< Yesaya 43 >

1 Koma tsopano, Yehova amene anakulenga, iwe Yakobo, amene anakuwumba, iwe Israeli akuti, “Usaope, pakuti ndakuwombola; Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.
And now the Lord God, makynge of nouyt thee, Jacob, and formynge thee, Israel, seith these thingis, Nyle thou drede, for Y ayenbouyte thee, and Y clepide thee bi thi name; thou art my seruaunt.
2 Pamene ukuwoloka nyanja, ndidzakhala nawe; ndipo pamene ukuwoloka mitsinje, sidzakukokolola. Pamene ukudutsa pa moto, sudzapsa; lawi la moto silidzakutentha.
Whanne thou schalt go bi watris, Y schal be with thee, and floodis schulen not hile thee; whanne thou schalt go in fier, thou schalt not be brent, and flawme schal not brenne in thee.
3 Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako, Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako. Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe, ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.
For Y am thi Lord God, the hooli of Israel, thi sauyour. I yaf thi merci Egipt; Ethiopie and Saba for thee.
4 Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga, ndipo chifukwa ndimakukonda, ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe, ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.
Sithen thou art maad onourable, and gloriouse in myn iyen; Y louyde thee, and Y schal yyue men for thee, and puplis for thi soule.
5 Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe; ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa, ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo.
Nyle thou drede, for Y am with thee; Y schal brynge thi seed fro the eest, and Y schal gadere thee togidere fro the west.
6 Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’ ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’ Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali, ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi;
Y schal seie to the north, Yyue thou, and to the south, Nyle thou forbede; brynge thou my sones fro afer, and my douytris fro the laste partis of erthe.
7 onsewo amadziwika ndi dzina langa; ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga, ndinawawumba, inde ndinawapanga.”
And ech that clepith my name to help, in to my glorie Y made hym of nouyt; Y fourmyde hym, and made hym.
8 Tulutsa anthu amene ali nawo maso koma sakupenya, anthu amene ali nawo makutu koma sakumva.
Lede thou forth the blynde puple, and hauynge iyen; the deef puple, and eeris ben to it.
9 Mitundu yonse ya anthu isonkhane pamodzi, anthu a mitundu ina akhale pamodzi pabwalo la milandu. Ndani wa iwo amene ananeneratu zimenezi? Ndani wa iwo anatifotokozerapo zinthu zakalekale? Abweretu ndi mboni zawo kuti adzatsimikizire kuti ananena zoona, kuti anthu ena amve ndi kunena kuti, “Ndi zoona.”
Alle hethene men ben gaderid togidere, and lynagis be gaderid togidere. Who among you, who schal telle this, and schal make you to here tho thingis, that ben the firste? yyue thei witnessis of hem, and be thei iustified, and here thei, and seie.
10 Yehova akunena kuti, “Inu Aisraeli ndinu mboni zanga, ndi mtumiki wanga amene ndinakusankha, kuti mundidziwe ndi kundikhulupirira, ndipo mudzamvetsa kuti Mulungu ndine ndekha. Patsogolo panga sipanapangidwepo mulungu wina, ngakhale pambuyo panga sipadzakhalaponso wina.”
Verili ye ben my witnessis, seith the Lord, and my seruaunt, whom Y chees; that ye wite, and bileue to me, and vndurstonde, for Y mysilf am; bifore me is no God formere, and after me schal noon be.
11 Akutero Yehova, “Ine, Inetu ndine Yehova, ndipo palibe Mpulumutsi wina koma Ine ndekha.
Y am, Y am the Lord, and with out me is no sauyour.
12 Ndine amene ndinaneneratu, amene ndinakupulumutsa; ndine, osati mulungu wina wachilendo pakati panu amene ndinalengezeratu. Inu ndinu mboni zanga, kuti Ine ndine Mulungu,” akutero Yehova.
I telde, and sauyde; Y made heryng, and noon alien God was among you. Ye ben my witnessis, seith the Lord;
13 “Ine ndine Mulungu kuyambira nthawi yamakedzana, ndipo ndidzakhalabe Mulungu ku nthawi zonse. Palibe amene angathe kuthawa mʼmanja mwanga, ndipo chimene ndachita palibe angathe kuchisintha.”
and Y am God fro the bigynnyng, Y my silf am, and noon is that delyuerith fro myn hoond; Y schal worche, and who schal distrie it?
14 Yehova akuti, Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti, “Chifukwa cha inu ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babuloni ndi kukupulumutsani. Ndidzagwetsa zitseko zonse za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.
The Lord, youre ayenbiere, the hooli of Israel, seith these thingis, For you Y sente out in to Babiloyne, and Y drow doun alle barris, and Caldeis hauynge glorie in her schippis.
15 Ine ndine Yehova, Woyera wanu uja, Mlengi wa Israeli. Ine ndine Mfumu yanu.”
Y am the Lord, youre hooli, youre king, makynge Israel of nouyt.
16 Yehova anapanga njira pa nyanja, anapanga njira pakati pa madzi amphamvu.
The Lord seith these thingis, that yaf weie in the see, and a path in rennynge watris;
17 Iye anasonkhanitsa magaleta, akavalo, gulu lankhondo ndi asilikali amphamvu, ndipo onse anagwa pamenepo, osadzukanso anazimitsidwa kutheratu ngati chingwe cha nyale. Yehova ameneyu akuti,
which ledde out a carte, and hors, a cumpany, and strong man; thei slepten togidere, nether thei schulen rise ayen; thei ben al tobrokun as flex, and ben quenchid.
18 “Iwalani zinthu zakale; ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale.
Thenke ye not on the formere thingis, and biholde ye not olde thingis.
19 Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano! Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona? Ine ndikulambula msewu mʼchipululu ndi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma.
Lo! Y make newe thingis, and now tho schulen bigynne to be maad; sotheli ye schulen know tho. Y schal sette weie in desert, and floodis in a lond without weie.
20 Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzi zinandilemekeza. Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowuma kuti ndiwapatse madzi anthu anga osankhidwa.
And a beeste of the feelde schal glorifie me, dragouns and ostrigis schulen glorifie me; for Y yaf watris in desert, and floodis in the lond without weie, that Y schulde yyue drynk to my puple, to my chosun puple.
21 Anthu amene ndinadziwumbira ndekha kuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine.
Y fourmyde this puple to me, it schal telle my preysyng.
22 “Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo, munatopa nane, Inu Aisraeli.
Jacob, thou clepidist not me to help; and thou, Israel, trauelidist not for me.
23 Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza, kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu. Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudya kapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza.
Thou offridist not to me the ram of thi brent sacrifice, and thou glorifiedist not me with thi slayn sacrifices. Y made not thee to serue in offryng, nethir Y yaf to thee trauel in encense.
24 Simunandigulire bango lonunkhira kapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu. Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anu ndipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu.
Thou bouytist not to me swete smellynge spicerie for siluer, and thou fillidist not me with fatnesse of thi slayn sacrifices; netheles thou madist me to serue in thi synnes, thou yauest trauel to me in thi wickidnessis.
25 “Ine, Inetu, ndi amene ndimafafaniza zolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini, ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu.
Y am, Y my silf am, that do awei thi wickidnessis for me, and Y schal not haue mynde on thy synnes.
26 Mundikumbutse zakale, ndipo titsutsane nkhaniyi pamodzi; fotokozani mlandu wanu kuti muonetse kuti ndinu osalakwa.
Brynge me ayen in to mynde, and be we demyd togidere; telle thou, if thou hast ony thing, that thou be iustified.
27 Kholo lanu loyamba linachimwa; ndipo Atsogoleri anu achipembedzo anandiwukira.
Thi firste fadir synnede, and thin interpretours trespassiden ayens me.
28 Chifukwa chake Ine ndidzanyazitsa akuluakulu a Nyumba yanu ya mapemphero, ndipo ndidzapereka Yakobo kuti awonongedwe ndi Israeli kuti achitidwe chipongwe.”
And Y made foul hooli princes, and Y yaf Jacob to deth, and Israel in to blasfemye.

< Yesaya 43 >