< Yobu 30 >

1 “Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
A sada smiju mi se mlaði od mene, kojima otaca ne bih bio htio metnuti sa psima stada svojega.
2 Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
A na što bi mi i bila sila ruku njihovijeh? u njima bješe propala starost.
3 Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
Od siromaštva i gladi samoæovahu bježeæi na suha, mraèna, pusta i opustošena mjesta;
4 Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
Koji brahu lobodu po èestama, i smrekovo korijenje bješe im hrana.
5 Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
Izmeðu ljudi bijahu izgonjeni i vikaše se za njima kao za lupežem.
6 Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
Življahu po strašnijem uvalama, po jamama u zemlji i u kamenu.
7 Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
Po grmovima rikahu, pod trnjem se skupljahu.
8 Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
Bijahu ljudi nikakvi i bez imena, manje vrijedni nego zemlja.
9 “Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
I njima sam sada pjesma, i postah im prièa.
10 Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
Gade se na me, idu daleko od mene i ne ustežu se pljuvati mi u lice.
11 Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
Jer je Bog odapeo moju tetivu i muke mi zadao te zbaciše uzdu preda mnom.
12 Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
S desne strane ustaju momci, potkidaju mi noge, i nasipaju put k meni da me upropaste.
13 Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
Raskopaše moju stazu, umnožiše mi muke, ne treba niko da im pomaže.
14 Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
Kao širokim prolomom naviru, i navaljuju preko razvalina.
15 Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
Strahote navališe na me, i kao vjetar tjeraju dušu moju, i kao oblak proðe sreæa moja.
16 “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
I sada se duša moja ražljeva u meni, stigoše me dani muèni.
17 Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
Noæu probada mi kosti u meni, i žile moje ne odmaraju se.
18 Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
Od teške sile promijenilo se odijelo moje, i kao ogrlica u košulje moje steže me.
19 Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
Bacio me je u blato, te sam kao prah i pepeo.
20 “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
Vièem k tebi, a ti me ne slušaš; stojim pred tobom, a ti ne gledaš na me.
21 Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
Pretvorio si mi se u ljuta neprijatelja; silom ruke svoje suprotiš mi se.
22 Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
Podižeš me u vjetar, posaðuješ me na nj, i rastapaš u meni sve dobro.
23 Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
Jer znam da æeš me odvesti na smrt i u dom odreðeni svjema živima.
24 “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
Ali neæe pružiti ruke svoje u grob; kad ih stane potirati, oni neæe vikati.
25 Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
Nijesam li plakao radi onoga koji bijaše u zlu? nije li duša moja žalosna bivala radi ubogoga?
26 Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
Kad se dobru nadah, doðe mi zlo; i kad se nadah svjetlosti, doðe mrak.
27 Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
Utroba je moja uzavrela, i ne može da se umiri, zadesiše me dani muèni.
28 Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
Hodim crn, ne od sunca, ustajem i vièem u zboru.
29 Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
Brat postah zmajevima i drug sovama.
30 Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
Pocrnjela je koža na meni i kosti moje posahnuše od žege.
31 Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.
Gusle se moje pretvoriše u zapijevku, i svirala moja u plaè.

< Yobu 30 >