< Yesaya 65 >

1 “Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu; ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze. Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine, ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’
Potražiše me koji ne pitahu za me; naðoše me koji me ne tražahu; rekoh narodu koji se ne zove mojim imenom: evo me, evo me.
2 Tsiku lonse ndatambasulira manja anga anthu owukira aja, amene amachita zoyipa, natsatira zokhumba zawo.
Vas dan pružah ruke svoje narodu nepokornu, koji ide za svojim mislima putem koji nije dobar,
3 Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa mopanda manyazi. Iwo amapereka nsembe mʼminda ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.
Narodu, koji me jednako gnjevi u oèi, koji prinosi žrtve u vrtovima i kadi na opekama;
4 Amakatandala ku manda ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika. Amadya nyama ya nkhumba, ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.
Koji sjede kod grobova i noæuju u peæinama, jedu meso svinjeæe i juha im je neèista u sudovima;
5 Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire, chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’ Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga, ngati moto umene umayaka tsiku lonse.
Koji govore: odlazi, ne dohvataj me se, jer sam svetiji od tebe. Ti su dim u nozdrvama mojim, oganj koji gori vas dan.
6 “Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo; sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu chifukwa cha machimo awo
Eto, napisano je preda mnom: neæu muèati, nego æu platiti, platiæu im u njedra.
7 ndi a makolo awo,” akutero Yehova. “Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo, Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata zimene anachita kale.”
Za bezakonja vaša i za bezakonja otaca vaših, veli Gospod, koji kadiše na gorama, i na humovima ružiše me, izmjeriæu im u njedra platu za djela koja èiniše od poèetka.
8 Yehova akuti, “Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo, popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’ Inenso chifukwa cha mtumiki wanga; sindidzawononga onse.
Ovako veli Gospod: kao kad ko naðe vina u grozdu, pa reèe: ne kvari ga, jer je blagoslov u njemu, tako æu uèiniti radi sluga svojih, neæu ih potrti svijeh,
9 Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo, ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo. Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi, ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.
Jer æu izvesti sjeme iz Jakova i iz Jude našljednika gorama svojim, i naslijediæe ih izbranici moji, i sluge moje naseliæe se ondje.
10 Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa, ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe kwa anthu anga ondifunafuna Ine.
A Saron æe biti tor za ovce i dolina Ahorska poèivalište za goveda narodu mojemu koji me traži.
11 “Koma inu amene mumasiya Yehova ndi kuyiwala phiri langa lopatulika, amene munamukonzera Gadi chakudya ndi kuthirira Meni chakumwa,
A vi, koji ostavljate Gospoda, koji zaboravljate svetu goru moju, koji postavljate sto Gadu i ljevate naljev Meniju,
12 ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe, ndipo nonse mudzaphedwa; chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani, ndinayankhula koma simunamvere. Munachita zoyipa pamaso panga ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”
Vas æu izbrojiti pod maè, i svi æete pripasti na klanje, jer zvah a vi se ne odzivaste, govorih a vi ne slušaste, nego èiniste što je zlo preda mnom i izabraste što meni nije po volji.
13 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, “Atumiki anga adzadya, koma inu mudzakhala ndi njala; atumiki anga adzamwa, koma inu mudzakhala ndi ludzu; atumiki anga adzakondwa, koma inu mudzakhala ndi manyazi.
Zato ovako veli Gospod Gospod: gle, sluge æe moje jesti, a vi æete gladovati; gle, sluge æe moje piti, a vi æete biti žedni; gle, sluge æe se moje veseliti, a vi æete se stidjeti.
14 Atumiki anga adzayimba mosangalala, koma inu mudzalira kwambiri chifukwa chovutika mu mtima ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.
Gle, sluge æe moje pjevati od radosti u srcu, a vi æete vikati od žalosti u srcu i ridaæete od tuge u duhu.
15 Anthu anga osankhidwa adzatchula dzina lanu potemberera. Ambuye Yehova adzakuphani, koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.
I ostaviæete ime svoje izbranima mojim za uklin; i Gospod æe te Bog ubiti, a sluge æe svoje nazvati drugim imenom.
16 Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo adzachita zimenezo kwa Mulungu woona; ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo adzalumbira mwa Mulungu woona. Pakuti mavuto akale adzayiwalika ndipo adzachotsedwa pamaso panga.
Ko se uzblagosilja na zemlji, blagosiljaæe se Bogom istinijem; a ko se uskune na zemlji, kleæe se Bogom istinijem; jer æe se prve nevolje zaboraviti i sakrivene æe biti od oèiju mojih.
17 “Taonani, ndikulenga mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano. Zinthu zakale sizidzakumbukika, zidzayiwalika kotheratu.
Jer, gle, ja æu stvoriti nova nebesa i novu zemlju, i što je prije bilo neæe se pominjati niti æe na um dolaziti.
18 Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya chifukwa cha zimene ndikulenga, pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.
Nego se radujte i veselite se dovijeka radi onoga što æu ja stvoriti; jer gle, ja æu stvoriti Jerusalim da bude veselje i narod njegov da bude radost.
19 Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga. Kumeneko sikudzamvekanso kulira ndi mfuwu wodandaula.
I ja æu se veseliti radi Jerusalima, i radovaæu se radi naroda svojega, i neæe se više èuti u njemu plaè ni jauk.
20 “Ana sadzafa ali akhanda ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse. Wamngʼono mwa iwo adzafa ali ndi zaka 100. Amene adzalephere kufika zaka 100 adzatengedwa kukhala wotembereredwa.
Neæe više biti ondje maloga djeteta ni starca koji ne bi navršio dana svojih; jer æe dijete umirati od sto godina, a grješnik od sto godina biæe proklet.
21 Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo, adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.
I oni æe graditi kuæe i sjedjeæe u njima; i sadiæe vinograde i ješæe rod njihov.
22 Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo, kapena kudzala ndi ena nʼkudya. Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo wautali ngati mitengo. Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito ya manja awo nthawi yayitali.
Neæe oni graditi a drugi se naseliti, neæe saditi a drugi jesti, jer æe dani narodu mojemu biti kao dani drvetu, i izbranicima æe mojim ovetšati djela ruku njihovijeh.
23 Sadzagwira ntchito pachabe kapena kubereka ana kuti aone tsoka; chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova, iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.
Neæe raditi uzalud, niti æe raðati za strah, jer æe biti sjeme blagoslovenijeh od Gospoda, i natražje æe njihovo biti s njima.
24 Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe. Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.
I prije nego povièu, ja æu se odazvati; još æe govoriti, a ja æu uslišiti.
25 Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi. Mkango udzadya udzu monga ngʼombe, koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka. Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala chinthu chopweteka kapena chowononga,” akutero Yehova.
Vuk i jagnje zajedno æe pasti, i lav æe jesti slamu kao vo; a zmiji æe biti hrana prah; neæe uditi ni potirati na svoj svetoj gori mojoj, veli Gospod.

< Yesaya 65 >