< Yesaya 23 >

1 Uthenga wonena za Turo: Lirani mofuwula, inu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi: pakuti mzinda wa Turo wawonongedwa ndipo mulibe nyumba kapena dooko. Zimenezi anazimva pochokera ku Kitimu.
Breme Tiru. Ridajte laðe Tarsiske, jer je raskopan, da nema kuæe niti ko dolazi. Iz zemlje Kitimske javi im se.
2 Khalani chete inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja, inu amalonda a ku Sidoni, iwe amene unalemera ndi anthu oyenda pa nyanja.
Umuknite koji živite na ostrvu, koje trgovci Sidonski pomorci puniše.
3 Pa nyanja zazikulu panabwera tirigu wa ku Sihori; zokolola za ku Nailo, ndipo munachita malonda ndi anthu a mitundu ina.
I dohodi mu bijahu po velikim vodama sjeme Siorsko, žetva s rijeke, i bješe trg narodima.
4 Chita manyazi, iwe Sidimu pakuti nyanja yayankhula, linga la ku nyanja (Turo) layankhula kuti, “Sindinamvepo zowawa za kubereka kapena kuberekapo mwana; sindinalerepo ana aamuna kapena kulera ana aakazi.”
Stidi se, Sidone, jer govori more, sila morska veli: ne muèim se poroðajem, ne raðam, ne odgajam momaka, ne podižem djevojaka.
5 Mawuwa akadzamveka ku Igupto, iwo adzachita mantha akadzamva kuti Turo wawonongeka.
Kao što se ožalostiše kad èuše za Misir, tako æe se ožalostiti kad èuju za Tir.
6 Wolokerani ku Tarisisi, lirani mofuwula, inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja.
Idite u Tarsis, ridajte ostrvljani!
7 Kodi uwu si mzinda wachisangalalo uja, mzinda wakalekale, umene anthu ake ankapita kukakhala ku mayiko akutali?
Je li to vaš veseli grad, kojega je starina od davnina? njegove æe ga noge zanijeti daleko u tuðinstvo.
8 Kodi ndani anakonza zimenezi kuti zigwere Turo, mzinda umene unakhazikitsa mizinda ina, mzinda umene amalonda ake ndi akalonga ndi otchuka pa dziko lapansi?
Ko je to smislio na Tir, koji razdavaše vijence, èiji trgovci bjehu knezovi, i prekupci slavni na zemlji?
9 Yehova Wamphamvuzonse anakonza zimenezi kuti athetse kunyada kwawo ndi kutsitsa anthu otchuka a pa dziko lapansi.
Gospod je nad vojskama to smislio, da osramoti ponos svake slave i da poništi sve slavne na zemlji.
10 Mubalalike mʼdziko mwanu ngati mtsinje wa Nailo inu anthu a ku Tarisisi, pakuti mulibenso chokutetezani.
Prijeði preko zemlje svoje kao potok, kæeri Tarsiska; nema više pojasa.
11 Yehova watambasula dzanja lake kuloza ku nyanja ndipo wagwedeza maufumu ake. Iye walamula kuti Kanaani agwetse malinga ake.
Ruku svoju podiže na more, zadrma carstva; Gospod je zapovjedio za Hanan da se raskopaju gradovi njegovi.
12 Iye anati, “Simudzakondwanso konse, inu anthu opanikizidwa a ku Sidoni, tsopano wamphwanyidwa! “Ngakhale muwolokere ku Kitimu, kumeneko simukapezako mpumulo.”
I veli: neæeš se više veseliti, osramoæena djevojko, kæeri Sidonska. Ustani, idi u Kitim, ni ondje neæeš imati mira.
13 Onani dziko la Ababuloni, anthu amenewa tsopano atheratu! Asiriya asandutsa Turo kukhala malo a zirombo za ku chipululu; anamanga nsanja zawo za nkhondo, anagumula malinga ake ndipo anawasandutsa bwinja.
Eto zemlje Haldejske; toga naroda nije bilo; Asur je osnova za one koji življahu u pustinjama, podigoše kule u njoj, pogradiše dvorove; i obrati se u razvaline.
14 Lirani mofuwula, inu anthu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi; chifukwa malinga ako agwetsedwa!
Ridajte laðe Tarsiske, jer je raskopan vaš grad.
15 Pa nthawi imeneyo Turo adzayiwalika pa zaka 70, amene ndi masiku a moyo wa mfumu. Koma potsiriza pa zaka 70 zimenezi, Turo adzakhala ngati mkazi wachiwerewere woyimbidwa mu nyimbo:
I tada æe Tir biti zarobljen sedamdeset godina, za vijek jednoga cara, a poslije sedamdeset godina pjevaæe se Tiru kao kurvi:
16 “Tenga zeze wako uzungulire mzinda, iwe mkazi wachiwerewere woyiwalika; imba zeze mokometsera, imba nyimbo zambiri, kuti anthu akukumbukire.”
Uzmi gusle, idi po gradu, zaboravljena kurvo; dobro udaraj, pjevaj i popijevaj, eda bi te se opet opomenuli.
17 Pakutha pa zaka 70, Yehova adzachitapo kanthu pa Turo. Iye adzabwerera ku ntchito yake yakale monga mkazi wachiwerewere ndipo adzachita zachiwerewere ndi maufumu onse a dziko lapansi.
Jer poslije sedamdeset godina Gospod æe pohoditi Tir, a on æe se vratiti na kurvarsku zaslugu svoju, i kurvaæe se sa svijem carstvima na zemlji.
18 Koma phindu lake ndi malipiro ake adzazipereka kwa Yehova; sadzazikundika kapena kuzisunga. Phindu lake lidzapita kwa mtumiki wa Yehova kuti agule zakudya zambiri ndi zovala zokongola.
Ali æe trgovina njegova i zasluga njegova biti posveæena Gospodu, neæe se ostavljati ni èuvati, nego æe trgovina njegova biti onima koji nastavaju pred Gospodom da jedu do sitosti i imaju odijelo dobro.

< Yesaya 23 >