< Yesaya 27 >

1 Tsiku limenelo, Yehova ndi lupanga lake lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu, adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija, Leviyatani chinjoka chodzikulunga; adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.
Tada æe Gospod pokarati maèem svojim ljutijem i velikim i jakim levijatana, prugu zmiju, i levijatana, krivuljastu zmiju, i ubiæe zmaja koji je u moru.
2 Tsiku limenelo Yehova adzati, “Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
Tada pjevajte o vinogradu koji raða crvenijem vinom:
3 Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira; ndimawuthirira nthawi zonse. Ndimawulondera usana ndi usiku kuti wina angawononge.
Ja Gospod èuvam ga, u svako doba zaljevaæu ga; dan noæ èuvaæu ga da ga ko ne ošteti.
4 Ine sindinakwiye. Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo! Ndikachita nazo nkhondo; ndikanazitentha zonse ndi moto.
Nema gnjeva u mene; ko æe staviti u boj nasuprot meni èkalj i trnje? ja æu pogaziti i spaliti sve.
5 Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze; apangane nane za mtendere, ndithu, apangane nane za mtendere.”
Ili neka se uhvati za silu moju da uèini mir sa mnom; uèiniæe mir sa mnom.
6 Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu, Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa, ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.
Jednom æe se ukorijeniti Jakov, procvjetaæe i uzrasti Izrailj, i napuniæe vasiljenu plodom.
7 Kodi Yehova anakantha Israeli ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli? Kapena kodi Yehova anapha Israeli ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
Je li ga udario onako kako je udario one koji njega udaraše? je li ga ubio onako kako su ubijeni oni koje je ubio?
8 Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo, mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa, monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
S mjerom ga je karao, kad ga je odbacio, kad ga je odnio silnijem vjetrom svojim istoènijem.
9 Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo. Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja, ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha. Sipadzapezekanso mafano a Asera kapena maguwa ofukiza lubani.
Zato æe se tijem oèistiti bezakonje Jakovljevo i to æe biti sva korist što æe se uzeti grijeh njegov kad sve kamenje oltarno razmetne kao razdrobljeno kreèno kamenje i ne bude više gajeva ni sunèanijeh likova,
10 Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja, wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu; kumeneko amadyetselako ana angʼombe kumeneko zimapumulako ziweto ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
Jer æe tvrdi grad opustjeti i biæe stan ostavljen i zanemaren kao pustinja; ondje æe pasti tele i ondje æe lijegati, i poješæe mu grane.
11 Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni. Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru; kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni, ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.
Kad se posuše grane, polomiæe se; žene æe dolaziti i ložiti ih na oganj. Jer je narod nerazuman; zato ga neæe žaliti koji ga je stvorio, i koji ga je sazdao neæe se smilovati na nj.
12 Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto.
U to æe vrijeme Gospod ovijati od obale rijeke do potoka Misirskoga, a vi, sinovi Izrailjevi, sabraæete se jedan po jedan.
13 Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.
I tada æe se zatrubiti u veliku trubu, i koji se bjehu izgubili u zemlji Asirskoj i koji bijahu zagnani u zemlju Misirsku, doæi æe i klanjaæe se Gospodu na svetoj gori u Jerusalimu.

< Yesaya 27 >