, ali sin jedne kurve, s kojom Galad rodi Jeftaja.
2 Mkazi wake wa Giliyadi anabereka naye ana aamuna. Tsono ana amenewa atakula anapirikitsa Yefita ndi kumuwuza kuti, “Sudzalandirako cholowa mʼnyumba ya abambo athu chifukwa ndiwe mwana wa mkazi wina.”
Ali Galadu i žena njegova rodi sinova, pa kad dorastoše sinovi te žene, otjeraše Jeftaja rekavši mu: neæeš imati našljedstva u domu oca našega, jer si sin druge žene.
3 Choncho Yefita anathawa kuchoka kwa abale ake ndi kukakhala mʼdziko la Tobu. Kumeneko anakakopa ndi kusonkhanitsa anthu achabechabe ndipo anatuluka pamodzi kukasakaza zinthu.
Zato pobježe Jeftaj od braæe svoje, i nastani se u zemlji Tovu; i stekoše se k njemu ljudi praznovi, i iðahu s njim.
4 Patapita nthawi Aamoni anadzachita nkhondo ndi Israeli.
A poslije nekoga vremena zavojštiše sinovi Amonovi na Izrailja;
5 Tsono pamene Aamoni ankathira nkhondo Aisraeli, akuluakulu a ku Giliyadi anapita kukamutenga Yefita ku dziko la Tobu.
I kad zavojštiše sinovi Amonovi na Izrailja, otidoše starješine Galadske da dovedu Jeftaja iz zemlje Tova.
6 Iwo anati kwa iye, “Bwera ukhale mkulu wathu wankhondo kuti timenyane ndi Amoni.”
I rekoše Jeftaju: hodi i budi nam vojvoda, da vojujemo sa sinovima Amonovijem.
7 Yefita anawawuza Agiliyadi kuti, “Kodi inu suja munkadana nane ndi kundithamangitsa ku nyumba ya abambo anga? Nʼchifukwa chiyani lero mwabwera kwa ine pamene muli pa mavuto?”
A Jeftaj reèe starješinama Galadskim: ne mrzite li vi na me, i ne istjeraste li me iz doma oca mojega? Što ste dakle došli k meni sada kad ste u nevolji?
8 Akuluakulu a ku Giliyadi aja anamuyankha kuti, “Chimene tabwerera kwa iwe ndi chakuti upite nafe kukamenyana ndi Aamoni, ndipo udzakhala wolamulira wa onse okhala mu Giliyadi.”
A starješine Galadske rekoše Jeftaju: zato smo sada došli opet k tebi da poðeš s nama i da vojuješ sa sinovima Amonovijem i da nam budeš poglavar svjema koji živimo u Galadu.
9 Yefita anawayankha akuluakulu a ku Giliyadi kuti, “Ngati mundibwezeranso kwathu kuti ndikachite nkhondo ndi Aamoni ndipo Yehova nʼkukandithandiza kuwagonjetsa, ndidzakhaladi wokulamulirani?”
A Jeftaj reèe starješinama Galadskim: kad hoæete da me odvedete natrag da vojujem sa sinovima Amonovijem, ako mi ih da Gospod, hoæu li vam biti poglavar?
10 Akuluakulu a ku Giliyadi anamuyankha kuti, “Yehova akhale mboni pakati pa inu ndi ife, ngati sitidzachita monga mwa mawu anu.”
A starješine Galadske rekoše Jeftaju: Gospod neka bude svjedok meðu nama, ako ne uèinimo kako si kazao.
11 Choncho Yefita anapita nawo akuluakulu a ku Giliyadi aja, ndipo anthu a kumeneko anamusandutsa kukhala wowalamulira ndi mkulu wankhondo. Tsono Yefita anabwerezanso mawu omwewa pamaso pa Yehova ku Mizipa.
Tada otide Jeftaj sa starješinama Galadskim, i narod ga postavi poglavarem i vojvodom nad sobom; i Jeftaj izgovori pred Gospodom u Mispi sve rijeèi koje bješe rekao.
12 Kenaka Yefita anatuma amithenga kwa mfumu ya Aamoni ndi funso lakuti, “Kodi ife takuchimwirani chiyani kuti muzichita nkhondo ndi dziko langa?”
Potom posla Jeftaj poslanike k caru sinova Amonovijeh, i poruèi: šta imaš ti sa mnom, te si došao k meni da ratuješ po mojoj zemlji?
13 Ndipo mfumu ya Aamoni inayankha amithenga a Yefita aja kuti, “Pamene Israeli amatuluka kuchokera mu Igupto, analanda dziko langa kuyambira ku mtsinje wa Arinoni mpaka ku mtsinje wa Yaboki mpakanso ku mtsinje wa Yorodani. Tsopano mundibwezere dziko langa mwamtendere.”
A car sinova Amonovijeh reèe poslanicima Jeftajevim: što je uzeo Izrailj moju zemlju kad doðe iz Misira, od Arnona do Javoka i do Jordana; sada dakle vrati mi je s mirom.
14 Yefita anatumizanso amithenga akewo kwa mfumu ya Aamoni
Ali Jeftaj posla opet poslanike k caru sinova Amonovijeh,
15 kukanena kuti, Yefita akuti, “Israeli sanalande dziko la Mowabu kapena dziko la Aamoni.
I poruèi mu: ovako veli Jeftaj: nije uzeo Izrailj zemlje Moavske ni zemlje sinova Amonovijeh.
16 Koma pamene Aisraeli ankachoka ku Igupto anadzera njira ya ku chipululu mpaka ku Nyanja Yofiira nakafika ku Kadesi.
Nego izašavši iz Misira prijeðe Izrailj preko pustinje do Crvenoga Mora i doðe do Kadisa.
17 Kenaka Israeli anatumiza amithenga kwa mfumu ya ku Edomu kuti, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu,’ Koma mfumu ya ku Edomu sinamvere zimenezo. Aisraeli anatumizanso amithenga kwa mfumu ya ku Mowabu, ndipo iyo inakananso. Choncho Israeli anakhala ku Kadesi.
I posla Izrailj poslanike k caru Edomskomu i reèe: pusti da proðem kroz tvoju zemlju. Ali ne posluša car Edomski. Posla takoðe k caru Moavskomu; ali ni on ne htje. I tako staja Izrailj u Kadisu.
18 “Pambuyo pake, Aisraeli ananyamuka ulendo kudzera ku chipululu nazungulira dziko la Edomu ndi dziko la Mowabu, ndipo anafika ku mmawa kwa dziko la Mowabu ndi kumanga zinthando zawo ku mbali ina ya mtsinje wa Arinoni. Iwo sanalowe mʼdziko la Mowabu, chifukwa mtsinje wa Arinoni ndiwo unali malire a dziko la Mowabu.
Potom iduæi preko pustinje obide zemlju Edomsku i zemlju Moavsku, i došavši s istoka zemlji Moavskoj stade u oko s onu stranu Arnona; ali ne prijeðoše preko meðe Moavske, jer Arnon bješe meða Moavska.
19 “Pambuyo pake Israeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, amene amalamulira ku Hesiboni ndipo anati kwa iye, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu popita kwathu.’
Nego posla Izrailj poslanike k Sionu caru Amorejskomu, caru Esevonskomu, i reèe mu Izrailj: dopusti nam da proðemo kroz tvoju zemlju do svojega mjesta.
20 Koma Sihoni sanalole Israeli kuti adzere mʼdziko mwake. Mʼmalo mwake Sihoni anasonkhanitsa ankhondo ake onse nakamanga msasa ku Yahazi ndipo anachita nkhondo ndi Israeli.
Ali Sion ne vjerova Izrailju da ga pusti da prijeðe preko meðe njegove, nego Sion skupi sav svoj narod i stadoše u oko u Jasi, i pobi se s Izrailjem.
21 “Koma Yehova Mulungu wa Israeli anamupereka Sihoni pamodzi ndi anthu ake onse mʼmanja mwa Israeli, ndipo anawagonjetsa. Choncho Aisraeli analanda dziko lonse la Aamori amene amakhala mʼdzikolo.
A Gospod Bog Izrailjev predade Siona i sav narod njegov u ruke sinovima Izrailjevijem, te ih pobiše; i zadobi Izrailj svu zemlju Amoreja, koji življahu u onoj zemlji.
22 Analanda dziko lonse kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki ndiponso kuchokera ku chipululu mpaka ku mtsinje wa Yorodani.
Zadobiše svu zemlju Amorejsku od Arnona do Javoka, i od pustinje do Jordana.
23 “Ndiye kuti Yehova Mulungu wa Aisraeli ndiye analanda dziko la Aamori, kuwalandirira anthu ake. Kodi inu mukufuna kutilanda dzikolo?
Tako je dakle Gospod Bog Izrailjev otjerao Amoreje ispred naroda svojega Izrailja, pa ti li hoæeš da je zemlja njihova tvoja?
24 Bwanji inu osakhazikika mʼdziko limene Kemosi mulungu wanu anakupatsani, ifenso tikhazikike mʼdziko limene Yehova Mulungu wathu anatipatsa?
Nije li tvoje ono što ti da da je tvoje Hemos bog tvoj? tako koga god Gospod Bog naš otjera ispred nas, onoga je zemlja naša.
25 Kodi ndinu abwino kuposa Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu? Kodi iye anakanganapo kapena kuchita nkhondo ndi Israeli?
Ili si ti po èem bolji od Valaka sina Seforova cara Moavskoga? Je li se on kad svaðao s Izrailjem? Je li kad vojevao s nama?
26 Pamene Aisraeli ankakhala mʼdziko la Hesiboni ndi mʼmidzi yake, mʼdziko la Aroeri ndi midzi yake, komanso mʼmizinda yonse imene ili mʼmbali mwa mtsinje wa Arinoni kwa zaka 300, nʼchifukwa chiyani inu simunalande malowo nthawi imeneyo?
Izrailj živi u Esevonu i u selima njegovijem i u Aroiru i selima njegovijem i po svijem gradovima duž Arnona tri stotine godina; zašto ne oteste za toliko vremena?
27 Choncho ine sindinakuchimwireni. Koma inu mukundilakwira pomenyana nane. Yehova woweruza, ndiye aweruze lero mlandu wa pakati pa Aisraeli ndi Aamoni.”
I tako nijesam ja tebi skrivio, nego ti meni èiniš zlo ratujuæi na me. Gospod sudija nek sudi danas izmeðu sinova Izrailjevijeh i sinova Amonovijeh.
28 Koma mfumu ya Aamori, sinasamale mawu amene Yefita anatumiza kwa iyo.
Ali car sinova Amonovijeh ne posluša rijeèi koje mu poruèi Jeftaj.
29 Tsono Mzimu wa Yehova unatsikira pa Yefita. Ndipo iye ananyamuka nadzera ku Giliyadi ndi ku Manase. Anafika ku Mizipa mʼdziko la Giliyadi, ndipo kuchokera kumeneko anapita kukalimbana ndi Aamoni.
I siðe na Jeftaja duh Gospodnji, te proðe kroz Galad i kroz Manasiju, proðe i Mispu Galadsku, i od Mispe Galadske doðe do sinova Amonovijeh.
30 Yefita analumbira kwa Yehova kuti, “Ngati mupereka Aamoni mʼmanja mwanga,
I zavjetova Jeftaj zavjet Gospodu i reèe: ako mi daš sinove Amonove u ruke,
31 aliyense amene atuluke pa khomo la nyumba yanga kudzandichingamira pobwerera nditagonjetsa Aamoni adzakhala wake wa Yehova, ndipo ndidzamupereka kuti akhale nsembe yopsereza.”
Što god izide na vrata iz kuæe moje na susret meni, kad se vratim zdrav od sinova Amonovijeh, biæe Gospodnje, i prinijeæu na žrtvu paljenicu.
32 Kenaka Yefita anawolokera kwa Aamoni kukamenya nawo nkhondo, ndipo Yehova anawaperekadi mʼmanja mwake.
I tako doðe Jeftaj do sinova Amonovijeh da se bije s njima; i Gospod mu ih dade u ruke.
33 Iye anawononga mizinda makumi awiri kuchokera ku Ariori mpaka pafupi ndi mzinda wa Miniti. Anapitirira mpaka ku Abeli-Keranimu. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamoni.
I pobi ih od Aroira pa do Minita u dvadeset gradova i do ravnice vinogradske u boju vrlo velikom; i sinovi Amonovi biše pokoreni pred sinovima Izrailjevijem.
34 Pambuyo pake Yefita anabwerera ku nyumba yake. Tsono anangoona mwana wake wamkazi akutuluka kudzamuchingamira akuyimba ngʼoma ndi kuvina. Uyu anali mwana yekhayo wa Yefita. Analibenso mwana wina wamwamuna kapena wamkazi.
A kad se vraæaše Jeftaj kuæi svojoj u Mispu, gle, kæi njegova izide mu na susret s bubnjima i sviralama; ona mu bijaše jedinica, i osim nje ne imaše ni sina ni kæeri.
35 Yefita ataona mwana wake uja, anangʼamba zovala zake ndi kulira, “Kalanga ine! Mwana wanga! Wandivulaza kwambiri ndipo iwe ndi gwero la mavuto anga. Ine ndinalumbira kwa Yehova ndi pakamwa pangapa ndipo sindingathe kubweza malumbiro angawo.”
Pa kad je ugleda, razdrije haljine svoje i reèe: ah kæeri moja! vele li me obori! ti si od onijeh što me cvijele; jer sam otvorio usta svoja ka Gospodu, i ne mogu poreæi.
36 Mwanayo anayankha kuti, “Abambo, ngati munalonjeza kwa Yehova ndi pakamwa panu, chitani zimene munalonjezera pakuti Yehova wakuthandizani kulipsira adani anu Amowabu.”
A ona mu reèe: oèe moj, kad si otvorio usta svoja ka Gospodu, uèini mi, kako je izašlo iz usta tvojih, kad te je Gospod osvetio od neprijatelja tvojih, sinova Amonovijeh.
37 Anatinso kwa abambo ake, “Ndikupempheni chinthu ichi: Mundilole ndikayendeyende ku mapiri miyezi iwiri ndizikalira pamodzi ndi anzanga chifukwa ndikufa ndikanali namwali wosadziwa mwamuna.”
Još reèe ocu svojemu: uèini mi ovo: ostavi me do dva mjeseca da otidem da se popnem na gore da oplaèem svoje djevojaštvo s drugama svojim.
38 Yefita anamuyankha kuti, “Pita.” Ndipo anamulola kuti apite miyezi iwiri. Tsono anapita kumapiri ndi atsikana anzake kukalira chifukwa cha unamwali wake.
A on joj reèe: idi. I pusti je na dva mjeseca, i ona otide s drugama svojim i oplakiva djevojaštvo svoje po gorama.
39 Miyezi iwiri itatha iye anabwerera kwa abambo ake, ndipo anachitadi zimene analonjeza. Motero unakhala mwambo wa Aisraeli,
A kad proðoše dva mjeseca, vrati se k ocu svojemu, i on svrši na njoj zavjet svoj koji bješe zavjetovao. A ona ne pozna èovjeka. I posta obièaj u Izrailju
40 kuti atsikana a Israeli ankapita chaka chilichonse kukalira maliro a mwana wa mkazi wa Yefita, Mgiliyadi uja masiku makumi anayi pa chaka.
Da od godine do godine idu kæeri Izrailjeve da plaèu za kæerju Jeftaja od Galada, èetiri dana u godini.

< Oweruza 11 >