< Yesaya 57 >

1 Anthu olungama amafa, ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake; anthu odzipereka amatengedwa, ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake. Anthu olungama amatengedwa kuti tsoka lisawagwere.
Pravednik mre, i niko ne mari; i pobožni se ljudi uzimaju, a niko se ne sjeæa da se pred zlo uzima pravednik;
2 Iwo amene amakhala moyo wolungama amafa mwamtendere; amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.
Dolazi u mir i poèiva na postelji svojoj ko god hodi pravijem putem.
3 “Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa, inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!
A vi sinovi vraèarini, rode kurvarski, koji se kurvate, pristupite ovamo.
4 Kodi inu mukuseka yani? Kodi mukumunena ndani ndi kupotoza pakamwa panu? Kodi inu si ana owukira, zidzukulu za anthu abodza?
Kim se rugate? na koga razvaljujete usta i plazite jezik? nijeste li sinovi prestupnièki, sjeme lažno?
5 Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu, ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri. Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.
Koji se upaljujete za lugovima, pod svakim zelenijem drvetom, koljete sinove svoje u potocima, pod vrletima kamenijem.
6 Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu. Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo, ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya. Kodi zimenezi zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?
Dio ti je meðu glatkim kamenjem potoènim; to je, to je tvoj dio; njemu ljevaš naljev svoj, prinosiš dar; tijem li æu se umiriti?
7 Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali. Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.
Na gori visokoj i uzvišenoj meæeš postelju svoju; i onamo izlaziš da prineseš žrtvu.
8 Mʼnyumba mwanu mwayika mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu. Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu. Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu, ndiye mwazilipira kuti mugone nazo. Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.
I iza vrata i iza dovrataka meæeš spomen svoj; otstupivši od mene otkrivaš se, i izašavši gore širiš odar svoj, ugovaraš s njima, mila ti je postelja njihova, gdje ugledaš mjesto.
9 Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta ndi zonunkhira zochuluka. Munachita kutumiza akazembe anu kutali; inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko! (Sheol h7585)
Ideš k caru s uljem, s mnogim mirisima svojim; šalješ poslanike svoje daleko i ponizuješ se do groba. (Sheol h7585)
10 Inu mumatopa ndi maulendo anu, koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’ Munapezako kumeneko zokhumba zanu nʼchifukwa chake simunalefuke.
Od daljnoga puta svoga umorna ne kažeš: zaludu. Nalaziš život ruci svojoj, zato ne sustaješ.
11 “Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa, kotero kuti mwakhala mukundinamiza, ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe, kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine? Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti ndakhala chete nthawi yayitali?
I od koga si se uplašila i koga si se pobojala, te si slagala i nijesi se mene opominjala niti si marila? što ja muèah odavna, zato li me se ne bojiš?
12 Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama, ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.
Ja æu objaviti tvoju pravdu i tvoja djela; ali ti neæe pomoæi.
13 Pamene mufuwula kupempha thandizo, mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni! Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo, mpweya chabe udzawulutsa mafanowo. Koma munthu amene amadalira ine adzalandira dziko lokhalamo. Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”
Kad staneš vikati, neka te izbave oni koje si sabrala; ali æe ih sve vjetar odnijeti, i uzeæe ih taština. Ali ko se u me uzda, naslijediæe zemlju i dobiæe svetu goru moju.
14 Ndipo panamveka mawu akuti, “Undani, undani, konzani msewu! Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”
I reæi æe se: poravnite, poravnite, pripravite put, uklonite smetnje s puta naroda mojega.
15 Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse, amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo, akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika, koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.
Jer ovako govori visoki i uzvišeni, koji živi u vjeènosti, kojemu je ime sveti: na visini i u svetinji stanujem i s onijem ko je skrušena srca i smjerna duha oživljujuæi duh smjernijeh i oživljujuæi srce skrušenijeh.
16 Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya kapena kuwapsera mtima nthawi zonse, popeza kuti ndinalenga anthu anga ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.
Jer se neæu jednako preti niti æu se dovijeka gnjeviti, jer bi išèeznuo preda mnom duh i duše koje sam stvorio.
17 Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera; ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya, koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.
Za bezakonje lakomosti njegove razgnjevih se, i udarih ga, sakrih se i razgnjevih se, jer odmetnuvši se otide putem srca svojega.
18 Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa; kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,
Vidim putove njegove, ali æu ga iscijeliti, vodiæu ga i daæu opet utjehu njemu i njegovijem koji tuže.
19 anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo. Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,” “Ndipo ndidzawachiritsa.” Akutero Yehova.
Ja stvaram plod usnama: mir, mir onomu ko je daleko i ko je blizu, veli Gospod, i iscijeliæu ga.
20 Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka, yosatha kukhala bata, mafunde ake amaponya matope ndi ndere.
A bezbožnici su kao more uskolebano, koje se ne može umiriti i voda njegova izmeæe neèistotu i blato.
21 “Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.
Nema mira bezbožnicima, veli Bog moj.

< Yesaya 57 >