< Yoswa 17 >

1 Gawo lina la dzikolo linapatsidwa kwa mabanja ena a fuko la Manase, mwana woyamba kubadwa wa Yosefe. Makiri anali mwana woyamba kubadwa wa Manase ndiponso kholo la anthu okhala ku Giliyadi. Popeza kuti iye anali munthu wankhondo, analandira Giliyadi ndi Basani.
Forsothe lot felde in to the lynage of Manasse, for he is the firste gendrid sone of Joseph; lot felde to Machir, the firste gendrid sone of Manasses, to the fadir of Galaad, that was a werriour, and he hadde possessioun Galaad and Basan.
2 Mabanja ena otsala a fuko la Manase amene analandira dziko ndi awa: Abiezeri, Heleki, Asirieli, Sekemu, Heferi ndi Semida. Izi ndi zidzukulu zina zazimuna za Manase mwana wa Yosefe ndiponso eni mbumba.
And lot felde to the othere of the sones of Manasses, bi her meynees; to the sones of Abiezer, and to the sones of Heleth, and to the sones of Hesriel, and to the sones of Sichen, and to the sones of Epher, and to the sones of Semyda; these ben the sones of Manasse, sone of Joseph, the male children, bi her meynees.
3 Panali Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri mwana wa Manase. Iyeyu analibe ana aamuna koma aakazi okhaokha ndipo mayina awo ndi awa: Mahila, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.
Sotheli to Salphaat, the sone of Epher, sone of Galaad, sone of Machir, sone of Manasses, weren not sones, but douytris aloone; of whiche these ben the names, Maala, and Noa, and Eegla, and Melcha, and Thersa.
4 Iwo anapita kwa Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni, ndi atsogoleri ndipo anati: “Yehova analamula Mose kuti ife ndi alongo athu atipatse cholowa chathu.” Choncho iwowo pamodzi ndi abale a abambo awo anawapatsa dera lina la dzikolo kuti likhale monga mwa lamulo la Yehova.
And thei camen in the siyt of Eleazar, preest, and of Josue, sone of Nun, and of the princes, and seiden, The Lord comaundide bi the hond of Moises, that possessioun should be youun to vs in the myddis of oure britheren. And Josue yaf to hem possessioun, bi comaundement of the Lord, in the myddis of the britheren of her fadir.
5 Choncho kuwonjezera pa mayiko a Giliyadi ndi Basani kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Manase analandiranso magawo khumi
And ten cordis, `that is, londis mesurid bi ten cordis, felden to Manasses, without the lond of Galaad and of Basan biyende Jordan;
6 chifukwa ana aakazi a fuko la Manase analandira cholowa chawo pakati pa ana aamuna. Dziko la Giliyadi linali dziko la zidzukulu zonse za Manase.
for the douytris of Manasses weldiden eritage in the myddis of the sones of hym. Sotheli the lond of Galaad felde in to the part of the sones of Manasses, that weren residue.
7 Malire a dziko la Manase anayambira ku Aseri, ndipo anakafika ku Mikimetati kummawa kwa Sekemu. Tsono malire anapita kummwera kuloza kwa anthu a ku Eni-Tapuwa.
And the terme of Manasses was fro Azer Machynathath, that biholdeth Sichem, and goith out to the riyt side, bisidis the dwelleris of the welle Taphue;
8 (Manase anatenga dziko la Tapuwa, koma mzinda wa Tapuwawo, umene unali mʼmalire mwa Manase unali wa fuko la Efereimu).
for the lond of Thaphue, which is bisidis the terme of Manasses, and of the sones of Effraym, felde in the lot of Manasses.
9 Ndipo malire ake anapitirira kummwera mpaka ku mtsinje wa ku Kana. Mizinda ya kummwera kwa mtsinjewo inali ya fuko la Efereimu ngakhale kuti inali mʼdziko la Manase. Malire a fuko la Manase anapita kumpoto kwa mtsinje wa Kana ndi kukathera ku Nyanja.
And the terme of the valey of place of rehedis goith doun in the south of the stronde of the citees of Effraym, that ben in the myddis of the citees of Manasses. The terme of Manasses is fro the north of the stronde, and the goyng out therof goith to the see;
10 Dziko la kummwera linali la Efereimu ndipo la kumpoto linali la Manase. Dziko la Manase linafika ku nyanja ndipo linachita malire ndi Aseri, kumpoto ndiponso Isakara, kummawa.
so that the possessioun of Effraym is fro the south, and the possessioun of Manasses fro the north, and the see closith euer either; and tho ben ioyned to hem silf in the linage of Aser fro the north, and in the lynage of Isachar fro the eest.
11 Mʼdziko la Isakara ndi Aseri, Manase analinso ndi mizinda ya Beti-Seani ndi Ibuleamu pamodzi ndi midzi yawo yozungulira. Panalinso Akanaani amene ankakhala ku Dori, Endori, Taanaki ndi Megido pamodzi ndi mizinda yozungulira (wachitatu pa mʼndandandawu ndi Nafati Dori).
And the eritage of Manasses was in Isachar and in Aser, Bersan, and the townes therof, and Jeblaan, with hise townes, and the dwellers of Dor, with her citees; and the dwelleris of Endor, with her townes, and also the dwelleris of Thanath, with her townes, and the dwelleris of Maiedo, with her townes, and the thridde part of the citee Nophet.
12 Komabe anthu a fuko la Manase sanathe kuwapirikitsa anthu okhala mʼmizinda imeneyi. Choncho Akanaani anakhalabe mʼmizindayi.
And the sones of Manasses miyten not distrie these citees, but Cananei bigan to dwelle in this lond.
13 Ngakhale Aisraeli anali a mphamvu mʼdzikomo, sanapirikitse Akanaani onse koma anangowasandutsa kukhala akapolo.
Sotheli aftir that the sones of Israel weren stronge, thei maden suget Cananeis, and maden tributaries to hem silf, and killiden not Cananeis.
14 Anthu a fuko la Yosefe anati kwa Yoswa, “Chifukwa chiyani mwatipatsa gawo limodzi lokha la dziko kuti likhale cholowa chathu? Ife tilipo anthu ambiri popeza Yehova watidalitsa kwambiri.”
And the sones of Joseph spaken to Josue, and seiden, Whi hast thou youe to me lond in to possessioun of o lot and part, sithen Y am of so greet multitude, and the Lord hath blesside me, `that is, hath alargid me in children?
15 Yoswa anayankha kuti, “Ngati muli ambiri ndipo dziko la ku mapiri la Efereimu lakucheperani kwambiri, lowani ku nkhalango mudule mitengo, mudzikonzere malo akuti mukhalemo, mʼdziko la Aperezi ndi Arefai.”
To whiche Josue seide, If thou art myche puple, stie thou into the wode, and kitte doun to thee spaces in the lond of Feresei, and of Raphaym, for the possessioun of the hil of Effraym is streiyt to thee.
16 Tsono zidzukulu za Yosefe zinati, “Dziko la ku mapiri ndi losatikwaniradi, komanso Akanaani onse amene akukhala ku chigwa pamodzi ndi amene akukhala ku Beti-Seani ndi madera awo ndiponso amene ali ku chigwa cha Yezireeli ali ndi magaleta azitsulo.”
To whom the sones of Joseph answerden, We moun not stie to the hilli places, sithen Cananeis, that dwellen in the `lond of the feeld, vsen ironne charis; in which lond Bersan, with hise townes, and Jesrael, weldynge the myddil valey, ben set.
17 Koma Yoswa anawuza zidzukulu za Yosefe, za fuko la Efereimu ndi za fuko la Manase kuti, “Inu mulipodi ambiri ndiponso amphamvu. Simulandira gawo limodzi lokha,
And Josue seide to the hows of Joseph, and of Effraym, and of Manasses, Thou art myche puple, and of greet strengthe; thou schalt not haue o lot,
18 dziko la ku mapiri lidzakhalanso lanu. Ngakhale kuti ndi nkhalango yokhayokha koma inu mudzadula mitengo yake ndipo lidzakhala lanu mpaka kumapeto. Ngakhale kuti Akanaani ali ndi magaleta azitsulo ndiponso kuti iwo ndi amphamvu, koma inu mudzawapirikitsa.”
but thou schalt passe to the hil, and thou schalt kitte doun to thee; and thou schalt clense spaces to dwelle. And thou schalt mow go forth ferthere, whanne thou hast distried Cananei, whom thou seist to haue irone charis, and to be moost strong.

< Yoswa 17 >