< Yoswa 23 >

1 Panapita nthawi yayitali kuchokera pamene Yehova anakhazikitsa mtendere pakati pa Aisraeli ndi adani awo owazungulira. Nthawi imeneyi nʼkuti Yoswa atakalamba, ali ndi zaka zambiri.
Forsothe whanne myche tyme was passid after that the Lord had youe pees to Israel, for alle naciouns `in cumpas weren suget; and whanne Josue was thanne of long lijf, and `of ful eld age, Josue clepide al Israel,
2 Yoswayo anayitanitsa Aisraeli onse pamodzi ndi akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi oyangʼanira anthu antchito ndipo anawawuza kuti, “Ine ndakalamba ndipo ndili ndi zaka zambiri.
and the grettere men in birthe, and the princes, and dukis, and maistris, and seide to hem, Y `wexide elde, and Y am of grettere age;
3 Inu mwaona zonse zimene Yehova Mulungu wanu wachita kwa mitundu yonseyi chifukwa cha inu. Ndi Yehova Mulungu wanu amene anakumenyerani nkhondo.
and ye seen alle thingis whiche youre Lord God hath do to alle naciouns `bi cumpas, hou he fauyt for you.
4 Tsono onani! Mitundu ya anthu otsalawa ndayipereka kwa mafuko anu pamodzi ndi mitundu ya anthu ya pakati pa Yorodani ndi Nyanja Yayikulu ya kumadzulo imene ndinayigonjetsa.
And now for he departide to you bi lot al the lond, fro the eest part of Jordan `til to the grete see, and many naciouns ben left yit,
5 Yehova Mulungu wanu ndiye adzawathamangitsa pamaso panu. Mudzatenga dziko lawo monga Yehova anakulonjezerani.
youre Lord God `schal distrie hem, and schal take awei fro youre face; and ye schulen welde the lond, as he bihiyte to you.
6 “Choncho khalani amphamvu, ndipo samalani kuti mumvere zonse zimene zalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose. Musapatuke pa malamulo onse amene alembedwamo.
Oneli be ye coumfortid, and be ye bisy, that ye kepe alle thingis that ben writun in the book of Moises lawe, and bowe not awei fro tho, nether to the riyt side nether to the left side,
7 Musagwirizane ndi mitundu ya anthu imene yatsala pakati panu. Musatchule mayina a milungu yawo kapena kuyitchula polumbira. Musayitumikire kapena kuyigwadira.
lest aftir that ye han entrid to the hethene men, that schulen be among you, ye swere in the name of `the goddis of hem, and ye serue tho goddis, and worschipe hem.
8 Koma mukuyenera kugwiritsa Yehova Mulungu wanu, monga mwachitira mpaka lero lino.
But cleue ye to youre Lord God, which thing ye han do `til in to this dai;
9 “Yehova wapirikitsa patsogolo panu mitundu ya anthu ikuluikulu ndi yolimba. Mpaka lero palibe amene watha kulimbana nanu.
and thanne the Lord God schal do awei in youre siyt grete folkis, and strongeste; and noon schal mow ayenstonde you.
10 Aliyense wa inu atha kuthamangitsa anthu 1,000 chifukwa Yehova Mulungu wanu ndiye amakumenyerani nkhondo, monga momwe analonjezera.
Oon of you schal pursue a thousynde men of enemyes, for youre Lord God schal fiyte for you, as he bihiyte.
11 Choncho samalitsani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu.
Be ye war bifore moost diligentli of this thing oneli, that ye loue youre Lord God.
12 “Koma ngati mubwerera mʼmbuyo ndi kuphatikizana ndi mitundu yotsalayi imene ili pakati panu ndi kumakwatirana nayo,
That if ye wolen cleue to the errouris of these folkis that dwellen among you, and wolen medle mariagis with hem, and couple frenschipis,
13 pamenepo mudziwe kuti Yehova, Mulungu wanu, sadzapirikitsa mitundu imeneyi pamaso panu, koma idzakhala ngati msampha kwa inu kapenanso khwekhwe lokukolani. Idzakhala ngati zikwapu pa msana panu kapenanso ngati minga mʼmaso mwanu mpaka mutatha psiti mʼdziko labwinoli limene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
wite ye riyt now, that `youre Lord God schal not do awei hem bifor youre face, but thei schulen be to you in to a dich, and a snare, and in to hirtyng of youre side, and in to stakis in youre iyen, til youre Lord God take awei you, and distrie fro this beste loond, which he yaf to you.
14 “Aliyense wa inu akudziwa mu mtima mwake komanso mʼmoyo mwake kuti zabwino zonse zimene Yehova Mulungu wanu anakulonjezani zachitika. Palibe lonjezo ndi limodzi lomwe limene silinakwaniritsidwe.
Lo! Y entre to dai in to the weye of al erthe; and ye schulen knowe `with al soule, that of al wordis whiche the Lord bihiyte hym silf to yyue to you, not oon passide in veyn.
15 Monga momwe Yehova Mulungu wanu wakuchitirani zabwino zonse zimene ananena kuti adzachita, Yehovayo angathenso kukuchitirani zoyipa zonse zimene waopseza, mpaka kukuchotsani mʼdziko lokoma limene anakupatsani.
Therfor as he fillide in werk that, that he bihiyte, and alle thingis bifelden `bi prosperite, so he schal brynge on you whateuer thing of yuelis he manaasside, til he take awei you, and distrie fro this beste lond, which he yaf to you.
16 Ngati muphwanya pangano la Yehova Mulungu wanu, limene anakulamulirani nʼkumapita kukatumikira milungu ina ndi kuyigwadira, Yehova adzakukwiyirani, ndiye mudzachotsedwa mʼdziko labwinoli limene Yehova wakupatsani.”
For ye braken the couenaunt of `youre Lord God, which he made with you, and serueden alien goddis, and worschipeden hem, sone and swiftli the strong veniaunce of the Lord schal rise `on to you; and ye schulen be takun awei fro this beste lond, which he yaf to you.

< Yoswa 23 >