< Yoweli 2 >

1 Lizani lipenga mu Ziyoni. Chenjezani pa phiri langa loyera. Onse okhala mʼdziko anjenjemere, pakuti tsiku la Yehova likubwera, layandikira;
Synge ye with a trumpe in Sion, yelle ye in myn hooli hil. Alle the dwelleris of erthe be disturblid; for the dai of the Lord cometh,
2 tsiku la mdima ndi chisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani. Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri, gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera, gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.
for the dai of derknessis and of myist is niy, the dai of cloude and of whirlewynde. As the morewtid spred abrood on hillis, a myche puple and strong. Noon was lijk it fro the bigynnyng, and after it schal not be, til in to yeeris of generacioun and of generacioun.
3 Patsogolo pawo moto ukupsereza, kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu. Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni, kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu, kulibe kanthu kotsalapo.
Bifore the face therof schal be fier deuourynge, and after it schal be brennynge flawme; as a gardyn of liking the lond schal be bifor him, and wildirnesse of desert schal be after him, and noon is that schal ascape him.
4 Maonekedwe awo ali ngati akavalo; akuthamanga ngati akavalo ankhondo.
The lokyng of hem schal be as the lokyng of horsis, and as horse men so thei schulen renne.
5 Akulumpha pamwamba pa mapiri ndi phokoso ngati la magaleta, ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu, ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.
As the sown of cartis on the heedis of hillis thei schulen skippe; as the sowne of the flawme of fier deuourynge stobil, as a strong puple maad redi to batel.
6 Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima; nkhope iliyonse imagwa.
Puplis schulen be turmentid of the face therof, alle facis schulen be dryuun in to a pot.
7 Amathamanga ngati ankhondo; amakwera makoma ngati asilikali. Onse amayenda pa mizere, osaphonya njira yawo.
As stronge men thei schulen renne, as men werriours thei schulen stie on the wal. Men schulen go in her weies, and thei schulen not bowe awei fro her pathis.
8 Iwo sakankhanakankhana, aliyense amayenda molunjika. Amadutsa malo otchingidwa popanda kumwazikana.
Ech man schal not make streyt his brother, ech man schal go in his path; but also thei schulen falle doun bi wyndows, and schulen not be hirt.
9 Amakhamukira mu mzinda, amathamanga mʼmbali mwa khoma. Amakwera nyumba ndi kulowamo; amalowera pa zenera ngati mbala.
Thei schulen entre in to the citee, thei schulen renne on the wal; thei schulen stie on housis, thei schulen entre as a niyt theef bi wyndows.
10 Patsogolo pawo dziko limagwedezeka, thambo limanjenjemera, dzuwa ndi mwezi zimachita mdima, ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.
The erthe tremblide of his face, heuenys weren mouyd, the sunne and the moone weren maad derk, and sterris withdrowen her schynyng.
11 Yehova amabangula patsogolo pawo, gulu lake lankhondo ndi losawerengeka, ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake. Tsiku la Yehova ndi lalikulu; ndi loopsa. Ndani adzapirira pa tsikulo?
And the Lord yaf his vois bifor the face of his oost, for hise oostis ben ful manye; for tho ben stronge, and doen the word of hym. For the dai of the Lord is greet, and ful ferdful, and who schal suffre it?
12 “Ngakhale tsopano, bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.
Now therfor seith the Lord, Be ye conuertid to me in al youre herte, in fastyng, and wepyng, and weilyng;
13 Ngʼambani mtima wanu osati zovala zanu. Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu, pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka, ndipo amaleka kubweretsa mavuto.
and kerue ye youre hertis, and not youre clothis, and be ye conuertid to youre Lord God, for he is benygne, and merciful, pacient, and of myche merci, and abidynge, ether foryyuynge, on malice.
14 Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni, nʼkutisiyira madalitso, a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa kwa Yehova Mulungu wanu.
Who woot, if God be conuertid, and foryyue, and leeue blessyng aftir hym? sacrifice and moist sacrifice to oure Lord God.
15 Lizani lipenga mu Ziyoni, lengezani tsiku losala zakudya, itanitsani msonkhano wopatulika.
Synge ye with a trumpe in Sion, halewe ye fastyng, clepe ye cumpany; gadere ye togidere the puple, halewe ye the chirche,
16 Sonkhanitsani anthu pamodzi, muwawuze kuti adziyeretse; sonkhanitsani akuluakulu, sonkhanitsani ana, sonkhanitsani ndi oyamwa omwe. Mkwati atuluke mʼchipinda chake, mkwatibwi atuluke mokhala mwake.
gadere ye togidere elde men, gadere ye togidere litle children, and soukynge the brestis; a spouse go out of his bed, and a spousesse of hir chaumbre.
17 Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova, alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova. Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu. Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka, kuti anthu a mitundu ina awalamulire. Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti, ‘Ali kuti Mulungu wawo?’”
Prestis, the mynystris of the Lord, schulen wepe bitwixe the porche and the auter, and schulen seie, Lord! spare thou, spare thi puple, and yyue thou not thin eritage in to schenschipe, that naciouns be lordis of hem. Whi seien thei among puplis, Where is the God of hem?
18 Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake ndi kuchitira chisoni anthu ake.
The Lord louyde gelousli his lond, and sparide his puple.
19 Yehova adzawayankha kuti, “Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta ndipo mudzakhuta ndithu; sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo kwa anthu a mitundu ina.
And the Lord answeride, and seide to his puple, Lo! Y schal sende to you wheete, and wyn, and oile, and ye schulen be fillid with tho; and Y schal no more yyue you schenschipe among hethene men.
20 “Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu, kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu, gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo. Ndipo mitembo yawo idzawola, fungo lake lidzamveka.” Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
And Y schal make hym that is at the north fer fro you; and Y schal cast hym out in to a lond with out weie, and desert; his face ayens the eest see, and the laste part therof at the last see; and the stynk therof schal stie, and the root therof schal stie, for he dide proudli.
21 Iwe dziko usachite mantha; sangalala ndipo kondwera. Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
Erthe, nyle thou drede, make thou ful out ioye, and be glad; for the Lord magnefiede that he schulde do.
22 Inu nyama zakuthengo, musachite mantha, pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira. Mitengo ikubala zipatso zake; mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.
Beestis of the cuntrei, nyle ye drede, for the faire thingis of desert buriowneden; for the tre brouyte his fruyt, the fige tre and vyner yauen her vertu.
23 Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani, kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu, pakuti wakupatsani mvula yoyambirira mwachilungamo chake. Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka, mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.
And the sones of Sion, make ye ful out ioie, and be ye glad in youre Lord God, for he yaf to you a techere of riytfulnesse, and he schal make morewtid reyn and euentid reyn to come doun to you, as in the bigynnyng.
24 Pa malo opunthira padzaza tirigu; mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.
And cornflooris schulen be fillid of wheete, and pressours schulen flowe with wyn, and oile.
25 “Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe, dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono, dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka; gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.
And Y schal yelde to you the yeris whiche the locuste, bruke, and rust, and wort worm, my greet strengthe, eet, which Y sente in to you.
26 Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta, ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu, amene wakuchitirani zodabwitsa; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
And ye schulen ete etyng, and ye schulen be fillid; and ye schulen herie the name of youre Lord God, that made merueils with you; and my puple schal not be schent with outen ende.
27 Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli, kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndi kuti palibenso wina; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
And ye schulen wite, that Y am in the myddis of Israel; and Y am youre Lord God, and `noon is more; and my puple schal not be schent with outen ende.
28 “Ndipo patapita nthawi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera, nkhalamba zanu zidzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya.
And it schal be, aftir these thingis Y schal schede out my spirit on ech man, and youre sones and youre douytris schulen profesie; youre elde men schulen dreme dremes, and youre yonge men schulen se visiouns.
29 Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.
But also Y schal schede out my spirit on my seruauntis, and handmaydis, in tho daies;
30 Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi pa dziko lapansi, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
and Y schal yyue grete wondris in heuene, and in erthe, blood, and fier, and the heete of smoke.
31 Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.
The sunne schal be turned in to derknessis, and the moone in to blood, bifor that the greet dai and orrible of the Lord come.
32 Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka; pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni ndi mu Yerusalemu, monga Yehova wanenera, pakati pa otsala amene Yehova wawayitana.
And it schal be, ech that clepith to helpe the name of the Lord, schal be saaf; for whi saluacioun schal be in the hil of Sion and in Jerusalem, as the Lord seide, and in the residue men, whiche the Lord clepith.

< Yoweli 2 >