< Yesaya 17 >

1 Uthenga wonena za Damasiko: “Taonani, mzinda wa Damasiko sudzakhalanso mzinda, koma udzasanduka bwinja.
The birthun of Damask. Lo! Damask schal faile to be a citee, and it schal be as an heep of stoonys in fallyng.
2 Mizinda ya Aroeri idzakhala yopanda anthu ndipo idzakhala ya ziweto, zimene zidzagona pansi popanda wina woziopseza.
The forsakun citees of Aroer schulen be to flockis; and tho schulen reste there, and noon schal be that schal make aferd.
3 Ku Efereimu sikudzakhalanso linga, ndipo ku Damasiko sikudzakhalanso ufumu; Otsalira a ku Siriya adzachotsedwa ulemu monga anthu a ku Israeli,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
And help schal ceesse fro Effraym, and a rewme fro Damask; and the relifs of Sirie schulen be as the glorie of the sones of Israel, seith the Lord of oostis.
4 “Tsiku limenelo ulemerero wa Yakobo udzazimirira; ndipo chuma chake chidzasanduka umphawi.
And it schal be, in that dai the glorie of Jacob schal be maad thinne, and the fatnesse of his fleisch shal fade.
5 Israeli adzakhala ngati munda wa tirigu umene anatsiriza kukolola. Adzakhalanso ngati munda wa mʼchigwa cha Refaimu anthu atatha kukunkha ngala za tirigu.
And it schal be as gaderyng togidere that that is left in heruest, and his arm schal gadere eeris of corn, and it schal be as sekynge eeris of corn in the valei of Raphaym.
6 Komabe Aisraeli ochepa okha ndiwo ati adzatsale monga mʼmene zimatsalira zipatso ziwiri kapena zitatu pa nthambi ya pamwamba penipeni kapena zipatso zisanu pa nthambi za mʼmunsi mwa mtengo wa olivi akawugwedeza,” akutero Yehova, Mulungu wa Israeli.
And there schal be left in it as a rasyn, and as the schakyng doun of the fruyt of olyue tre, as of tweyne ether of thre olyue trees in the hiynesse of a braunche, ether of foure ether of fyue; in the cooppis therof schal be the fruyt therof, seith the Lord God of Israel.
7 Tsiku limenelo anthu adzayangʼana Mlengi wawo ndipo adzatembenukira kwa Woyerayo wa Israeli.
In that dai a man schal be bowid to his maker, and hise iyen schulen biholde to the hooli of Israel.
8 Iwo sadzakhulupiriranso maguwa ansembe, ntchito ya manja awo, ndipo sadzadaliranso mitengo ya mafano a Asera, ndiponso maguwa ofukizirapo lubani amene manja awo anapanga.
And he schal not be bowid to the auteris, whiche hise hondis maden, and whiche hise fyngris wrouyten; he schal not biholde wodis, and templis of idols.
9 Tsiku limenelo mizinda yawo yamphamvu, imene anasiya chifukwa cha Aisraeli, idzakhala ngati malo osiyidwa kuti awirire ndi kumera ziyangoyango. Ndipo yonse idzakhala mabwinja.
In that dai the citees of strengthe therof schulen be forsakun as plowis, and cornes that weren forsakun of the face of the sones of Israel; and thou schalt be forsakun.
10 Inu mwayiwalatu Mulungu Mpulumutsi wanu; simunakumbukire Thanthwe, linga lanu. Choncho, ngakhale munadzala mbewu zabwino, ndi kuyitanitsa kunja mitengo ya mpesa,
For thou hast foryete God, thi sauyour, and haddist not mynde on thi stronge helpere; therfor thou schalt plaunte a feithful plauntyng, and thou schalt sowe an alien seed.
11 nimuyembekeza kuti zikule tsiku lomwelo ndi kuphukira maluwa mmawa mwake, komabe zimenezi sizidzakupindulirani pa tsiku la mavuto.
In the dai of thi plauntyng schal be a wielde vyne, and erli thi seed schal floure; ripe corne is takun awei in the dai of eritage, and Israel schal make sorewe greuousli.
12 Aa, mkokomo wa anthu a mitundu yambiri, akusokosa ngati kukokoma kwa nyanja! Aa, phokoso la anthu a mitundu ina, akusokosa ngati mkokomo wa madzi amphamvu!
Wo to the multitude of many puplis, as the multitude of the see sownynge, and the noise of cumpenyes as the sown of many watris.
13 Ngakhale ankhondo a mitundu ina akubwera ndi mkokomo ngati wa madzi ambiri, koma adzathawira kutali Mulungu akadzawadzudzula. Yehova adzawapirikitsa ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pa phiri, ndi ngati fumbi la kamvuluvulu asanayambe.
Puplis schulen sowne as the sown of flowynge watris, and God schal blame hym; and he schal fle fer, and he schal be rauyschid as the dust of hillis fro the face of the wynd, and as a whirlewynd bifor tempest.
14 Pofika nthawi yamadzulo zoopsa zidzayamba kuchitika, ndipo zidzakhala zitatha pofika mmawa. Izi ndizo zidzachitikire anthu otilanda zinthu, gawo la amene amatibera zinthu zathu.
In the time of euentide, and lo! disturbling; in the morewtid, and he schal not abide. This is the part of hem that destrieden vs, and the part of hem that rauyschiden vs.

< Yesaya 17 >