< Yesaya 47 >

1 “Tsika, ndi kukhala pa fumbi, iwe namwali, Babuloni; khala pansi wopanda mpando waufumu, iwe namwali, Kaldeya pakuti sadzakutchulanso wanthete kapena woyenera kumugwira mosamala.
Siði i sjedi u prah, djevojko, kæeri Vavilonska; sjedi na zemlju, nema prijestola, kæeri Haldejska; jer se neæeš više zvati nježna i ljupka.
2 Tenga mphero ndipo upere ufa; chotsa nsalu yako yophimba nkhope kwinya chovala chako mpaka ntchafu ndipo woloka mitsinje.
Uzmi žrvnje, i melji brašno, otkrij kosu svoju, izuj se, zagali golijeni, idi preko rijeka.
3 Maliseche ako adzakhala poyera ndipo udzachita manyazi. Ndidzabwezera chilango ndipo palibe amene adzandiletse.”
Otkriæe se golotinja tvoja, i vidjeæe se sramota tvoja; osvetiæu se, i niko mi neæe smetati.
4 Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wathu, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Ime je izbavitelju našemu Gospod nad vojskama, svetac Izrailjev.
5 “Khala chete, ndipo lowa mu mdima, iwe namwali, Kaldeya; chifukwa sadzakutchulanso mfumukazi ya maufumu.
Sjedi muèeæi, i uði u tamu, kæeri Haldejska; jer se neæeš više zvati gospoða carstvima.
6 Ndinawakwiyira anthu anga, osawasamalanso. Ndinawapereka manja mwako, ndipo iwe sunawachitire chifundo. Iwe unachitira nkhanza ngakhale nkhalamba.
Razgnjevih se na narod svoj, oskvrnih našljedstvo svoje i predadoh ga tebi u ruke; a ti im ne pokaza milosti; na starce si metala preteški jaram svoj;
7 Iwe unati, ‘Ine ndidzakhalapo nthawi zonse ngati mfumukazi.’ Koma sunaganizire zinthu izi kapena kusinkhasinkha za mmene ziti zidzathere.
I govorila si: dovijeka æu biti gospoða; ali nikad nijesi to uzimala na um, niti si pomišljala šta æe biti na pošljedak.
8 “Ndipo tsopano, tamvera, iwe wongokonda zokondweretsawe, amene ukukhala mosatekesekawe, umaganiza mu mtima mwako kuti, ‘Ine ndi Ine, ndipo kupatula ine palibenso wina. Sindidzakhala konse mkazi wamasiye, ndipo ana anga sadzamwalira.’
Sada dakle èuj ovo, koja živiš u slastima i bez brige sjediš i govoriš u srcu svom: ja sam, i nema druge osim mene, neæu biti udovica niti æu osirotjeti.
9 Koma mʼkamphindi, ndiponso tsiku limodzi, zinthu ziwiri izi zidzakuchitikira: ana ako kukufera komanso kukhala mkazi wamasiye. Zimenezi zidzakuchitikira kwathunthu ngakhale ali ndi amatsenga ambiri ndi mawula amphamvu.
To æe ti oboje doæi ujedanput, u isti dan, da osirotiš i obudoviš, doæi æe ti potpuno, radi mnoštva èini tvojih i radi velike sile èaranja tvoga.
10 Iwe unkadalira kuyipa kwako ndipo unati, ‘Palibe amene akundiona.’ Kuchenjera ndi nzeru zako zidzakusokoneza, choncho ukuganiza mu mtima mwako kuti, ‘Ine ndine basi, ndipo kupatula ine palibenso wina.’
Jer si se pouzdala u zloæu svoju govoreæi: niko me ne vidi. Mudrost tvoja i znanje tvoje prevariše te, te si govorila u srcu svom: ja sam, i osim mene nema druge.
11 Ngozi yayikulu idzakugwera ndipo sudzadziwa momwe ungayipewere ndi matsenga ako. Mavuto adzakugwera ndipo sudzatha kuwachotsa; chipasupasu chimene iwe sukuchidziwa chidzakugwera mwadzidzidzi.
Zato æe doæi na te zlo, a neæeš znati odakle izlazi, i popašæe te nevolja, da je neæeš moæi odbiti, i doæi æe na te ujedanput pogibao, za koju neæeš znati.
12 “Pitiriza tsono kukhala ndi matsenga ako, pamodzi ndi nyanga zako zochulukazo, wakhala ukuzigwiritsa ntchito kuyambira ubwana wako. Mwina udzatha kupambana kapena kuopsezera nazo adani ako.
Stani sada s vraèanjem svojim i s mnoštvom èini svojih, oko kojih si se trudila od mladosti svoje, ne bi li se pomogla, ne bi li se okrijepila.
13 Malangizo onse amene unalandira angokutopetsa basi! Abwere patsogolopa anthu amene amatanthauzira za kumwamba kuti adzakupulumutseni. Abwere amene amayangʼana nyenyezi, ndi kumalosera mwezi ndi mwezi zimene ziti zidzakuchitikire.
Umorila si se od mnoštva namjera svojih; neka stanu sada zvjezdari, koji gledaju zvijezde, koji prorièu svakoga mjeseca, i neka te saèuvaju od onoga što æe doæi na te.
14 Ndithudi, anthuwo ali ngati phesi; adzapsa ndi moto. Sangathe kudzipulumutsa okha ku mphamvu ya malawi a moto. Awa si makala a moto woti wina nʼkuwotha; kapena moto woti wina nʼkuwukhalira pafupi.
Gle, oni su kao pljeva, oganj æe ih spaliti, ni sami sebe neæe izbaviti iz plamena; neæe ostati uglja da se ko ogrije, ni ognja da bi se posjedjelo kod njega.
15 Umu ndi mmene adzachitire amatsenga, anthu amene wakhala ukugwira nawo ntchito ndi kuchita nawo malonda chiyambire cha ubwana wako. Onse adzamwazika ndi mantha, sipadzakhala ndi mmodzi yemwe wokupulumutsa.”
Taki æe biti oni s kojima si se trudila i s kojima si trgovala od mladosti svoje, razbjeæi æe se svaki na svoju stranu; neæe biti nikoga da te izbavi.

< Yesaya 47 >