< Yeremiya 37 >

1 Nebukadinezara mfumu ya Babuloni, inakhazika pa mpando waufumu Zedekiya mwana wa Yosiya kukhala mfumu ya Yuda. Iye analowa mʼmalo mwa Yehoyakini mwana wa Yehoyakimu.
Potem królował król Sedekiasz, syn Jozjasza, w miejsce Choniasza, syna Joakima, którego Nabuchodonozor, król Babilonu, ustanowił królem w ziemi Judy.
2 Koma Zedekiya kapena atumiki ake ngakhalenso anthu a mʼdzikomo sanasamalire mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa mneneri Yeremiya.
Lecz ani on, ani jego słudzy, ani lud tej ziemi nie słuchali słów PANA, które wypowiedział przez proroka Jeremiasza.
3 Tsono Zedekiya anatuma Yehukali mwana wa Selemiya ndi wansembe Zefaniya mwana wa Maseya kwa mneneri Yeremiya ndi uthenga uwu: “Chonde tipempherereni kwa Yehova Mulungu wathu.”
Król Sedekiasz jednak posłał Jehuchala, syna Szelemiasza, i Sofoniasza, syna Maasejasza, kapłana, do proroka Jeremiasza, aby powiedzieli: Módl się za nas do PANA, naszego Boga.
4 Nthawi imeneyinso nʼkuti Yeremiya ali ndi ufulu woyenda pakati pa anthu chifukwa anali asanaponyedwe mʼndende.
Jeremiasz zaś chodził swobodnie wśród ludu, gdyż jeszcze nie wtrącono go do więzienia.
5 Nthawi imeneyinso nʼkuti gulu lankhondo la Farao litatuluka mʼdziko la Igupto. Ndipo Ababuloni amene anali atazinga Yerusalemu atamva zimenezi, anachoka ku Yerusalemuko.
Tymczasem wojsko faraona wyruszyło z Egiptu. A gdy usłyszeli tę wieść Chaldejczycy oblegający Jerozolimę, odstąpili od Jerozolimy.
6 Tsono Yehova anawuza mneneri Yeremiya kuti,
I słowo PANA doszło do proroka Jeremiasza mówiące:
7 “Uyiwuze mfumu ya Yuda imene inakutuma kuti udzapemphe nzeru kwa ine kuti Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, gulu lankhondo la Farao limene linatuluka kuti lidzakuthandize lidzabwerera kwawo ku Igupto.
To mówi PAN, Bóg Izraela: Tak powiedzcie królowi Judy, który posłał was do mnie, abyście się mnie radzili: Oto wojsko faraona, które wyruszyło wam na pomoc, wróci do swojej ziemi, do Egiptu.
8 Ndipo Ababuloni adzabwerera kudzathira nkhondo mzinda uno. Iwo adzawugonjetsa ndi kuwutentha.
I Chaldejczycy powrócą, i będą walczyli przeciwko temu miastu, zdobędą je i spalą ogniem.
9 “Yehova akuti: Musadzinyenge, nʼkumaganiza kuti, ‘Ndithu Ababuloni adzatisiya.’ Ndithudi sadzakusiyani!
Tak mówi PAN: Nie zwódźcie samych siebie, mówiąc: Z pewnością Chaldejczycy odstąpią od nas. Bo nie odstąpią.
10 Ngakhale mutagonjetsa gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene likukuthirani nkhondo ndipo mʼmatenti mwawo ndikutsala anthu ovulala okhaokha, amenewo adzabwera ndi kudzatentha mzinda uno.”
Choćbyście nawet pobili całe wojsko Chaldejczyków, którzy walczą z wami, i zostaliby z nich tylko ranni, to [ci] powstaliby ze swoich namiotów i ogniem spaliliby to miasto.
11 Gulu lankhondo la Ababuloni litaleka kuthira nkhondo mzinda wa Yerusalemu chifukwa choopa gulu lankhondo la Farao,
A gdy wojsko Chaldejczyków odstąpiło od Jerozolimy przed wojskiem faraona;
12 Yeremiya ananyamuka kuchoka ku Yerusalemu ndi kumapita ku dziko la Benjamini kuti akalandire gawo lake la minda ya makolo ake.
Jeremiasz wychodził z Jerozolimy, aby udać się do ziemi Beniamina, by tym sposobem ujść stamtąd pośród ludu.
13 Koma atafika pa Chipata cha Benjamini, mkulu wa alonda amene dzina lake linali Iriya mwana wa Selemiya, mwana wa Hananiya, anagwira mneneri Yeremiyayo ndipo anati, “Iwe ukuthawira kwa Ababuloni!”
A gdy był [już] w Bramie Beniamina, znajdował się tam dowódca straży, imieniem Jirijasz, syn Szelemiasza, syna Chananiasza; ten pojmał proroka Jeremiasza, mówiąc: Przechodzisz do Chaldejczyków!
14 Yeremiya anati, “Zimenezo si zoona! Ine sindikuthawira kwa Ababuloni.” Koma Iriya sanamumvere. Mʼmalo mwake anagwira Yeremiya nʼkupita naye kwa akuluakulu.
Jeremiasz odpowiedział: Nieprawda, nie przechodzę do Chaldejczyków. Ale [tamten] nie chciał go słuchać. Jirijasz pojmał Jeremiasza i przyprowadził go do książąt.
15 Akuluakuluwo anamupsera mtima Yeremiya ndipo anamukwapula ndi kumuyika mʼnyumba ya mlembi Yonatani, imene anayisandutsa ndende.
Książęta rozgniewali się na Jeremiasza, bili go i wsadzili do więzienia w domu Jonatana, pisarza, bo ten zamieniono na więzienie.
16 Yeremiya anayikidwa mʼndende ya pansi pa nthaka, kumene anakhalako nthawi yayitali.
A gdy Jeremiasz wszedł do tego lochu i do celi, i siedział tam Jeremiasz przez wiele dni;
17 Kenaka Mfumu Zedekiya inatuma anthu kuti akayitane Yeremiya ndipo anabwera naye ku nyumba ya mfumu. Atafika mfumu inamufunsa mwamseri kuti, “Kodi pali mawu ena amene Yehova wakuwuza?” Yeremiya anayankha kuti, “Inde. Inu mfumu mudzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni.”
Wtedy król Sedekiasz posłał, aby go przyprowadzono. I król wypytywał go potajemnie w swoim domu: Czy jest [jakieś] słowo od PANA? Jeremiasz odpowiedział: Jest. I dodał: Będziesz wydany w ręce króla Babilonu.
18 Pamenepo Yeremiya anafunsa Mfumu Zedekiya kuti, “Kodi ndakulakwirani chiyani inuyo kapena akuluakulu anu kapenanso anthu awa, kuti mundiyike mʼndende?
Nadto Jeremiasz powiedział do króla Sedekiasza: Czym zgrzeszyłem [przeciwko] tobie, twoim sługom lub twemu ludowi, że wsadziliście mnie do tego więzienia?
19 Kodi ali kuti aneneri anu amene anakuloserani kuti, ‘Mfumu ya ku Babuloni sidzakuthirani nkhondo pamodzi ndi dziko lino’?
Gdzie są wasi prorocy, którzy wam prorokowali, mówiąc: Król Babilonu nie nadciągnie przeciwko wam ani przeciwko tej ziemi.
20 Koma tsopano, mbuye wanga mfumu, chonde tamverani. Loleni ndinene pempho langa pamaso panu: Musandibwezere ku nyumba ya mlembi Yonatani, kuopa kuti ndingakafere kumeneko.”
Teraz więc słuchaj, proszę, królu, mój panie. Niech moja prośba dotrze do ciebie: Nie odsyłaj mnie do domu Jonatana, pisarza, abym tam nie umarł.
21 Tsono Mfumu Zedekiya analamula kuti Yeremiya asungidwe mʼbwalo la alonda. Ankamupatsa buledi tsiku ndi tsiku amene ankamugula kwa ophika buledi. Anapitiriza kutero mpaka buledi yense anatha mu mzindamo. Choncho Yeremiya anapitirira kukhala mʼbwalo la alonda.
Król Sedekiasz rozkazał więc oddać Jeremiasza pod straż na dziedzińcu więzienia i aby dawano mu bochenek chleba dziennie z ulicy Piekarzy, póki nie został wyczerpany cały chleb w mieście. A Jeremiasz pozostał na dziedzińcu więzienia.

< Yeremiya 37 >