< Yoswa 22 >

1 Pambuyo pake Yoswa anayitanitsa fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase,
Tada sazva Isus sinove Ruvimove i sinove Gadove i polovinu plemena Manasijina,
2 ndipo anawawuza kuti, “Inu mwachita zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani, ndipo mwamvera mu zonse zimene ndinakulamulirani.
I reèe im: vi držaste sve što vam je zapovjedio Mojsije sluga Gospodnji, i slušaste glas moj u svemu što sam vam zapovijedao.
3 Aisraeli anzanu simunawasiye nthawi yayitali yonseyi mpaka lero lino. Inu mwaonetsetsa kuti mwachita zonse zimene Yehova anakulamulani.
Ne ostaviste braæe svoje dugo vremena, do ovoga dana, i dobro èuvaste zapovijest Gospoda Boga svojega.
4 Tsono pakuti Yehova Mulungu wanu wapereka mpumulo kwa abale anu monga anayankhulira nawo, bwererani ku nyumba zanu ku dziko limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani, dziko limene lili pa tsidya la Yorodani kummawa.
A sada Gospod je Bog vaš smirio braæu vašu, kako im je rekao; sada dakle vratite se i idite u šatore svoje u zemlju našljedstva svojega, koju vam je dao Mojsije sluga Gospodnji s onu stranu Jordana.
5 Koma samalitsani kuti mumvere malamulo ndi malangizo amene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani: kukonda Yehova Mulungu wanu, kuchita zimene iye amafuna, kumvera malamulo ake, kukhala okhulupirika kwa Iye ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.”
Samo pazite dobro da vršite zapovijest i zakon, što vam je zapovjedio Mojsije sluga Gospodnji, da ljubite Gospoda Boga svojega i da hodite svijem putovima njegovijem, i èuvate zapovijesti njegove i držite ih se, i da mu služite svijem srcem svojim i svom dušom svojom.
6 Ndipo Yoswa anawadalitsa ndi kuwalola kuti apite ndipo anapitadi ku nyumba zawo.
I blagoslovi ih Isus, i otpusti ih da idu u svoje šatore.
7 Apa nʼkuti Mose atapereka dziko la Basani ku theka lina la fuko la Manase. Koma theka lina la fuko la Manase Yoswa analipatsa dziko la kumadzulo kwa Yorodani pamodzi ndi abale awo onse. Pamene Yoswa ankawatumiza kwawo anthu amenewa, anawadalitsa,
A polovini plemena Manasijina bješe dao Mojsije našljedstvo u Vasanu, a drugoj polovini dade Isus s braæom njihovom s ovu stranu Jordana k zapadu. I otpuštajuæi ih Isus u šatore njihove blagoslovi ih,
8 nawawuza kuti, “Mukubwerera kwanu ndi chuma chambiri. Muli ndi ngʼombe zambiri pamodzi ndi siliva, golide, mkuwa ndi chitsulo, ndiponso zovala zambiri. Izi zimene munafunkha kwa adani anu agawireni abale anu.”
I reèe im govoreæi: s velikim blagom vraæate se u šatore svoje, sa stokom vrlo mnogom; sa srebrom i zlatom i mjeðu i gvožðem i odijelom vrlo mnogim; podijelite plijen od neprijatelja svojih s braæom svojom.
9 Choncho mafuko a Rubeni, Gadi, pamodzi ndi theka la fuko la Manase anabwerera kwawo. Aisraeli ena onse anawasiya ku Silo mʼdziko la Kanaani. Tsono anapita ku dziko la Giliyadi, dziko limene linali lawo popeza analilandira potsata malamulo a Yehova kudzera mwa Mose.
I vrativši se sinovi Ruvimovi i sinovi Gadovi i polovina plemena Manasijina otidoše od sinova Izrailjevijeh iz Siloma, koji je u zemlji Hananskoj, iduæi u zemlju Galadsku, u zemlju našljedstva svojega, koju naslijediše, kako bješe Gospod zapovjedio preko Mojsija.
10 Atafika ku Geliloti, malo amene ali mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani mʼdziko la Kanaani, fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase anamanga guwa lansembe lalikulu pamenepo.
A kad doðoše na meðu Jordansku u zemlji Hananskoj, naèiniše sinovi Ruvimovi i sinovi Gadovi i polovina plemena Manasijina oltar ondje na Jordanu, oltar velik i naoèit.
11 Ndipo pamene Aisraeli ena onse anawuzidwa kuti anthu a fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase amanga guwa lansembe mʼmalire a Kanaani ku Geliloti, ku tsidya lathu lino la Yorodani,
I èuše sinovi Izrailjevi gdje se govori: gle, sinovi Ruvimovi i sinovi Gadovi i polovina plemena Manasijina naèiniše oltar prema zemlji Hananskoj na meði Jordanskoj, pokraj sinova Izrailjevijeh.
12 gulu lonse la Aisraeli linasonkhana ku Silo kuti lipite kukachita nawo nkhondo.
A kad èuše sinovi Izrailjevi, skupi se sav zbor sinova Izrailjevijeh u Silom da idu da se biju s njima.
13 Choncho Aisraeli anatumiza Finehasi mwana wa wansembe, Eliezara ku dziko la Giliyadi kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase.
I poslaše sinovi Izrailjevi k sinovima Ruvimovijem i sinovima Gadovijem i polovini plemena Manasijina u zemlju Galadsku Finesa sina Eleazara sveštenika,
14 Pamodzi ndi Finehasiyo anatumiza akuluakulu khumi ochokera ku fuko lililonse la Aisraeli. Aliyense mwa akuluakulu amenewa anali mtsogoleri wa banja limodzi la mafuko a Aisraeli.
I s njim deset knezova, po jednoga kneza od doma otaèkoga od svijeh plemena Izrailjevijeh, a svaki ih bješe poglavar u domu otaca svojih u tisuæama Izrailjevijem.
15 Atafika ku Giliyadi anawuza fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lija la fuko la Manase kuti,
A oni doðoše k sinovima Ruvimovijem i sinovima Gadovijem i polovini plemena Manasijina u zemlju Galadsku, i rekoše im govoreæi:
16 “Gulu lonse likukufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani mwachita chinthu chonyansa chotere potsutsana ndi Mulungu wa Israeli? Nʼchifukwa chiyani mwapatuka ndi kuleka kutsata Yehova podzimangira nokha guwa lansembe? Mwapandukiratu Yehova!
Ovako veli sav zbor Gospodnji: kakav je to grijeh kojim se ogriješiste Bogu Izrailjevu odvrativši se danas od Gospoda naèinivši oltar da se odmetnete danas od Gospoda?
17 Kodi tchimo lija la ku Peori ndi lochepa kwa inu? Paja Yehova analanga gulu lonse ndi mliri chifukwa cha tchimolo, ndipo mpaka lero tchimo limene lija tikanazunzika nalobe.
Malo li nam je grijeha Fegorova, od kojega se još nijesmo oèistili do danas i s kojega doðe pogibao na zbor Gospodnji,
18 Kodi inu tsono mufuna kupatuka kuleka kumutsata Yehova? “‘Ngati lero mumupandukira Yehovayo, ndiye kuti mawamawali Iye adzakwiyira gulu lonse wa Israeli.
Te se danas odvraæate od Gospoda, i odmeæete se danas od Gospoda, da se sjutra razgnjevi na sav zbor Izrailjev?
19 Ngati dziko limene inu mwatenga ndi loyipitsidwa, bwerani ku dziko la Yehova kumene kuli chihema chake kuja, ndipo mukhale nafe limodzi. Koma inu musawukire Yehova kapena kutisandutsa ife kukhala opanduka podzimangira guwa lansembe, kuwonjezera pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu.
Ako je zemlja našljedstva vašega neèista, prijeðite u zemlju našljedstva Gospodnjega, u kojoj stoji šator Gospodnji, i uzmite našljedstvo meðu nama; samo se ne odmeæite od Gospoda i ne odmeæite se od nas gradeæi sebi oltar mimo oltar Gospoda Boga našega.
20 Kumbukirani pamene Akani mwana wa Zera anakana kumvera lamulo la zinthu zoyenera kuwonongedwa, kodi suja mkwiyo wa Yehova unagwera gulu lonse la Israeli? Akaniyo sanafe yekha chifukwa cha tchimo lakelo.’”
Nije li se Ahan sin Zarin ogriješio o stvari proklete, te doðe gnjev na sav zbor Izrailjev? i on ne pogibe sam za grijeh svoj.
21 Tsono mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawayankha atsogoleri a mabanja a Israeli aja kuti,
A sinovi Ruvimovi i sinovi Gadovi i polovina plemena Manasijina odgovoriše i rekoše poglavarima tisuæa Izrailjevih:
22 “Wamphamvu uja, Mulungu ndiye Yehova! Wamphamvu uja Mulungu ndiye Yehova. Iyeyu ndiye akudziwa chifukwa chiyani tinachita zimenezi. Tikufunanso kuti inu mudziwe. Ngati tinachita izi mopandukira ndiponso moonetsa kusakhulupirira Yehova, lero lomwe lino musatisiye ndi moyo.
Gospod Bog nad bogovima, Gospod Bog nad bogovima, on zna, i Izrailj neka zna. Ako smo radi odmetati se i griješiti Gospodu, neka nas ne saèuva danas.
23 Ngati tinapandukira Yehova ndi kuleka kumutsata pamene tinadzimangira guwa loti tizipserezerapo nsembe kapena kupereka nsembe zaufa, kapena nsembe za mtendere, Yehova yekha ndiye atilange.
Ako smo naèinili oltar da se odvratimo od Gospoda ili da prinosimo na njemu žrtve paljenice ili dare ili da prinosimo na njemu žrtve zahvalne, Gospod neka traži.
24 “Ayi! Ife tinachita izi kuopa kuti tsiku lina zidzukulu zanu zingadzanene kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Kodi inu mukufuna chiyani kwa Yehova Mulungu wa Israeli?
Nego to uèinismo bojeæi se ovoga: rekosmo: sjutra æe reæi sinovi vaši sinovima našim govoreæi: šta vi imate s Gospodom Bogom Izrailjevim?
25 Yehova anayika mtsinje wa Yorodani kukhala malire pakati pa ife ndi inu, anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi. Inuyo mulibe gawo mwa Yehova.’ Tsono mwina zidzukulu zanuzo nʼkudzaletsa zathu kupembedza Yehova.
Meðu je postavio Gospod izmeðu nas i vas, sinovi Ruvimovi i Gadovi, Jordan; vi nemate dijela u Gospoda. Te æe sinovi vaši odbiti sinove naše da se ne boje Gospoda.
26 “Nʼchifukwa chake tinaganiza kuti, ‘Tiyeni timange guwa lansembe, koma osati kuti tiziperekapo nsembe zopsereza kapena zopereka.’
Zato rekosmo: uèinimo tako, i naèinimo oltar, ne za žrtvu paljenicu ni za drugu žrtvu,
27 Koma mosiyana ndi zimenezi, guwali likhale umboni pakati pa ife ndi inu ndiponso mibado imene ikubwerayo, kuti ife timapembedzanso Yehova ndi nsembe zathu zopsereza, zopereka, ndiponso nsembe za mtendere. Motero mʼtsogolo muno zidzukulu zanu sizidzatha kunena kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Inu mulibe gawo mwa Yehova!’
Nego da bude svjedok meðu nama i vama, i meðu natražjem našim nakon nas, da bismo služili Gospodu pred njim žrtvama svojim paljenicama i prinosima svojim, i žrtvama svojim zahvalnim, i da ne bi rekli kadgod sinovi vaši sinovima našim: vi nemate dijela u Gospoda.
28 “Ndipo ife tinati kuti, ‘Ngati iwo adzatiyankhulira kapena kuyankhulira zidzukulu zathu motero mʼtsogolo muno, ife tidzayankha kuti, onani guwa lansembe, lofanana ndi lomwe makolo athu anamanga osati loperekerapo nsembe zopsereza kapena nsembe zina koma ngati umboni pakati pa inu ndi ife.’
Jer rekosmo: ako kad reku tako nama ili natražju našemu, tada æemo im kazati: vidite sliku od oltara Gospodnjega koju naèiniše oci naši ne za žrtvu paljenicu ni za drugu žrtvu, nego da je svjedoèanstvo meðu nama i vama.
29 “Sizingatheke konse kuti ife lero nʼkupandukira Yehova. Ife sitingapatuke kuleka kumutsata Yehova ndi kumanga guwa lina la nsembe zopsereza, nsembe za zakudya, ndi nsembe zina zopikisana ndi guwa la Yehova, Mulungu wathu limene lili patsogolo pa Hema ya Yehova mʼmene amakhalamo.”
Ne daj Bože da se odmeæemo Gospodu i da se danas odvraæamo od Gospoda naèinivši oltar za žrtvu paljenicu, za dar ili za prinos, mimo oltar Gospoda Boga našega, koji je pred šatorom njegovijem.
30 Tsono Finehasi wansembe ndi atsogoleri a gululo amene anali naye atamva zimene anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lakummawa la fuko la Manase ananena, anakondwera kwambiri.
A kad èu Fines sveštenik i knezovi od zbora, poglavari od tisuæa Izrailjevih koji bijahu s njim, rijeèi koje im rekoše sinovi Ruvimovi i sinovi Gadovi i sinovi Manasijini, bi im po volji.
31 Ndipo Finehasi wansembe, mwana wa Eliezara anati kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi Manase, “Lero tadziwa kuti Yehova ali nafe chifukwa zimene mwachitazi simunawukire nazo Yehova. Inu mwapulumutsa Aisraeli onse ku chilango cha Yehova.”
I reèe Fines sin Eleazara sveštenika sinovima Ruvimovijem i sinovima Gadovijem i sinovima Manasijinim: danas poznasmo da je meðu nama Gospod kad se ne ogriješiste Gospodu tijem grijehom, i saèuvaste sinove Izrailjeve od ruku Gospodnjih.
32 Ndipo Finehasi mwana wa wansembe Eliezara, pamodzi ndi atsogoleriwo anachoka ku Giliyadi nasiya anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi nabwerera ku Kanaani kwa Aisraeli anzawo, ndipo anakafotokoza zonsezi.
I Fines sin Eleazara sveštenika i oni knezovi vratiše se od sinova Ruvimovijeh i od sinova Gadovijeh iz zemlje Galadske u zemlju Hanansku k sinovima Izrailjevijem, i javiše im stvar.
33 Mawu amenewa anakondweretsa Aisraeli onse ndipo anayamika Mulungu. Choncho sanakambenso zopita ku nkhondo kukawononga dziko limene Arubeni ndi Agadi ankakhalamo.
I bi po volji sinovima Izrailjevijem; i hvališe Boga sinovi Izrailjevi, i ne govoriše više da idu da se biju s njima da potru zemlju, u kojoj žive sinovi Ruvimovi i sinovi Gadovi.
34 Arubeni ndi Agadi anatcha guwalo kuti Mboni: Mboni pakati pathu kuti Yehova ndi Mulungu.
I prozvaše sinovi Ruvimovi i sinovi Gadovi onaj oltar Ed govoreæi: svjedok je meðu nama da je Gospod Bog.

< Yoswa 22 >