< Yoswa 18 >

1 Atagonjetsa dziko lonse Aisraeli anasonkhana ku Silo ndipo anayimikako tenti ya msonkhano.
And alle the sones of Israel weren gaderid in Silo, and there thei `settiden faste the tabernacle of witnessing; and the lond was suget to hem.
2 Koma pa nthawiyo nʼkuti mafuko asanu ndi awiri a Aisraeli asanalandire cholowa chawo.
Sotheli seuene linagis of the sones of Israel dwelliden, that hadden not yit takun her possessiouns.
3 Ndipo Yoswa anati kwa Aisraeli, “Kodi mudikira mpaka liti kuti mulowe ndi kulanda dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani?
To whiche Josue seide, Hou longe faden ye `bi cowardise, `ethir slouthe, and entren not to welde the lond, which the Lord God of youre fadris yaf to you?
4 Sankhani amuna atatu kuchokera ku fuko lililonse ndipo ine ndidzawatuma kuti akayendere dzikolo ndi kukalilembera bwino kuti ndiligawe kukhala lawo. Akatero, abwererenso kwa ine.
Chese ye of ech lynage thre men, that Y sende hem, and thei go, and cumpasse the lond; and that thei discryue `the lond bi the noumbre of ech multitude, and brynge to me that, that ye han discriued.
5 Aligawe dzikolo mʼzigawo zisanu ndi ziwiri; fuko la Yuda lidzakhale ndi dziko lake la kummwera ndi nyumba ya Yosefe ikhalebe mʼdziko lawo la kumpoto.
Departe ye the lond to you in to seuene partis; Judas be in hise termes at the south coost, and `the hows of Joseph at the north;
6 Mudzalembe mawu ofotokoza za zigawo zisanu ndi ziwiri za dzikolo, ndi kubwera nawo kwa ine. Tsono ineyo ndidzakuchitirani maere pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
discryue ye `the myddil lond bitwixe hem in to seuene partis; and thanne ye schulen come to me, that Y sende lot to you here bifor youre Lord God;
7 Alevi asakhale ndi dziko pakati panu, chifukwa gawo lawo ndi kutumikira Yehova pa ntchito ya unsembe. Ndipo Gadi, Rubeni ndi theka la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo kummawa kwa Yorodani. Mose mtumiki wa Yehova ndiye anawapatsa.”
for the part of Leuytis is not among you, but the preesthod of the Lord, this is the eritage `of hem. Forsothe Gad, and Ruben, and the half lynage of Manasses hadden take now her possessiouns ouer Jordan, at the eest coost, whiche possessiouns Moises, the `seruaunt of the Lord, yaf to hem.
8 Anthuwo akupita kukalembera dzikolo, Yoswa anawalangiza kuti, “Pitani mukayendere ndi kulembera dzikolo. Kenaka mukabwere kwa ine, ndidzakuchitirani maere kuno ku Silo pamaso pa Yehova.”
And whanne the men hadden rise to go, to discryue the lond, Josue comaundide to hem, and seide, Cumpasse ye the lond, and discryue it, and turne ayen to me, that Y sende lot to you here in Silo, bifore youre Lord God.
9 Ndipo anthu anachoka ndi kukayendera dziko lonse. Iwo analemba bwinobwino mʼbuku za dzikolo, mzinda ndi mzinda. Analigawa magawo asanu ndi awiri, ndipo anabwerera kwa Yoswa ku misasa ya ku Silo.
And so thei yeden, and cumpassiden that lond, and departiden `in to seuene partis, writynge in a book; and thei turneden ayen to Josue, in to the castels in Silo.
10 Pambuyo pake Yoswa anawachitira maere ku Silo pamaso pa Yehova, ndipo fuko lililonse la Israeli analigawira dziko lake.
Which Josue sente lottis bifor the Lord God in Silo, and departide the lond to the sones of Israel, in to seuene partis.
11 Maere anagwera mabanja a fuko la Benjamini. Dziko limene anapatsidwa linali pakati pa fuko la Yuda ndi fuko la Yosefe:
And the firste lot of the sones of Beniamyn, bi her meynees, stiede, that thei schulden welde the lond bitwixe the sones of Juda and the sones of Joseph.
12 Mbali ya kumpoto malire awo anayambira ku Yorodani nalowera chakumpoto kwa matsitso a ku Yeriko kulowera cha kumadzulo kwa dziko la ku mapiri ndi kukafika ku chipululu cha Beti-Aveni.
And the terme of hem was ayens the north fro Jordan, and passide bi the side of Jerico of the north coost; and it stiede fro thennus ayens the west to the hilli places, and it cam to the wildirnesse of Bethauen;
13 Kuchokera kumeneko malirewo analoza ku Luzi nadutsa mʼmbali mwa mapiri kummwera kwa Luzi (ndiye Beteli) ndipo anatsika mpaka ku Ataroti Adari, ku mapiri a kummwera kwa Beti-Horoni wa Kumunsi.
and it passide bisidis Luza to the south; thilke is Bethel; and it goith doun in to Astoroth Adar, in to the hil which is at the south of lowere Betheron; and is bowid,
14 Ndipo malirewo analowanso kwina, analunjika kummwera kuchokera kumadzulo kwake kwa phiri loyangʼanana ndi Beti-Horoni, mpaka ku mzinda wa Kiriyati Baala (ndiye Kiriati Yearimu), mzinda wa anthu a fuko la Yuda. Amenewa ndiye anali malire a mbali ya kumadzulo.
and cumpassith ayens the see, at the south of the hil that biholdith Betheron ayens the north; and the outgoyngis therof ben in to Cariathbaal, which is clepid also Cariathiarym, the citee of the sones of Juda; this is the greet coost ayens the see, at the west.
15 Malire a kummwera anayambira mʼmphepete mwenimweni mwa Kiriati Yearimu napita kumadzulo mpaka kukafika ku akasupe a Nefitowa.
Sotheli fro the south, bi the part of Cariathiarym, the terme goith out ayens the see, and cometh til to the wel of watris of Nepthoa;
16 Malire anatsikira mʼmphepete mwa phiri loyangʼanana ndi chigwa cha Beni Hinomu, kumpoto kwa chigwa cha Refaimu. Anapitirira kutsikira ku chigwa cha Hinomu kummwera kwa chitunda cha Ayebusi mpaka ku Eni Rogeli.
and it goith doun in to the part of the hil that biholdith the valei of the sones of Ennon, and is ayens the north coost, in the laste part of the valey of Raphaym; and Jehennon, that is, the valei of Ennon, goith doun bi the side of Jebusei, at the south, and cometh to the welle of Rogel,
17 Kenaka anakhotera kumpoto kupita ku Eni-Semesi, kupitirira mpaka ku Geliloti amene amayangʼanana ndi pokwera pa Adumimu. Kenaka malire anatsikira ku Mwala wa Bohani, mwana wa Rubeni.
and passith to the north, and goith out to Emsemes, that is, the welle of the sunne,
18 Anabzola cha kumpoto kwa chitunda cha Beti Araba ndi kutsikabe mpaka ku chigwa cha Yorodani.
and passith to the litle hillis that ben ayens the stiyng of Adomyn; and it goith doun to Taben Boen, that is, the stoon of Boen, sone of Ruben, and passide bi the side of the north to the feeldi places; and it goith doun in to the pleyn,
19 Anabzolanso cha kumpoto kwa chitunda cha Beti-Hogila kukafika cha kumpoto ku gombe la Nyanja ya Mchere kumene mtsinje wa Yorodani umathirirako, cha kummwera kwenikweni. Awa anali malire a kummwera.
and passith forth ayens the north to Bethagala; and the outgoyngis therof ben ayens the arm of the salteste see, fro the north, in the ende of Jordan at the south coost,
20 Yorodani ndiye anali malire a mbali ya kummawa. Awa anali malire a dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira.
which is the terme therof fro the eest. This is the possessioun of the sones of Beniamyn, bi her termes in cumpas, and bi her meynees;
21 Mabanja a fuko la Benjamini anali ndi mizinda iyi; Yeriko, Beti-Hogila, Emeki Kezizi,
and the citees therof weren Jerico, and Bethagla, and the valei of Casis,
22 Beti-Araba, Zemaraimu, Beteli
Betharacha, and Samaraym,
23 Avimu, Para, Ofiri,
and Bethel, and Anym, and Affara,
24 Kefari-Amoni, Ofini ndi Geba, mizinda khumi ndi awiri ndi midzi yake
and Offira, the toun of Hesmona, and Offym, and Gabee, twelue citees, and `the townes of tho;
25 Panalinso Gibiyoni, Rama, Beeroti,
Gabaon, and Rama,
26 Mizipa, Kefira, Moza
and Beroth, and Mesphe, and Caphera, and Ammosa,
27 Rekemu, Iripeeli, Tarala,
and Recem, Jarephel, and Tharela,
28 Zera Haelefu, mzinda wa Ayebusi (ndiye kuti Yerusalemu) Gibeya ndi Kiriati, mizinda 14 ndi midzi yake. Limeneli ndilo dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira kuti likhale lawo.
and Sela, Heleph, and Jebus, which is Jerusalem, Gabaath, and Cariath, fouretene citees and `the townes of tho; this is the possessioun of the sones of Beniamyn, bi her meynees.

< Yoswa 18 >