< Yesaya 28 >

1 Tsoka ufumu wonyada wa zidakwa za ku Efereimu. Tsoka kwa ulemerero wake wokongola umene ukufota ngati duwa limene lili pa mutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde.
Teško gizdavome vijencu pijanica Jefremovijeh, uvelom cvijetu krasnoga nakita njihova, koji su uvrh rodnoga dola, pijani od vina!
2 Taonani, ambuye ali naye wina wamphamvu ndi nyonga. Iye adzabwera ngati mkuntho wamatalala ndi namondwe wowononga, ngati madzi amphamvu osefukira a mvula yamkuntho; ndipo adzawagwetsa pansi mwankhanza.
Gle, u Gospoda ima neko jak i silan kao pljusak od grada, kao oluja koja sve lomi, kao poplava silne vode, kad navali, oboriæe sve na zemlju rukom.
3 Ulamuliro wa atsogoleri oledzera a ku Efereimu adzawuthetsa.
Nogama æe se izgaziti gizdavi vijenac, pijanice Jefremove.
4 Ndipo ulemerero wokongola wa mzinda umene uli ngati duwa lofota pamutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde uja, udzakhala ngati nkhuyu yoyambirira kupsa imene munthu akangoyiona amayithyola nthawi yokolola isanakwane.
I uveli cvijet krasnoga nakita njihova, što je uvrh rodnoga dola, biæe kao voæe uzrelo prije ljeta, koje èim ko vidi, uzme u ruku i pojede.
5 Tsiku limenelo Yehova Wamphamvuzonse adzakhala ngati nkhata yaufumu, chipewa chokongola kwa anthu ake otsala.
U ono æe vrijeme Gospod nad vojskama biti slavna kruna i dièan vijenac ostatku naroda svojega,
6 Iye adzapereka mtima wachilungamo kwa oweruza, adzakhala chilimbikitso kwa amene amabweza adani pa zipata za mzinda.
I duh suda onome koji sjedi da sudi, i sila onima koji uzbijaju boj do vrata.
7 Nawonso awa ali dzandidzandi chifukwa cha vinyo ndipo akusochera chifukwa cha mowa: ansembe ndi aneneri akudzandira chifukwa cha mowa ndipo akusokonezeka chifukwa cha vinyo; akusochera chifukwa cha mowa, akudzandira pamene akuona masomphenya, kupunthwa pamene akupereka chigamulo.
Ali se i oni zanose od vina, i posræu od silovita piæa; sveštenik i prorok zanose se od silovita piæa, osvojilo ih je vino, posræu od silovita piæa, zanose se u prorokovanju, spotièu se u suðenju.
8 Pa matebulo onse pali masanzi okhaokha ndipo palibenso malo wopanda zonyansa.
Jer su svi stolovi puni bljuvotine i neèistote, nema mjesta èista.
9 Iwo akuti, “Kodi munthu ameneyu akufuna aphunzitse ndani? Uthengawu akufuna kufotokozera yani? Ndi kwa ana amene aleka kuyamwa, kwa makanda ongowachotsa kumene ku bere?
Koga æe uèiti mudrosti, i koga æe uputiti da razumije nauku? Djecu, kojoj se ne daje više mlijeko, koja su odbijena od sise?
10 Akuyesa kumatiphunzitsa pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Zonsezi akungoti apa pangʼono apa pangʼono.”
Jer zapovijest po zapovijest, zapovijest po zapovijest, pravilo po pravilo, pravilo po pravilo, ovdje malo, ondje malo davaše se.
11 Mulungu adzayankhula kwa anthu ake kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo, ziyankhulo zosamveka bwino. Mulungu adzayankhula kwa anthu awa, amene
Zato æe nerazumljivom besjedom i tuðim jezikom govoriti tome narodu;
12 anakuwuzani kuti, “Malo opumulira ndi ano, otopa apumule, malo owusira ndi ano.” Koma inu simunamvere.
Jer im reèe: ovo je poèinak, ostavite umorna da poèine; ovo je odmor; ali ne htješe poslušati.
13 Choncho Yehova adzakuphunzitsani pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Kotero mudzayenda ndi kugwa chambuyo, adzapweteka ndi kukodwa mu msampha ndipo adzakutengani ku ukapolo.
I biæe im rijeè Gospodnja, zapovijest po zapovijest, zapovijest po zapovijest, pravilo po pravilo, pravilo po pravilo, malo ovdje, malo ondje, da idu i padaju nauznako i razbiju se, i da se zapletu u zamke i uhvate.
14 Nʼchifukwa chake imvani mawu a Yehova, inu anthu achipongwe amene mumalamulira anthu awa mu Yerusalemu.
Zato slušajte rijeè Gospodnju, ljudi potsmjevaèi, koji vladate narodom što je u Jerusalimu.
15 Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa, ife tachita mgwirizano ndi manda. Pamene mliri woopsa ukadzafika sudzatikhudza ife, chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.” (Sheol h7585)
Što rekoste: uhvatismo vjeru sa smræu, i ugovorismo s grobom; kad zaðe biè kao povodanj, neæe nas dohvatiti, jer od laži naèinismo sebi utoèište, i za prijevaru zaklonismo se; (Sheol h7585)
16 Tsono zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi: “Taonani, ndikuyika mwala wovomerezeka ndi amisiri ngati maziko mu Ziyoni, mwala wapangodya, wamtengowapatali wopanga maziko amphamvu; munthu amene awukhulupirira sadzagwedezeka.
Zato ovako veli Gospod Gospod: evo, ja meæem u Sionu kamen, kamen izabran, kamen od ugla, skupocjen, temelj tvrd; ko vjeruje neæe se plašiti.
17 Ntchito zolungama zidzakhala ngati chingwe choyezera maziko ake, ndipo chilungamo chidzakhala chowongolera mzere; matalala adzawononga malo anu othawirapo, amene ndi mabodza, ndipo madzi adzamiza malo anu obisalako.
I izvršiæu sud po pravilu i pravdu po mjerilima; i grad æe potrti lažno utoèište i voda æe potopiti zaklon.
18 Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa; mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa. Pakuti mliri woopsa udzafika, ndipo udzakugonjetsani. (Sheol h7585)
I vjera vaša sa smræu uništiæe se, i ugovor vaš s grobom neæe ostati, a kad zaðe biè kao povodanj, potlaèiæe vas. (Sheol h7585)
19 Ndipo ukadzangofika udzakutengani. Udzafika mmawa uliwonse, usiku ndi usana.” Anthu akadzamvetsetsa uthenga umenewu adzaopsedwa kwambiri.
Èim zaðe, odnijeæe vas, jer æe zalaziti svako jutro, danju i noæu, i kad se èuje vika, biæe sam strah.
20 Mudzakhala ngati munthu wogona pa bedi lalifupi kwambiri kuti sangathe kutambalitsapo miyendo; ndiponso mudzakhala ngati munthu amene wafunda bulangeti lochepa kwambiri kuti sangathe nʼkufunda komwe.
Jer æe odar biti kratak da se èovjek ne može pružiti, i pokrivaè uzak da se ne može umotati.
21 Yehova adzamenya nkhondo monga anachitira ku phiri la Perazimu adzakalipa monga anachitira ku chigwa cha Gibiyoni; adzagwira ntchito yake yooneka ngati yachilendo, ndipo zimene ati adzachite zidzakhala ngati zodabwitsa.
Jer æe Gospod ustati kao na gori Ferasimu, razgnjeviæe se kao u dolu Gavaonskom, da uèini djelo svoje, neobièno djelo svoje, da svrši posao svoj, neobièan posao svoj.
22 Tsopano lekani kunyoza, mukapanda kutero maunyolo anu adzakuthinani kwambiri; Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse wandiwuza kuti, “Ndagamula kuti ndidzawononga dziko lapansi.”
Nemojte se dakle više potsmijevati da ne postanu jaèi okovi vaši, jer èuh od Gospoda Gospoda nad vojskama pogibao odreðenu svoj zemlji.
23 Tcherani khutu ndipo mumve mawu anga; mvetserani ndipo mumve zimene ndikunena.
Slušajte, i èujte glas moj, pazite i èujte besjedu moju.
24 Kodi mlimi wofuna kudzala mbewu amangokhalira kutipula kokhakokha? Kodi amangokhalira kugawula ndi kugalawuza kokhakokha?
Ore li oraè svaki dan da posije? ili brazdi i povlaèi njivu svoju?
25 Pamene iye wasalaza mundawo, kodi samafesa mawere ndi chitowe? Kodi suja samadzala tirigu ndi barele mʼmizere yake, nadzala mchewere mʼphepete mwa mundawo?
Kad poravni ozgo, ne sije li grahor i kim? i ne meæe li pšenicu na najbolje mjesto, i jeèam na zgodno mjesto, i krupnik na njegovo mjesto?
26 Mulungu wake amamulangiza ndi kumuphunzitsa njira yabwino.
I Bog ga njegov uèi i upuæuje kako æe raditi.
27 Mawere sapunthira chopunthira cha galeta lopanda mikombero, kapena chitowe sapuntha popondetsapo mikombero ya galeta; mawere amapuntha ndi ndodo ndipo chitowe amapuntha ndi kamtengo.
Jer se grahor ne vrše branom, niti se toèak kolski obræe po kimu, nego se cijepom mlati grahor i kim prutom.
28 Tirigu ayenera kusinjidwa kuti apangire buledi, komabe munthu samangokhalira kupuntha tiriguyo osalekeza, kuopa kuti angatekedzeke. Ngakhale kuti amapuntha tiriguyo poyendetsapo mikombero ya galeta, koma akavalo ake satekedza tiriguyo.
Pšenica se vrše, ali neæe jednako vrijeæi niti æe je satrti toèkom kolskim ni zupcima razdrobiti.
29 Izinso zimachokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, wa uphungu wodabwitsa ndi wa nzeru zopambana.
I to dolazi od Gospoda nad vojskama, koji je divan u savjetu, velik u mudrosti.

< Yesaya 28 >