< Genesis 7 >

1 Ndipo Yehova anati kwa Nowa, “Lowa mu chombo iwe ndi banja lako lonse, chifukwa ndaona kuti ndiwe wolungama mu mʼbado uwu.
Also the Lord seide to Noe, Entre thou and al thin hous in to the schip, for Y seiy thee iust bifore me in this generacioun.
2 Pa mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya utengepo zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi zazikazi zisanu ndi ziwirinso. Koma pa mtundu wa nyama iliyonse yosati nʼkudya utengepo zazimuna ziwiri ndi zazikazi ziwirinso.
Of alle clene lyuynge beestis thou schalt take bi seuene and bi seuene, male and female; forsothe of vnclene lyuynge beestis thou schalt take bi tweyne and bi tweyne, male and female;
3 Chimodzimodzinso mbalame, utenge zisanu ndi ziwiri zazimuna ndi zisanu ndi ziwiri zazikazi za mtundu uliwonse kuti mitundu yawo isungike ndi moyo pa dziko lonse lapansi.
but also of volatils of heuene thou schalt take, bi seuene and bi seuene, male and female, that her seed be saued on the face of al erthe.
4 Pakapita masiku asanu ndi awiri ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku ndipo ndidzawononga cha moyo chilichonse chimene ndinachipanga pa dziko lapansi.”
For yit and aftir seuene daies Y schal reyne on erthe fourti daies and fourti nyytis, and Y schal do awey al substaunce which Y made, fro the face of erthe.
5 Ndipo Nowa anachita zonse zimene Yehova anamulamulira.
Therfor Noe dide alle thingis whiche the Lord comaundide to hym.
6 Pamene chigumula chinabwera pa dziko lapansi Nowa anali ndi zaka 600.
And he was of sixe hundrid yeer, whanne the watris of the greet flood flowiden on erthe.
7 Ndipo Nowa, ana ake aamuna, mkazi wake, pamodzi ndi ana ake aakazi analowa mu chombo chija kuthawa madzi a chigumula.
And Noe entride in to the schip, and hise sones, and hise wijf, and the wyues of his sones, entriden with him for the watris of the greet flood.
8 Nyama zoti nʼkudya ndi nyama zosadyedwa, mbalame, pamodzi ndi nyama zokwawa zonse zinadza kwa Nowa ziwiriziwiri ndi kulowa mʼchombomo.
And of lyuynge beestis clene and vnclene, and of briddis of heuene, and of ech beeste which is moued on erthe,
9 Ndipo Nowa anatenga ziwiriziwiri, yayimuna ndi yayikazi monga anamulamulira Mulungu.
bi tweyne and bi tweyne, male and female entriden to Noe in to the schip, as the Lord comaundide to Noe.
10 Patapita masiku asanu ndi awiri chigumula chinabwera pa dziko lapansi.
And whanne seuene daies hadden passid, the watris of the greet flood flowiden on erthe.
11 Pa tsiku la 17 la mwezi wachiwiri, Nowa ali ndi zaka 600, akasupe onse akuya kwambiri anasefuka ndiponso zitseko za madzi akumwamba zinatsekuka.
In the sixe hundrid yeer of the lijf of Noe, in the secunde moneth, in the seuententhe dai of the moneth, alle the wellis of the greet see weren brokun, and the wyndowis of heuene weren opened,
12 Ndipo mvula inagwa pa dziko lapansi masiku makumi anayi usana ndi usiku.
and reyn was maad on erthe fourti daies and fourti nyytis.
13 Linali tsiku lomwelo pamene Nowa ndi ana ake aamuna, Semu, Hamu ndi Yafeti, pamodzi ndi mkazi wake ndi akazi a ana ake atatu aja analowa mu chombo.
In the ende of that dai Noe entride, and Sem, Cham, and Japheth, hise sones, his wijf, and the wyues of hise sones, entriden with hem into the schip.
14 Iwowa analowa mʼchombomo pamodzi ndi nyama iliyonse ya kutchire monga mwa mtundu wake, ziweto zonse monga mwa mitundu yawo, nyama yokwawa iliyonse monga mwa mtundu wake ndi mbalame iliyonse monga mwa mtundu wake.
Thei entriden, and ech beeste bi his kynde, and alle werk beestis in her kynde, and ech beeste which is moued on erthe in his kynde, and ech volatil bi his kynde; alle briddis and alle volatils entriden to Noe in to the schip,
15 Nowa analowa mu chombo muja pamodzi ndi zamoyo zonse.
bi tweyne and bi tweyne of ech fleisch in whiche the spirit of lijf was.
16 Iye analowa nazo zazimuna ndi zazikazi monga mmene Mulungu anamulamulira. Kenaka Yehova anatseka pa khomo.
And tho that entriden, entriden male and female of ech fleisch, as God comaundide to hym. And the Lord encloside hym fro with out-forth.
17 Chigumula chinagwa pa dziko la pansi kwa masiku makumi anayi. Madzi anayamba kuchuluka ndipo ananyamula chombo chija ndi kuchiyandamitsa pamwamba pa dziko.
And the greet flood was maad fourti daies and fourti niytis on erthe, and the watris weren multiplied, and reiseden the schip on hiy fro erthe.
18 Madzi anafika mwamphamvu ndipo anachulukirachulukira pa dziko lapansi moti chombo chinayandama pamwamba pa madziwo.
The watris flowiden greetli, and filliden alle thingis in the face of erthe. Forsothe the schip was borun on the watris.
19 Madzi a chigumula anabwerabe molimbika motero kuti mapiri ataliatali onse a pa dziko anamizidwa.
And the watris hadden maistrie greetli on erthe, and alle hiye hillis vndur alle heuene weren hilid;
20 Madzi anakwera namiza mapiri kwa mamita pafupifupi asanu ndi awiri.
the watyr was hiyere bi fiftene cubitis ouer the hilis whiche it hilide.
21 Chamoyo chilichonse choyenda pa dziko lapansi chinafa: mbalame, ziweto, nyama zakuthengo, miyandamiyanda ya zonse zolengedwa za pa dziko lapansi pamodzi ndi anthu.
And ech fleisch was wastid that was moued on erthe, of briddis, of lyuynge beestis, of vnresonable beestis, and of alle `reptilis that crepen on erthe.
22 Chilichonse chamoyo, chokhala pa mtunda chinafa.
Alle men, and alle thingis in whiche the brething of lijf was in erthe, weren deed.
23 Chamoyo chilichonse pa dziko lapansi chinawonongedwa, kuyambira munthu, nyama, zokwawa ndi mbalame. Nowa yekha ndiye anatsala pamodzi ndi onse amene anali naye.
And God dide awei al substaunce that was on erthe, fro man til to beeste, as wel a crepynge beeste as the briddis of heuene; and tho weren doon awei fro erthe. Forsothe Noe dwellide aloone, and thei that weren with hym in the schip.
24 Madziwo anadzaza dziko lonse lapansi kwa masiku 150.
And the watris of the greet flood ouereyeden the erthe an hundrid and fifti daies.

< Genesis 7 >

The Great Flood
The Great Flood