< Yesaya 55 >

1 “Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu, bwerani madzi alipo; ndipo inu amene mulibe ndalama bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye! Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
Alle that thirsten, come ye to watris, and ye han not siluer, haaste, bie ye, and ete ye; come ye, bie ye, with out siluer and with outen ony chaungyng, wyn and mylk.
2 Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya, ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa? Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino; ndipo mudzisangalatse.
Whi peisen ye siluer, and not in looues, and youre trauel, not in fulnesse? Ye herynge here me, and ete ye good, and youre soule schal delite in fatnesse.
3 Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine; mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo. Ndidzachita nanu pangano losatha, chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
Bowe ye youre eere, and `come ye to me; here ye, and youre soule schal lyue; and Y schal smyte with you a couenaunt euerlastynge, the feithful mercies of Dauid.
4 Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu, kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
Lo! Y yaf hym a witnesse to puplis, a duyk and a comaundour to folkis.
5 Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa, ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu. Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu, Woyerayo wa Israeli, wakuvekani ulemerero.”
Lo! thou schalt clepe folkis, whiche thou knewist not; and folkis, that knewen not thee, schulen renne to thee; for thi Lord God, and the hooli of Israel, for he glorifiede thee.
6 Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka. Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.
Seke ye the Lord, while he mai be foundun; clepe ye hym to help, while he is niy.
7 Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa, ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa. Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo, ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.
An vnfeithful man forsake his weie, and a wickid man forsake hise thouytis; and turne he ayen to the Lord, and he schal haue merci on hym, and to oure God, for he is myche to foryyue.
8 “Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu, ngakhale njira zanu si njira zanga,” akutero Yehova.
For why my thouytis ben not youre thouytis, and my weies ben not youre weies, seith the Lord.
9 “Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.
For as heuenys ben reisid fro erthe, so my weies ben reisid fro youre weies, and my thouytis fro youre thouytis.
10 Monga mvula ndi chisanu chowundana zimatsika kuchokera kumwamba, ndipo sizibwerera komweko koma zimathirira dziko lapansi. Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.
And as reyn and snow cometh doun fro heuene, and turneth no more ayen thidur, but it fillith the erthe, and bischedith it, and makith it to buriowne, and yyueth seed to hym that sowith, and breed to hym that etith,
11 Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga. Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake, koma adzachita zonse zimene ndifuna, ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.
so schal be my word, that schal go out of my mouth. It schal not turne ayen voide to me, but it schal do what euer thingis Y wolde, and it schal haue prosperite in these thingis to whiche Y sente it.
12 Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe ndipo adzakutsogolerani mwamtendere; mapiri ndi zitunda zidzakuyimbirani nyimbo, ndipo mitengo yonse yamʼthengo idzakuwombereni mʼmanja.
For ye schulen go out in gladnesse, and ye schulen be led forth in pees; mounteyns and litil hillis schulen synge heriynge bifore you, and alle the trees of the cuntrei schulen make ioie with hond.
13 Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini, ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu. Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova, ngati chizindikiro chamuyaya, chimene sichidzafafanizika konse.”
A fir tre schal grow for a firse, and a mirte tre schal wexe for a nettil; and the Lord schal be nemyd in to a signe euerlastynge, that schal not be doon awei.

< Yesaya 55 >