< Yobu 29 >

1 Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
Još nastavi Jov besjedu svoju i reèe:
2 “Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
O da bih bio kao preðašnjih mjeseca, kao onijeh dana kad me Bog èuvaše,
3 pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
Kad svijetljaše svijeæom svojom nad glavom mojom, i pri vidjelu njegovu hoðah po mraku,
4 Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
Kako bijah za mladosti svoje, kad tajna Božija bijaše u šatoru mom,
5 nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
Kad još bijaše svemoguæi sa mnom, i djeca moja oko mene,
6 pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
Kad se trag moj oblivaše maslom, i stijena mi toèaše ulje potocima,
7 “Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
Kad izlažah na vrata kroz grad, i na ulici namještah sebi stolicu:
8 anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
Mladiæi videæi me uklanjahu se, a starci ustajahu i stajahu,
9 atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
Knezovi prestajahu govoriti i metahu ruku na usta svoja,
10 anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
Upravitelji ustezahu glas svoj i jezik im prianjaše za grlo.
11 Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
Jer koje me uho èujaše, nazivaše me blaženijem; i koje me oko viðaše, svjedoèaše mi
12 chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
Da izbavljam siromaha koji vièe, i sirotu i koji nema nikoga da mu pomože;
13 Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
Blagoslov onoga koji propadaše dolažaše na me, i udovici srce raspijevah;
14 Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
U pravdu se oblaèih i ona mi bijaše odijelo, kao plašt i kao vijenac bijaše mi sud moj.
15 Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
Oko bijah slijepcu i noga hromu.
16 Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
Otac bijah ubogima, i razbirah za raspru za koju ne znah.
17 Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
I razbijah kutnjake nepravedniku, i iz zuba mu istrzah grabež.
18 “Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
Zato govorah: u svojem æu gnijezdu umrijeti, i biæe mi dana kao pijeska.
19 Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
Korijen moj pružaše se kraj vode, rosa bivaše po svu noæ na mojim granama.
20 Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
Slava moja pomlaðivaše se u mene, i luk moj u ruci mojoj ponavljaše se.
21 “Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
Slušahu me i èekahu, i muèahu na moj svjet.
22 Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
Poslije mojih rijeèi niko ne pogovaraše, tako ih natapaše besjeda moja.
23 Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
Jer me èekahu kao dažd, i usta svoja otvorahu kao na pozni dažd.
24 Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
Kad bih se nasmijao na njih, ne vjerovahu, i sjajnosti lica mojega ne razgonjahu.
25 Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”
Kad bih otišao k njima, sjedah u zaèelje, i bijah kao car u vojsci, kad tješi žalosne.

< Yobu 29 >