< Yeremiya 38 >

1 Sefatiya mwana wa Matani, Gedaliya mwana wa Pasi-Huri, Yukali mwana wa Selemiya, ndi Pasi-Huri mwana wa Malikiya anamva zimene Yeremiya ankawuza anthu onse kuti,
Wtedy Szefatiasz, syn Matana, Gedaliasz, syn Paszchura, Jukal, syn Szelemiasza, i Paszchur, syn Malkiasza, usłyszeli słowa, które Jeremiasz wypowiadał do całego ludu:
2 “Yehova akuti, ‘Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzafa ndi nkhondo njala kapena mliri. Koma aliyense amene atatuluke kukadzipereka kwa Ababuloni adzapulumutsa moyo wake; iyeyo adzakhala ndi moyo.
Tak mówi PAN: Kto zostanie w tym mieście, zginie od miecza, od głodu i od zarazy. Ale kto przejdzie do Chaldejczyków, będzie żyć; jego życie będzie dla niego jak zdobycz i pozostanie żywy.
3 Mzinda uno udzaperekedwa ndithu kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulande.’”
Tak mówi PAN: To miasto na pewno będzie wydane w ręce wojska króla Babilonu i on je zdobędzie.
4 Tsono akuluakuluwo anawuza mfumu kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa. Iye akutayitsa mtima asilikali pamodzi ndi anthu onse amene atsala mu mzinda muno, chifukwa cha zimene akuwawuza. Munthu ameneyu sakufunira zabwino anthuwa koma chiwonongeko chawo.”
Dlatego książęta powiedzieli do króla: Ten człowiek musi umrzeć, ponieważ osłabia on ręce wojowników, którzy pozostali w tym mieście, i ręce całego ludu, gdy mówi do nich takie słowa. Ten człowiek bowiem nie szuka pomyślności tego ludu, lecz jego nieszczęścia.
5 Mfumu Zedekiya anayankha kuti, “Munthuyu ali mʼmanja mwanu. Ine sindingakuletseni chimene mukufuna kumuchitira.”
Wtedy król Sedekiasz powiedział: Oto jest w waszych rękach, bo król nic nie może czynić przeciwko wam.
6 Choncho iwo anatenga Yeremiya nakamuponya mʼchitsime cha Malikiya, mwana wa mfumu, chimene chinali mʼbwalo la alonda. Iwo anamutsitsira mʼdzenjemo ndi chingwe. Munalibe madzi koma matope okhaokha, ndipo Yeremiya anamira mʼmatopewo.
Zabrali więc Jeremiasza i wrzucili go do lochu Malkiasza, syna Meleka, który [zbudowany] był na dziedzińcu więzienia; spuścili Jeremiasza na sznurach. A w tym lochu nie było żadnej wody, tylko [samo] błoto. I Jeremiasz ugrzązł w [tym] błocie.
7 Koma Ebedi-Meleki, Mkusi, mmodzi mwa anthu ofulidwa ogwira ntchito mʼnyumba ya mfumu, anamva kuti Yeremiya anamuponya mʼchitsime. Nthawi imeneyo nʼkuti mfumu ili ku chipata cha Benjamini.
A gdy Ebedmelek, Etiopczyk, eunuch w domu króla, usłyszał, że Jeremiasza wrzucono do lochu – a król siedział w Bramie Beniamina;
8 Ebedi-Meleki anatuluka ku nyumba ya mfumu kukayiwuza kuti,
Ebedmelek wyszedł z domu króla i powiedział do króla:
9 “Mbuye wanga mfumu, zimene anthu awa amuchitira mneneri Yeremiya ndi zoyipa kwambiri. Iwo amuponya mʼchitsime, ndipo adzafa ndi njala chifukwa buledi watha mu mzinda muno.”
Królu, mój panie! Ci ludzie postąpili źle we wszystkim, co uczynili wobec proroka Jeremiasza, którego wrzucili do tego lochu; umrze z głodu w tym miejscu, ponieważ już nie ma chleba w mieście.
10 Tsono mfumu inalamula Ebedi-Meleki, Mkusi, kuti, “Tenga anthu makumi atatu, ndipo mukamutulutse mʼchitsimemo mneneri Yeremiya asanafe.”
Wtedy król rozkazał Ebedmelekowi, Etiopczykowi: Weź stąd ze sobą trzydziestu mężczyzn i wyciągnij proroka Jeremiasza z lochu, zanim umrze.
11 Pamenepo Ebedi-Meleki anatenga anthuwo, napita nawo ku nyumba ya mfumu ya pansi pa chipinda chosungiramo chuma. Kumeneko anakatengako sanza ndipo anatsitsira sanzazo ndi chingwe mʼchitsime mʼmene munali Yeremiya.
Wziął więc Ebedmelek tych mężczyzn ze sobą, wszedł do domu króla pod skarbnicę i zabrał stamtąd stare, podarte łachmany i zbutwiałe szmaty, które spuścił na sznurach do Jeremiasza, do lochu.
12 Ebedi-Meleki, Mkusi, anawuza Yeremiya kuti, “Ika sanzazo mkwapa mwako kuti zingwe zingakupweteke.” Yeremiya anachitadi zimenezi,
I Ebedmelek, Etiopczyk, powiedział do Jeremiasza: Podłóż te stare, podarte łachmany i zbutwiałe szmaty pod pachy swoich rąk, pod sznury. I Jeremiasz tak uczynił.
13 ndipo anamukoka ndi zingwe ndi kumutulutsa mʼchitsimecho. Ndipo Yeremiya anakhalabe ku bwalo la alonda.
Wyciągnęli więc Jeremiasza sznurami i wydobyli go z lochu. Potem Jeremiasz siedział na dziedzińcu więzienia.
14 Tsiku lina Mfumu Zedekiya anayitana mneneri Yeremiya ndipo anabwera naye ku chipata chachitatu cha Nyumba ya Yehova. Mfumu inawuza Yeremiya kuti, “Ndikufuna kukufunsa kanthu kena, ndipo usandibisire chilichonse.”
Następnie król Sedekiasz posłał i wziął proroka Jeremiasza do siebie, do trzeciego wejścia domu PANA. I król powiedział do Jeremiasza: Zapytam cię o jedną rzecz, nie taj niczego przede mną.
15 Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Ndikakuyankhani, kodi simundipha? Ngakhaletu ine nditakulangizani, inu simudzandimvera.”
Jeremiasz odpowiedział Sedekiaszowi: Jeśli ci powiem, czy na pewno nie zabijesz mnie? Jeśli ci [coś] poradzę, nie posłuchasz mnie.
16 Koma Mfumu Zedekiya mwachinsinsi inalumbira kwa Yeremiya kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene amatipatsa moyo, sindidzakupha ngakhalenso kukupereka kwa amene akufuna kukuphawa.”
Wedy król Sedekiasz przysiągł Jeremiaszowi potajemnie: Jak żyje PAN, który stworzył nam dusze, nie zabiję cię ani nie wydam cię w ręce tych mężczyzn, którzy czyhają na twoje życie.
17 Pamenepo Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ngati mutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mudzakhala ndi moyo ndipo mzinda uno sadzawutentha, inu pamodzi ndi banja lanu mudzakhala ndi moyo.
Jeremiasz powiedział do Sedekiasza: Tak mówi PAN, Bóg zastępów, Bóg Izraela: Jeśli dobrowolnie wyjdziesz do książąt króla Babilonu, wtedy twoja dusza będzie żyć, a to miasto nie zostanie spalone ogniem; pozostaniesz żywy ty i twój dom;
18 Koma ngati simutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mzinda uno udzaperekedwa kwa Ababuloni ndipo adzawutentha; inuyo simudzapulumuka mʼdzanja mwawo.’”
Ale jeśli nie wyjdziesz do książąt króla Babilonu, na pewno to miasto będzie wydane w ręce Chaldejczyków, którzy spalą je ogniem, a ty nie ujdziesz z ich rąk.
19 Mfumu Zedekiya inati kwa Yeremiya, “Ine ndikuopa Ayuda amene anathawira kale kwa Ababuloni, pakuti mwina Ababuloniwo adzandipereka kwa Ayudawo ndipo iwowo adzandizunza.”
Król Sedekiasz powiedział do Jeremiasza: Bardzo się boję Żydów, którzy przeszli do Chaldejczyków, by czasem nie wydali mnie w ich ręce i nie szydzili ze mnie.
20 Yeremiya anayankha kuti, “Ngati mumvera Yehova ndi kuchita zimene ndakuwuzani, ndiye kuti zinthu zidzakuyenderani bwino. Inu simudzaphedwa.
Jeremiasz odpowiedział: Nie wydadzą [cię]. Posłuchaj, proszę, głosu PANA, który ci przekazuję, a dobrze ci się powiedzie i twoja dusza będzie żyć.
21 Koma mukakana kudzipereka, chimene Yehova wandiwululira ndi ichi:
Jeśli zaś będziesz wzbraniał się wyjść, takie jest słowo, które PAN mi pokazał:
22 Akazi onse amene atsala mʼnyumba ya mfumu ya Yuda adzaperekedwa kwa akuluakulu a mfumu ya ku Babuloni. Akazi amenewo adzakuwuzani kuti, “‘Abwenzi ako okhulupirika aja anakusokeretsa, ndipo anakugonjetsa. Poti tsopano miyendo yako yazama mʼmatope; abwenzi ako aja akusiya.’
Oto wszystkie kobiety, które pozostały w domu króla Judy, będą wyprowadzone do książąt króla Babilonu i tak one powiedzą: Twoi przyjaciele oszukali cię i przemogli, twoje nogi ugrzęzły w błocie, [a] oni się wycofali.
23 “Akazi pamodzi ndi ana anu adzaperekedwa kwa Ababuloni. Inuyo simudzapulumuka mʼmanja mwawo koma mfumu ya ku Babuloni idzakugwirani; mzinda uno adzawutentha.”
Wszystkie twoje żony i twoich synów wyprowadzą do Chaldejczyków, a i ty nie ujdziesz ich rękom, lecz będziesz pojmany ręką króla Babilonu, a to miasto spalą ogniem.
24 Pamenepo Zedekiya anati kwa Yeremiya, “Usawuze munthu wina aliyense zimene takambiranazi, ukatero udzaphedwa.
Wtedy Sedekiasz powiedział do Jeremiasza: Niech nikt nie wie o tej rozmowie, a ty nie umrzesz;
25 Akuluakulu akamva kuti ndinayankhula nawe ndipo akabwera kwa iwe nʼkudzakufunsa kuti, ‘Tiwuze zimene unanena kwa mfumu ndi zimene mfumu inanena kwa iwe; usatibisire, ukatero tidzakupha,’
A jeśli książęta usłyszą, że rozmawiałem z tobą, przyjdą do ciebie i powiedzą: Powiedz nam, proszę, co mówiłeś do króla; nie ukrywaj przed nami, a nie zabijemy cię; a co ci mówił król?
26 udzawawuze kuti, ‘Ine ndimapempha mfumu kuti isandibwezerenso ku nyumba ya Yonatani kuti ndikafere kumeneko.’”
Wtedy im powiesz: Przedłożyłem królowi moją prośbę, aby mnie nie odsyłał do domu Jonatana, abym tam nie umarł.
27 Akuluakulu onse anabweradi kwa Yeremiya kudzamufunsa. Iye anawayankha monga momwe mfumu inamulamula. Choncho palibe amene ananenanso kanthu, pakuti palibe amene anamva zomwe anakambirana ndi mfumu.
I wszyscy książęta przyszli do Jeremiasza, i pytali go, a on odpowiedział im zgodnie z tym wszystkim, co król mu rozkazał. I odstąpili w milczeniu od niego, gdyż sprawa nie wyszła na jaw.
28 Ndipo Yeremiya anakhalabe mʼbwalo la alonda mpaka tsiku limene mzinda wa Yerusalemu unalandidwa.
A Jeremiasz przebywał na dziedzińcu więzienia aż do tego dnia, kiedy zdobyto Jerozolimę. Był tam, gdy Jerozolima została zdobyta.

< Yeremiya 38 >