< Yoswa 24 >

1 Tsono Yoswa anasonkhanitsa mafuko onse a Israeli ku Sekemu. Iye anayitanitsa akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi akuluakulu a boma la Israeli, ndipo iwo anafika pamaso pa Mulungu.
And Josue gaderide alle the lynagis of Israel in to Sechem; and he clepide the grettere men in birthe, and the princes, and iugis, and maistris; and thei stoden in the siyt of the Lord.
2 Yoswa anati kwa anthu onse, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Kalekale makolo anu, kuphatikiza Tera, abambo a Abrahamu ndi Nahori ankakhala kutsidya kwa Mtsinje ndipo ankapembedza milungu ina.
And he spak thus to the puple, The Lord God of Israel seith these thingis, Youre fadris dwelliden at the bigynnyng biyende the flood Eufrates, Thare, the fadir of Abraham, and Nachor, and thei serueden alien goddis.
3 Koma ine ndinatenga kholo lanu Abrahamu kumuchotsa ku dziko la kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndipo ndinamutsogolera kupita ku dziko la Kanaani. Ndinamupatsa zidzukulu zambiri. Ndinamupatsa Isake,
Therfor Y took youre fadir Abraham fro the coostis of Mesopotanye, and Y brouyte hym in to the lond of Canaan; and Y multipliede `the seed of hym,
4 ndipo Isake ndinamupatsa Yakobo ndi Esau. Ndinapereka dziko la mapiri la Seiri kwa Esau, koma Yakobo ndi ana ake anapita ku Igupto.
and Y yaf Isaac to hym; and eft Y yaf to Isaac, Jacob, and Esau, of whiche Y yaf to Esau the hil of Seir, to `haue in possessioun; forsothe Jacob and hise sones yeden doun in to Egipt.
5 “‘Kenaka ndinatuma Mose ndi Aaroni, ndipo ine ndinazunza Aigupto. Pambuyo pake ndinakutulutsani.
And Y sente Moises and Aaron, and Y smoot Egipt with many signes and wondris,
6 Nditatulutsa makolo anu ku Igupto ndinafika nawo ku Nyanja Yofiira. Aigupto anawathamangira ndi magaleta ndi okwera pa akavalo mpaka ku Nyanja Yofiira.
and Y ledde you and youre fadris out of Egipt. And ye camen to the see, and Egipcians pursueden youre fadris with charis, and multitude of knyytis, `til to the Reed See.
7 Tsono makolo anuwo anapemphera kwa Ine kuti ndiwathandize, ndipo ndinayika mtambo wakuda pakati pawo ndi Aiguptowo, ndipo Nyanja inamiza Aigupto aja. Inu munaona ndi maso anu zimene ndinachita kwa Aiguptowo ndipo inu munakhala mʼchipululu nthawi yayitali.
Forsothe the sones of Israel crieden to the Lord, and he settide derknessis bitwixe you and Egipcians; and he brouyte the see on hem, and hilide hem. Youre iyen sien alle thingis, whiche Y dide in Egipt. And ye dwelliden in wildirnesse in myche tyme.
8 “‘Pambuyo pake Ine ndinabwera nanu ku dziko la Aamori amene amakhala kummawa kwa Yorodani. Iwo anamenyana nanu koma ndinawapereka mʼdzanja lanu. Ndinawawononga pamaso panu, ndipo inu munalanda dziko lawo.
And Y brouyte you in to the lond of Ammorrei, that dwellide biyende Jordan; and whanne thei fouyten ayens you, Y bitook hem in to youre hondis, and ye hadden in possessioun `the lond of hem, and ye killiden hem.
9 Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu, analimbana ndi Israeli. Iye anayitanitsa Balaamu mwana wa Beori kuti akutemberereni.
Sotheli Balach, the sone of Sephor, the king of Moab, roos, and fauyt ayens Israel; and he sente, and clepide Balaam, the sone of Beor, that he schulde curse you.
10 Koma ine sindinamvere Balaamu, kotero iye anakudalitsani mowirikiza ndipo ndinakulanditsani mʼdzanja lake.
And Y nolde here hym, but ayenward bi hym Y blesside you, and delyuerede you fro hise hondis.
11 “‘Ndipo inu munawoloka Yorodani ndi kufika ku Yeriko. Anthu a ku Yeriko analimbana nanu pamodzi ndi Aamori, Aperezi, Akanaani, Ahiti, Agirigasi, Ahivi ndi Ayebusi. Koma Ine ndinawapereka mʼdzanja lanu.
And ye passiden Jordan, and camen to Jerico; and men of that citee fouyten ayens you, Ammorrei, and Feresei, and Cananei, Ethei, and Gergesei, and Euei, and Jebusei; and Y bitook hem in to youre hondis.
12 Ine ndinatumiza mavu amene anapirikitsa mafumu awiri Aamori aja pamaso panu. Inu simunachite izi ndi lupanga ndi uta wanu.
And Y sente flies with venemouse tongis bifor you, and Y castide hem out of her places; Y kyllide twei kyngis of Ammorreis, not in thi swerd and bowe.
13 Motero ndinakupatsani dziko limene simunalivutikire ndiponso mizinda imene simunamange. Inu mukukhala mʼmenemo ndi kumadya zipatso za mʼmunda wamphesa ndi kuthyola zipatso mʼmitengo ya olivi zimene simunadzale.’
And Y yaf to you the lond in which ye traueiliden not, and citees whiche ye bildiden not, that ye schulden dwelle in tho, and vyneris, and places of olyue trees, whiche ye plauntiden not.
14 “Ndipo tsopano wopani Yehova ndi kumutumikira Iye mokhulupirika ndi moona. Chotsani milungu imene makolo anu ankapembedza kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndi ku Igupto ndipo tumikirani Yehova.
Now therfor drede ye the Lord, and serue ye hym with perfite herte and moost trewe; and do ye awei the goddis, to whiche youre fadris seruyden in Mesopotanye, and in Egipt; and serue ye the Lord.
15 Koma ngati kutumikira Yehova kukuyipirani, sankhani lero amene mudzamutumikire, kapena milungu imene makolo anu ankayitumikira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, kapena milungu ya Aamori, amene mukukhala mʼdziko lawo. Koma ine ndi banja langa, tidzatumikira Yehova.”
But if it semeth yuel to you, `that ye serue the Lord, chesyng is youun to you; chese ye to you to dai that, that plesith, whom ye owen most to serue; whether to goddis, whiche youre fadris serueden in Mesopotanye, whether to the goddis of Ammorreis, in whose lond ye dwellen; forsothe Y, and myn hows schulen serue the Lord.
16 Ndipo anthu anayankha, “Sizingatheke kuti timusiye Yehova ndi kutumikira milungu ina!
And al the puple answeride and seide, Fer be it fro vs that we forsake the Lord, and serue alien goddis.
17 Yehova Mulungu wathu ndiye amene anatitulutsa ife ndi makolo athu mu ukapolo, mʼdziko la Igupto. Tinaona ndi maso athu zizindikiro zozizwitsa zimene anachita. Iye anatiteteza pa ulendo wathu wonse ndi pakati pa mitundu yonse imene tinkakumana nayo.
`Oure Lord God hym silf ledde vs and oure fadris out of the lond of Egipt, fro the hows of seruage, and dide grete signes in oure siyt; and he kepte vs in al the weie, bi which we yeden, and in alle puplis, bi whiche we passiden; and he castide out alle folkis,
18 Ife tikufika Iye anapirikitsa anthu onse pamodzi ndi Aamori amene ankakhala mʼdzikoli. Ifenso tidzatumikira Yehova chifukwa Iye ndiye Mulungu.”
Ammorrei, the dwellere of the lond, in to which we entriden. Therfor we schulen serue the Lord, for he is `oure Lord God.
19 Koma Yoswa anati kwa anthuwo, “Inutu simungathe kutumikira Yehova. Iye ndi Mulungu woyera, salola kupikisana naye. Sadzakukhululukirani ngati mumuwukira ndi kumuchimwira.
And Josue seide to the puple, Ye moun not serue the Lord; for God is hooli, and a strong feruent louyere, and he foryyueth not youre trespassis and synnes.
20 Ngati inu musiya Yehova ndi kutumikira milungu yachilendo, adzakufulatirani. Iye adzakulangani ndi kukuwonongani ngakhale kuti poyamba anakuchitirani zabwino.”
If ye forsaken the Lord, and seruen alien goddis, the Lord schal turne `hym silf, and schal turment you, and schal distrie, after that he hath youe goodis to you.
21 Koma anthuwo anati kwa Yoswa, “Ayi! Ife tidzatumikira Yehova.”
And the puple seide to Josue, It schal not be so, as thou spekist, but we schulen serue the Lord.
22 Kenaka Yoswa anati, “Inu mukudzichitira nokha umboni kuti mwasankha kutumikira Yehova.” Iwo anayankha kuti, “Inde ife ndife mboni.”
And Josue seide to the puple, Ye ben witnessis, that ye han chose the Lord to you, that ye serue him. And thei answeriden, We ben witnessis.
23 Yoswa anati, “Tsono chotsani milungu yachilendo imene ili pakati panu ndipo perekani mitima yanu kwa Yehova Mulungu wa Israeli.”
Therfor, he seide, Now do ye awei alien goddis fro the myddis of you, and bowe ye youre hertis to the Lord God of Israel.
24 Ndipo anthuwo anati kwa Yoswa, “Ife tidzatumikira Yehova Mulungu wathu ndi kumvera Iye.”
And the puple seide to Josue, We schulen serue `oure Lord God, and we schulen be obedient to hise heestis.
25 Choncho pa tsiku limenelo Yoswa anachita pangano mʼmalo mwa anthuwo, ndipo pa Sekemu pomwepo iye anapereka malamulo ndi malangizo kwa anthu aja.
Therfor Josue smoot a boond of pees in that dai, and settide forth to the puple comaundementis and domes in Sichen.
26 Ndipo Yoswa analemba zinthu izi mʼbuku la malamulo a Mulungu. Kenaka iye anatenga mwala waukulu nawuyimika pansi pa mtengo wa thundu pa malo wopatulika a Yehova.
And he wroot alle these wordis in the book of Goddis lawe. And he took a greet stoon, and puttide it vndur an ook, that was in the seyntuarie of the Lord.
27 Yoswa anati kwa anthu onse, “Tamvani! Mwala uwu udzakhala mboni yotitsutsa. Mwalawu wamva mawu onse amene Yehova wayankhula kwa ife. Udzakhala mboni yotitsutsa ngati mukhala osakhulupirika kwa Mulungu wanu.”
And he seide to al the puple, Lo! this stoon schal be to you in to witnessing, that ye herden alle the wordis of the Lord, whiche he spak to you, lest perauenture ye wolden denye aftirward, and lye to youre Lord God.
28 Kenaka Yoswa analola anthu kuti apite, aliyense ku dera lake.
And he lefte the puple, ech man in to his possessioun.
29 Zitatha zinthu izi, Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110,
And after these thingis Josue, the sone of Nun, the `seruaunt of the Lord, diede, an hundride yeer eld and ten.
30 ndipo anamuyika mʼmanda mʼdziko lake, ku Timnati-Sera dziko lamapiri la ku Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
And thei birieden hym in the costis of his possessioun, in Thannath of Sare, which is set in the hil of Effraym, fro the north part of the hil Gaas.
31 Israeli anatumikira Yehova pa nthawi yonse imene Yoswa anali ndi moyo ndiponso pa nthawi ya akuluakulu amene anali moyo Yoswa atamwalira, anthu amene ankadziwa zonse zimene Yehova anachitira Israeli.
And Israel seruede the Lord in alle the daies of Josue, and of the eldre men, that lyueden in long tyme aftir Josue, and whiche eldre men knewen alle the werkis of the Lord, whiche he hadde do in Israel.
32 Ndipo mafupa a Yosefe amene Aisraeli anawatulutsa ku Igupto anawayika mʼmanda a ku Sekemu pa malo amene Yakobo anagula ndi ndalama zasiliva 100 kwa ana a Hamori, abambo a Sekemu. Malo awa anakhala cholowa cha adzukulu a Yosefe.
Also `the sones of Israel birieden the boonys of Joseph, whiche thei baren fro Egipt in Sichen, in the part of the feeld, which feeld Jacob bouyte of the sones of Emor, fadir of Sichen, for an hundrid yonge scheep; and it was in to possessioun of the sones of Joseph.
33 Ndipo Eliezara mwana wa Aaroni anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda ku Gibeya, malo amene anapatsidwa kwa Finehasi mwana wake, mʼdziko lamapiri la Efereimu.
Also Eliazar, sone of Aaron, preest, diede; and Fynees and hise sones biryden hym in Gabaa, which was youun to hym in the hil of Efraym.

< Yoswa 24 >