< Yesaya 66 >

1 Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
Ovako veli Gospod: nebo je prijesto moj i zemlja podnožje nogama mojim: gdje je dom koji biste mi sazidali, i gdje je mjesto za moje poèivanje?
2 Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
Jer je sve to ruka moja stvorila, to je postalo sve, veli Gospod; ali na koga æu pogledati? na nevoljnoga i na onoga ko je skrušena duha i ko drkæe od moje rijeèi.
3 Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
Ko kolje vola, to je kao da ubije èovjeka; ko kolje ovcu, to je kao da zakolje psa; ko prinosi dar, to je kao da prinese krv svinjeæu; ko kadi kadom, to je kao da blagoslovi idola. To oni izabraše na putovima svojim, i duši se njihovoj mile gadovi njihovi.
4 Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
Izabraæu i ja prema nevaljalstvu njihovu, i pustiæu na njih èega se boje; jer zvah a niko se ne odazva, govorih a oni ne slušaše, nego èiniše što je zlo preda mnom i izabraše što meni nije po volji.
5 Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
Slušajte rijeè Gospodnju, koji drkæete od njegove rijeèi: braæa vaša, koja mrze na vas i izgone vas imena mojega radi, govore: neka se pokaže slava Gospodnja. I pokazaæe se na vašu radost, a oni æe se posramiti.
6 Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
Vika ide iz grada, glas iz crkve, glas Gospodnji koji plaæa neprijateljima svojim.
7 “Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
Ona se porodi prije nego osjeti bolove, prije nego joj doðoše muke, rodi djetiæa.
8 Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
Ko je igda èuo to? ko je vidio tako što? Može li zemlja roditi u jedan dan? može li se narod roditi ujedanput? a Sion rodi sinove svoje èim osjeti bolove.
9 Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
Eda li ja, koji otvoram matericu, ne mogu roditi? veli Gospod; eda li æu ja, koji dajem da se raða, biti bez poroda? veli Bog tvoj.
10 “Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
Radujte se s Jerusalimom i veselite se u njemu svi koji ga ljubite; radujte se s njim svi koji ga žaliste.
11 Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
Jer æete sati sise od utjehe njegove, i nasitiæete se, saæete i naslaðivaæete se u svjetlosti slave njegove.
12 Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
Jer ovako veli Gospod: gle, ja æu kao rijeku dovesti k njemu mir i slavu naroda kao potok bujan, pa æete sati; biæete nošeni na rukama i milovani na koljenima.
13 Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
Kao kad koga mati njegova tješi tako æu ja vas tješiti, i utješiæete se u Jerusalimu.
14 Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
Vidjeæete i obradovaæe se srce vaše i kosti æe se vaše pomladiti kao trava, i znaæe se ruka Gospodnja na slugama njegovijem i gnjev na neprijateljima njegovijem.
15 Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
Jer, gle, Gospod æe doæi s ognjem, i kola æe mu biti kao vihor, da izlije gnjev svoj u jarosti i prijetnju u plamenu ognjenom.
16 Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
Jer æe Gospod suditi ognjem i maèem svojim svakom tijelu, i mnogo æe biti pobijenijeh od Gospoda.
17 Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
Koji se osveštavaju i koji se oèišæaju u vrtovima jedan za drugim javno, koji jedu meso svinjeæe i stvari gadne i miše, svi æe izginuti, veli Gospod.
18 “Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
A ja znam djela njihova i misli njihove, i doæi æe vrijeme, te æu sabrati sve narode i jezike, i doæi æe i vidjeæe slavu moju.
19 “Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
I postaviæu znak na njih, i poslaæu izmeðu njih koji se spasu k narodima u Tarsis, u Ful i u Lud, koji natežu luk, u Tuval i u Javan i na daljna ostrva, koja ne èuše glasa o meni niti vidješe slave moje, i javljaæe slavu moju po narodima.
20 Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
I svu æe braæu vašu iz svijeh naroda dovesti Gospodu na dar na konjima i na kolima i na nosilima i na mazgama i na kamilama ka svetoj gori mojoj u Jerusalim, veli Gospod, kao što prinose sinovi Izrailjevi dar u èistu sudu u dom Gospodnji.
21 Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
I izmeðu njih æu uzeti sveštenike i Levite, veli Gospod.
22 “Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
Jer kao što æe nova nebesa i nova zemlja, što æu ja naèiniti, stajati preda mnom, veli Gospod, tako æe stajati sjeme vaše i ime vaše.
23 “Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
I od mladine do mladine, i od subote do subote dolaziæe svako tijelo da se pokloni preda mnom, veli Gospod.
24 “Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”
I izlaziæe i gledaæe mrtva tjelesa onijeh ljudi koji se odmetnuše od mene; jer crv njihov neæe umrijeti i oganj njihov neæe se ugasiti, i biæe gad svakom tijelu.

< Yesaya 66 >