< Yoweli 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.
The word of the Lord is this, that was maad to Joel, the sone of Phatuel.
2 Inu akuluakulu, imvani izi; mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko. Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu, kapena mʼnthawi ya makolo anu?
Elde men, here ye this, and alle dwelleris of the lond, perseyue ye with eeris. If this thing was don in youre daies, ether in the daies of youre fadris.
3 Muwafotokozere ana anu, ndipo ana anuwo afotokozere ana awo, ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.
Of this thing telle ye to your sones, and your sones telle to her sones, and the sones of hem telle to another generacioun.
4 Chimene dzombe losamera mapiko lasiya dzombe lowuluka ladya; chimene dzombe lowuluka lasiya dzombe lalingʼono ladya; chimene dzombe lalingʼono lasiya chilimamine wadya.
A locuste eet the residue of a worte worm, and a bruke eet the residue of a locuste, and rust eet the residue of a bruke.
5 Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire! Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo; lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano, pakuti wachotsedwa pakamwa panu.
Drunken men, wake ye, and wepe; and yelle ye, alle that drynken wyn in swetnesse; for it perischide fro youre mouth.
6 Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa, wamphamvu ndi wosawerengeka; uli ndi mano a mkango, zibwano za mkango waukazi.
For whi a folc strong and vnnoumbrable stiede on my lond. The teeth therof ben as the teeth of a lioun, and the cheek teeth therof ben as of a whelp of a lioun.
7 Wawononga mphesa zanga ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu. Wakungunula makungwa ake ndi kuwataya, kusiya nthambi zake zili mbee.
It settide my vyner in to desert, and took awei the riynde of my fige tre. It made nakid and spuylide that vyner, and castide forth; the braunchis therof ben maad white.
8 Lirani ngati namwali wovala chiguduli, chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.
Weile thou, as a virgyn gird with a sak on the hosebonde of hir tyme of mariage.
9 Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova. Ansembe akulira, amene amatumikira pamaso pa Yehova.
Sacrifice and moist sacrifice perischide fro the hous of the Lord; and preestis, the mynystris of the Lord, moureneden.
10 Minda yaguga, nthaka yauma; tirigu wawonongeka, vinyo watsopano watha, mitengo ya mafuta yauma.
The cuntrey is maad bare of puple. The erthe mourenyde; for whete is distried. Wyn is schent, and oile was sijk, ether failide.
11 Khalani ndi nkhawa, inu alimi, lirani mofuwula inu alimi a mphesa; imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele, pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.
The erthe tilieris ben schent, the vyn tilieris yelliden on wheete and barli; for the ripe corn of the feeld is perischid.
12 Mpesa wauma ndipo mtengo wamkuyu wafota; makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi, mitengo yonse ya mʼmunda yauma. Ndithudi chimwemwe cha anthu chatheratu.
The vyner is schent; and the fige tre was sijk. The pomgarnate tre, and the palm tre, and the fir tre, and alle trees of the feeld drieden vp; for ioie is schent fro the sones of men.
13 Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani; lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe. Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse, inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga; pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.
Ye prestis, girde you, and weile; ye mynystris of the auter, yelle. Mynystris of my God, entre ye, ligge ye in sak; for whi sacrifice and moist sacrifice perischide fro the hous of youre God.
14 Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya, itanani msonkhano wopatulika. Sonkhanitsani akuluakulu ndi anthu onse okhala mʼdziko ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu ndipo alirire Yehova.
Halewe ye fastyng, clepe ye cumpeny, gadere ye togidere elde men, and alle dwelleris of the erthe in to the hous of youre God; and crie ye to the Lord, A!
15 Kalanga ine tsikulo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
A! A! to the dai; for the dai of the Lord is niy, and schal come as a tempest fro the myyti.
16 Kodi chakudya chathu sichachotsedwa ife tikuona? Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?
Whether foodis perischiden not bifore youre iyen; gladnesse and ful out ioie perischide fro the hous of youre God?
17 Mbewu zikunyala poti pansi ndi powuma. Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka; nkhokwe zapasuka popeza tirigu wauma.
Beestis wexen rotun in her drit. Bernes ben distried, celeris ben distried, for wheete is schent.
18 Taonani mmene zikulirira ziweto; ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku chifukwa zilibe msipu; ngakhalenso nkhosa zikusauka.
Whi weilide a beeste? whi lowiden the flockis of oxun and kien? for no lesewe is to hem; but also the flockis of scheep perischiden.
19 Kwa Inu Yehova ndilirira, pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo, malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.
Lord, Y schal crye to thee, for fier eet the faire thingis of desert, and flawme brente all the trees of the cuntrei.
20 Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu; timitsinje tonse taphwa ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.
But also beestis of the feeld, as a corn floor thirstynge reyn, bihelden to thee; for the wellis of watris ben dried vp, and fier deuouride the faire thingis of desert.

< Yoweli 1 >