< Yeremiya 42 >

1 Atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi Yohanani mwana wa Kareya ndi Azariya mwana wa Hosayia, ndiponso anthu onse, ana ndi akuluakulu omwe, anapita
Potom doðoše sve vojvode i Joanan sin Karijin i Jezanija sin Osajin, i sav narod, malo i veliko,
2 kwa mneneri Yeremiya ndipo anamuwuza kuti, “Chonde imvani dandawulo lathu ndipo mutipempherere anthu otsalafe kwa Yehova Mulungu wanu. Pakuti monga tsopano mukuona, ngakhale kuti kale tinalipo ambiri, koma tsopano ochepa okha ndiye amene atsala.
I rekoše Jeremiji proroku: pusti preda se našu molbu, i pomoli se za nas Gospodu Bogu svojemu, za sav ovaj ostatak, jer nas je ostalo malo od mnogih, kao što nas oèi tvoje vide,
3 Mupemphere kuti Yehova Mulungu wanu atiwuze kumene tiyenera kupita ndi chimene tiyenera kuchita.”
Da bi nam pokazao Gospod Bog tvoj put kojim æemo iæi i šta æemo raditi.
4 Mneneri Yeremiya anawayankha kuti, “Ndamva zimene mwanenazi. Ndithu ndidzapemphera kwa Yehova Mulungu wanu monga momwe mwandipemphera. Ndidzakuwuzani chilichonse chimene Yehova anene ndipo sindidzakubisirani kanthu kalikonse.”
A Jeremija prorok reèe im: poslušaæu; evo, pomoliæu se Gospodu Bogu vašemu po vašim rijeèima, i što vam odgovori Gospod kazaæu vam, neæu vam zatajiti ni rijeèi.
5 Ndipo iwo anawuza Yeremiya kuti, “Yehova akhale mboni yoona ndi yokhulupirika yodzatitsutsa ife ngati sitichita mogwirizana ndi chilichonse chimene Yehova Mulungu adzakutumani kuti mutiwuze.
A oni rekoše Jeremiji: Gospod neka nam je svjedok istinit i vjeran da æemo èiniti sve što ti Gospod Bog tvoj zapovjedi za nas.
6 Kaya ndi zotikomera kapena zosatikomera, ife tidzamvera Yehova Mulungu wathu, amene takutumaniko. Tidzamvera Yehova Mulungu wathu kuti zinthu zidzatiyendere bwino.”
Bilo dobro ili zlo, poslušaæemo rijeè Gospoda Boga svojega ka kojemu te šaljemo, da bi nam dobro bilo kad poslušamo glas Gospoda Boga svojega.
7 Patapita masiku khumi, Yehova anayankhula ndi Yeremiya.
A poslije deset dana doðe rijeè Gospodnja Jeremiji;
8 Choncho Yeremiya anayitana Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye ndiponso anthu onse, ana ndi akulu omwe.
Te sazva Joanana sina Karijina i sve vojvode što bijahu s njim, i sav narod, malo i veliko,
9 Yehova, Mulungu wa Israeli amene munanditumako kuti ndikapereke madandawulo mʼdzina lanu akuti,
I reèe im: ovako veli Gospod Bog Izrailjev, ka kojemu me poslaste da iznesem preda nj molbu vašu:
10 “Ngati mukhala mʼdziko muno, ndiye kuti ndidzakukhazikitsani, osakuchotsani. Inde ndidzakudzalani osakuchotsani pakuti ndi kumva chisoni kwambiri chifukwa cha mavuto amene ndabweretsa pa inu.
Ako ostanete u ovoj zemlji, sazidaæu vas, i neæu vas razoriti, i nasadiæu vas i neæu vas istrijebiti; jer mi je žao sa zla koje sam vam uèinio.
11 Musayiope mfumu ya ku Babuloni, imene mukuyiopa tsopano. Musachite nayo mantha, akutero Yehova, pakuti Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani ndi kukulanditsani mʼmanja mwake.
Ne bojte se cara Vavilonskoga, kojega se bojite; ne bojte ga se, govori Gospod, jer sam ja s vama da vas saèuvam i da vas izbavim iz njegove ruke.
12 Ndidzakuchitirani chifundo, ndipo mfumuyonso idzakuchitirani chifundo ndi kukulolani kuti mukhale mʼdziko mwanumwanu.
I uèiniæu vam milost da se smiluje na vas, i vrati vas u zemlju vašu.
13 “Koma mwina simudzamvera Yehova Mulungu wanu nʼkumanena kuti, ‘Ayi ife sitidzakhala mʼdziko muno,
Ako li reèete: neæemo da ostanemo u toj zemlji, ne slušajuæi glasa Gospoda Boga svojega
14 ndipo ngati mukunena kuti, ‘Ayi, koma tidzapita ku Igupto kumene sitidzaonako nkhondo kapena kumva kulira kwa lipenga kapenanso kusowa chakudya.’
Govoreæi: ne, nego idemo u zemlju Misirsku, da ne vidimo rata i glasa trubnoga ne èujemo i ne budemo gladni hljeba, i ondje æemo se naseliti,
15 Tsono, inu otsala a ku Yuda, imvani mawu a Yehova. Iye akuti, ngati mutsimikiza zopita ku Igupto, nʼkupitadi kukakhala kumeneko,
Onda èujte rijeè Gospodnju, koji ste ostali od Jude; ovako veli Gospod nad vojskama Bog Izrailjev: ako vi okrenete lice svoje da idete u Misir i otidete da se naselite ondje,
16 ndiye nkhondo imene mukuyiopayo idzakugonjetsani ku Igupto komweko. Njala imene mukuyiopayo idzakupezani ku Igupto komweko ndipo mudzafera kumeneko.
Ondje æe vas u zemlji Misirskoj stignuti maè kojega se bojite, i glad, radi koje se brinete, goniæe vas ondje u Misiru i ondje æete pomrijeti.
17 Kunena zoona, onse amene atsimikiza zopita ku Igupto kuti akakhale kumeneko adzafa ndi nkhondo njala ndi mliri. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzapulumuke kapena kuthawa mavuto amene ndidzawagwetsera.’
I svi ljudi koji su okrenuli lice svoje da idu u Misir da se ondje nasele, izginuæe od maèa i od gladi i od pomora, i nijedan ih neæe ostati niti æe koji uteæi od zla koje æu pustiti na njih.
18 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Momwe ndinawakwiyira mwaukali anthu okhala mu Yerusalemu, koteronso ndidzakukwiyirani mukapita ku Igupto. Mudzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, choseketsa ndi chonyozeka. Malo ano simudzawaonanso.’
Jer ovako veli Gospod nad vojskama Bog Izrailjev: kao što se gnjev moj i jarost moja izli na stanovnike Jerusalimske, tako æe se izliti gnjev moj na vas, ako otidete u Misir, i biæete uklin i èudo i kletva i rug, i neæete više vidjeti ovoga mjesta.
19 “Inu otsala a ku Yuda, Yehova wakuwuzani kuti, ‘Musapite ku Igupto.’ Dziwani chinthu ichi: Ine lero ndikukuchenjezani
Gospod vam govori, ostanci Judini! ne idite u Misir. Znajte da vam ja svjedoèim danas.
20 kuti munalakwitsa kwambiri. Inu munandituma kwa Yehova Mulungu wanu nʼkumati ‘Mukatipempherere kwa Yehova Mulungu wathu, nʼkudzatiwuza chimene afuna kuti tichite, ndipo ife tidzachita.’
Jer varaste duše svoje kad me poslaste ka Gospodu Bogu svojemu rekavši: pomoli se za nas Gospodu Bogu našemu, i kako reèe Gospod Bog naš, javi nam i uèiniæemo.
21 Ine lero ndakuwuzani, koma inu simukumverabe zonse zimene Yehova Mulungu anandituma kuti ndikuwuzeni.
A kad vam javih danas, neæete da poslušate glasa Gospoda Boga svojega niti išta što mi zapovjedi za vas.
22 Tsono dziwani ichi: mudzafadi ndi nkhondo, njala ndi mliri kumalo kumene mukufuna mukakhaleko.”
Znajte dakle da æete izginuti od maèa i od gladi i od pomora na mjestu kuda ste radi otiæi da se stanite.

< Yeremiya 42 >