< Yobu 10 >

1 “Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
Dodijao je duši mojoj život moj; pustiæu od sebe tužnjavu svoju, govoriæu u jadu duše svoje.
2 Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
Reæi æu Bogu: nemoj me osuditi; kaži mi zašto se preš sa mnom.
3 Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
Je li ti milo da èiniš silu, da odbacuješ djelo ruku svojih i savjet bezbožnièki obasjavaš?
4 Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
Jesu li u tebe oèi tjelesne? vidiš li kao što vidi èovjek?
5 Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
Jesu li dani tvoji kao dani èovjeèji, i godine tvoje kao vijek ljudski,
6 kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
Te istražuješ moje bezakonje i za grijeh moj razbiraš?
7 ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
Ti znaš da nijesam kriv, i nema nikoga ko bi izbavio iz tvoje ruke.
8 “Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
Tvoje su me ruke stvorile i naèinile, i ti me otsvuda potireš.
9 Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
Opomeni se da si me kao od kala naèinio, i opet æeš me u prah obratiti.
10 Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
Nijesi li me kao mlijeko slio i kao sir usirio me?
11 Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
Navukao si na me kožu i meso, i kostima i žilama spleo si me.
12 Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
Životom i milošæu darivao si me; i staranje tvoje èuvalo je duh moj.
13 “Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
I sakrio si to u srcu svojem; ali znam da je u tebe.
14 Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
Ako sam zgriješio, opazio si me, i nijesi me oprostio bezakonja mojega.
15 Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
Ako sam skrivio, teško meni! ako li sam prav, ne mogu podignuti glave, pun sramote i videæi muku svoju.
16 Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
I ako se podigne, goniš me kao lav, i opet èiniš èudesa na meni.
17 Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
Ponavljaš svjedoèanstva svoja protiv mene, i umnožavaš gnjev svoj na me; vojske jedna za drugom izlaze na me.
18 “Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
Zašto si me izvadio iz utrobe? o da umrijeh! da me ni oko ne vidje!
19 Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
Bio bih kao da nigda nijesam bio; iz utrobe u grob bio bih odnesen.
20 Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
Nije li malo dana mojih? prestani dakle i okani me se da se malo oporavim,
21 ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
Prije nego otidem odakle se neæu vratiti, u zemlju tamnu i u sjen smrtni,
22 ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”
U zemlju tamnu kao mrak i u sjen smrtni, gdje nema promjene i gdje je vidjelo kao tama.

< Yobu 10 >