< Yesaya 22 >

1 Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya: Kodi chachitika nʼchiyani, kuti nonsenu mukwere pa madenga?
Breme dolini viðenja. Što ti je te si sva izašla na krovove?
2 Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya, iwe mzinda waphokoso ndi wosokonekera? Anthu ako ophedwa aja sanaphedwe ndi lupanga, kapena kufera pa nkhondo.
Grade puni vike i vreve, grade veseli! tvoji pobijeni nijesu pobijeni maèem niti pogiboše u boju.
3 Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi; koma anagwidwa osadziteteza nʼkomwe. Inu munapezeka ndipo nonse pamodzi munatengedwa ukapolo, ngakhale munathawa pamene mdani akanali patali.
Glavari tvoji uzmakoše svikoliki, povezaše ih strijelci; što se god naðe tvojih, svi su povezani, ako i pobjegoše daleko.
4 Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga; ndilekeni ndilire ndi mtima wowawa. Musayesere kunditonthoza chifukwa cha kuwonongeka kwa anthu anga.”
Zato rekoh: proðite me se, da plaèem gorko; ne trudite se da me tješite za pogiblju kæeri naroda mojega.
5 Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione mavuto ndi kugonjetsedwa ndiponso chisokonezo mʼChigwa cha Masomphenya. Malinga agumuka, komanso anthu akanalira mofuwula ku mapiri.
Jer je ovo dan muke i potiranja i smetnje od Gospoda, Gospoda nad vojskama, u dolini viðenja; obaliæe zid, i vika æe biti do gore.
6 Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta ndi akavalo ali ndi mivi mʼmanja. Ankhondo a ku Kiri anakonzeka ndi zishango.
I Elam uze tul, s kolima ljudi i s konjicima, i Kir istaèe štit.
7 Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta, ndipo asilikali okwera pa akavalo ayikidwa pa zipata za mzinda;
I krasne doline tvoje napuniše se kola, i konjici se namjestiše pred vratima.
8 zonse zoteteza Yuda zachotsedwa. Ndipo tsiku limenelo munayangʼanayangʼana zida zankhondo zomwe zinali mʼnyumba yaufumu ya nkhalango;
I odastrije se zastiraè Judin; i pogledao si u to vrijeme na oružje u kuæi šumskoj.
9 inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide anali ndi malo ambiri ogumuka; munasunga madzi mu chidziwe chakumunsi.
I vidjeste da je mnogo proloma na gradu Davidovu, i sabraste vodu u donjem jezeru.
10 Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu ndipo munagwetsa nyumba zina kuti mulimbitse linga logumuka lija.
I izbrojiste kuæe Jerusalimske, i razvaliste kuæe da utvrdite zid.
11 Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime chosungiramo madzi ochokera ku dziwe lakale, koma inu simunadalire Mulungu amene anapanga zimenezi, kapena kusamalako za Iye amene anazilenga kale lomwe.
I naèiniste jaz meðu dva zida za vodu iz staroga jezera; ali ne pogledaste na onoga koji je to uèinio i ne obazreste se na onoga koji je to odavna spremio.
12 Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse anakuyitanani kuti mulire ndi kukhetsa misozi; kumeta mutu wanu mpala ndi kuvala ziguduli.
I zva vas Gospod nad vojskama u onaj dan da plaèete i ridate i da skubete kose i pripašete kostrijet;
13 Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala; munapha ngʼombe ndi nkhosa; munadya nyama ndi kumwa vinyo. Inu mumati, “Tiyeni tidye ndi kumwa pakuti mawa tifa!”
A gle, radost i veselje, ubijaju goveda, kolju ovce, jedu meso i piju vino govoreæi: jedimo i pijmo, jer æemo sjutra umrijeti.
14 Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.
Ali Gospod nad vojskama javi mi: neæe vam se oprostiti ovo bezakonje do smrti, veli Gospod, Gospod nad vojskama.
15 Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pita, ukanene kwa Sabina kapitawo, amene amayangʼanira nyumba yaufumu:
Ovako veli Gospod, Gospod nad vojskama: idi k onomu riznièaru, k Somni, upravitelju dvorskom,
16 Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo kuti udzikumbire manda kuno, kudzikumbira manda pa phiri ndi kudzisemera malo opumulira mʼthanthwe?
I reci mu: šta æeš ti tu? i ko ti je tu? te si tu istesao sebi grob? istesao si sebi grob na visoku mjestu i spremio si sebi stan u kamenu.
17 “Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba ndi kukuponya mwamphamvu, iwe munthu wamphamvu.
Evo, èovjeèe, Gospod æe te baciti daleko i zatrpaæe te.
18 Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira ndipo adzakuponyera mʼdziko lalikulu. Kumeneko ndiko ukafere ndipo kumeneko ndiko kudzatsalire magaleta ako. Ndipo udzasanduka wochititsa manyazi nyumba ya mbuye wako.
Zavitlaæe te i hititi kao loptu u zemlju prostranu; ondje æeš umrijeti i ondje æe biti kola slave tvoje, sramoto domu gospodara svojega;
19 Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako ndipo ndidzakutsitsa pa udindo wako.
I svræi æu te s mjesta tvojega, i istjeraæu te iz službe tvoje.
20 “Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya.
I u to vrijeme pozvaæu slugu svojega Elijakima sina Helkijina;
21 Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda.
I obuæi æu mu tvoju haljinu, i tvojim æu ga pojasom opasati, i tvoju æu mu vlast dati u ruku, i biæe otac Jerusalimljanima i domu Judinu.
22 Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula.
I metnuæu mu kljuè od doma Davidova na rame: kad on otvori, neæe niko zatvoriti, i kad on zatvori, neæe niko otvoriti.
23 Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye.
I kao klin uglaviæu ga na tvrdu mjestu, i biæe prijesto slave domu oca svojega;
24 Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.
I o njemu æe se vješati sva slava doma oca njegova, sinova i unuka, svakojaki sudovi, i najmanji, i èaše i mjehovi.
25 “Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’” Yehova wayankhula chomwechi.
U to vrijeme, veli Gospod nad vojskama, pomjeriæe se klin uglavljeni na tvrdom mjestu, i izvadiæe se i pašæe, i teža što je na njemu propašæe; jer Gospod reèe.

< Yesaya 22 >