< Yesaya 46 >

1 Beli wagwada pansi, Nebo wawerama; nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo. Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe. Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.
Pade Vil, izvali se Nevo; likovi njihovi metnuše se na životinju i na stoku; što nosite, teško je, i umoriæe.
2 Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo; sizikutha kupulumutsa katunduyo, izo zomwe zikupita ku ukapolo.
Izvališe se, padoše svi, ne mogoše izbaviti tovara, nego i sami otidoše u ropstvo.
3 Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo, inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli, Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu, ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.
Slušajte me, dome Jakovljev i svi koji ste ostali od doma Izrailjeva, koje nosim od utrobe, koje držim od roðenja.
4 Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi ndidzakusamalirani ndithu. Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani, ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.
I do starosti vaše ja æu biti isti, i ja æu vas nositi do sijeda vijeka; ja sam stvorio i ja æu nositi, ja æu vas nositi i izbaviæu.
5 “Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani? Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?
S kim æete me izjednaèiti i isporediti? koga æete mi uzeti za priliku da bi bio kao ja?
6 Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo ndipo amayeza siliva pa masikelo; amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu, kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.
Prosipaju zlato iz toboca i mjere srebro na mjerila, plaæaju zlataru da naèini od njega boga, pred kojim padaju i klanjaju se.
7 Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo; amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo. Singathe kusuntha pamalo pakepo. Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha; kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.
Meæu ga na rame i nose ga, i postavljaju ga na mjesto njegovo, te stoji i ne mièe se s mjesta svojega; ako ga ko zove, ne odziva se niti ga izbavlja iz nevolje njegove.
8 “Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi, Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.
Pamtite to, i pokažite se da ste ljudi, uzmite na um, prestupnici!
9 Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana; chifukwa Ine ndine Mulungu ndipo palibe wina ofanana nane.
Pamtite što je bilo od starine; jer sam ja Bog, i nema drugoga Boga, i niko nije kao ja,
10 Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe. Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike. Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi. Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.
Koji od poèetka javljam kraj i izdaleka što još nije bilo; koji kažem: namjera moja stoji i uèiniæu sve što mi je volja.
11 Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa. Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa. Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi; zimene ndafuna ndidzazichitadi.
Zovem s istoka pticu i iz daljne zemlje èovjeka koji æe izvršiti što sam naumio. Rekoh i dovešæu to, naumih i uèiniæu.
12 Ndimvereni, inu anthu owuma mtima, inu amene muli kutali ndi chipulumutso.
Slušajte me, koji ste uporna srca, koji ste daleko od pravde.
13 Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa; sichili kutali. Tsikulo layandikira ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.
Približih pravdu svoju, nije daleko, i spasenje moje neæe odocniti, jer æu u Sionu postaviti spasenje, u Izrailju slavu svoju.

< Yesaya 46 >