< Genesis 6 >

1 Anthu atayamba kuchuluka pa dziko lapansi ndi kubereka ana aakazi,
And whanne men bigunnen to be multiplied on erthe, and hadden gendrid douytris,
2 ana aamuna a Mulungu anaona kuti ana aakazi a anthuwo anali okongola. Ndipo anakwatira aliyense amene anamusankha.
the sones of God seiyen the douytris of men that thei weren faire, and token wyues to hem of alle whiche thei hadden chose.
3 Tsono Yehova anati, “Sindilola kuti chipwirikiti chikuchitikachi chipitirire mpaka muyaya, pakuti iye ndi munthu; masiku a moyo wake adzakhala zaka 120.”
And God seide, My spirit schal not dwelle in man with outen ende, for he is fleisch; and the daies of hym schulen be an hundrid and twenti yeer.
4 Masiku amenewo komanso pambuyo pake, pa dziko lapansi panali Anefili, anthu amphamvu ndiponso otchuka. Anthuwa ndi amene ankabadwa ana a Mulungu aja atakwatira ana aakazi a anthu.
Sotheli giauntis weren on erthe in tho daies, forsothe aftir that the sones of God entriden to the douytris of men, and tho douytris gendriden; these weren myyti of the world and famouse men.
5 Pamene Yehova anaona kuti kuyipa kwa munthu pa dziko lapansi kunali kwakukulu ndi kuti nthawi zonse amalingalira ndi kukhumbira kuchita zoyipa zokhazokha,
Sotheli God seiy that myche malice of men was in erthe, and that al the thouyt of herte was ententif to yuel in al tyme,
6 Yehova anamva chisoni kuti analenga munthu ndi kumuyika pa dziko lapansi, ndipo anawawidwa mtima.
and repentide him that he hadde maad man in erthe; and God was war bifore ayens tyme to comyng, and was touchid with sorewe of herte with ynne;
7 Choncho Yehova anati, “Ndidzafafaniza munthu, nyama, zonse zokwawa, ndi mbalame za mu mlengalenga pa dziko lapansi, pakuti ndikumva chisoni kuti ndinazilenga zimenezi.”
and seide, Y schal do awei man, whom Y made of nouyt, fro the face of the erthe, fro man til to lyuynge thingis, fro crepynge beeste til to the briddis of heuene; for it repentith me that Y made hem.
8 Koma Yehova anamukomera mtima Nowa.
Forsothe Noe foond grace bifore the Lord.
9 Mbiri ya Nowa inali yotere: Nowa anali munthu wolungama ndi wopanda tchimo pakati pa anthu a mʼbado wake. Ndipo anayenda ndi Mulungu.
These ben the generaciouns of Noe. Noe was a iust man and perfit in hise generaciouns; Noe yede with God,
10 Nowa anabereka ana aamuna atatu: Semu, Hamu ndi Yafeti.
and gendride thre sones, Sem, Cam, and Jafeth.
11 Chiwawa chinadzaza pa dziko lapansi kotero kuti dziko linakhala lowonongeka pamaso pa Mulungu.
Forsothe the erthe was corrupt bifore God, and was fillid with wickidnes.
12 Mulungu atayangʼana, anaona kuti dziko layipadi chifukwa cha makhalidwe oyipa a anthu onse pa dziko lapansi.
And whanne God seiy, that the erthe was corrupt, for ech fleisch ether man hadde corrupt his weie on erthe,
13 Ndipo Mulungu anati kwa Nowa, “Ndatsimikiza mtima kuti ndiwononge anthu onse, pakuti dziko lapansi ladzaza ndi ntchito zawo zoyipa. Ndithudi ndiwawononga pamodzi ndi zonse za pa dziko.
he seide to Noe, The ende of al fleisch is comen bifore me; the erthe is fillid with wickidnesse of the face of hem, and Y schal distrye hem with the erthe.
14 Tsono udzipangire chombo cha matabwa a mtengo wanjale; mʼkati mwake upange zipinda ndipo upake phula mʼkati ndi kunja.
Make thou to thee a schip of trees hewun and planed; thou schalt make dwellynge placis in the schip, and thou schalt anoynte it with pitche with ynne and with outforth.
15 Uchipange motere: Chombo chikhale mamita 140 mulitali, mamita 23 mulifupi ndi mamita 13 mu msinkhu wake.
And so thou schalt make it. The lengthe of the schip schal be of thre hundrid cubitis, the brede schal be of fifti cubitis, and the hiynesse therof schal be of thretti cubitis.
16 Uchipangire denga ndi kuchimaliza ndi zenera la masentimita makumi asanu. Uyike khomo mʼmbali mwa chombocho ndi kupanga zipinda zosanjikana; chapansi, chapakati ndi chapamwamba.
Thou schalt make a wyndow in the schip, and thou schalt ende the hiynesse therof in a cubite; sotheli thou schalt sette the dore of the schip in the side binethe; thou shalt make soleris and placis of thre chaumbris in the schip.
17 Ndidzagwetsa mvula ya chigumula pa dziko lapansi kuti ndiwononge zamoyo zonse za pansi pa thambo ndipo chilichonse cha pa dziko lapansi chidzafa.
Lo! Y schal brynge `watris of diluuye ether greet flood on erthe, and Y schal sle ech fleisch in which is the spirit of lijf vndir heuene, and alle thingis that ben in erthe, schulen be wastid.
18 Koma ndidzachita pangano langa ndi iwe. Iwe, ana ako aamuna, mkazi wako ndi akazi a ana ako nonse mudzalowa mʼchombocho.
And Y schal sette my couenaunt of pees with thee; and thou schalt entre in to the schip, and thy sones, and thi wijf, and the wiues of thi sones schulen entre with thee.
19 Iwe udzalowa mʼchombocho ndi zolengedwa zamoyo zonse ziwiriziwiri, chachimuna ndi chachikazi, kuti zisungike ndi moyo pamodzi ndi iwe.
And of alle lyuynge beestis of al fleisch thou schalt brynge in to the schip tweyne and tweyne, of male kynde and female, that thei lyue with thee;
20 Udzatenga ziwiriziwiri za mitundu yonse ya mbalame, mitundu yonse ya nyama, ndi mitundu yonse ya zokwawa kuti zikhale ndi moyo.
of briddis bi her kynde, and of werk beestis in her kynde, and of ech crepynge beeste of erthe, by her kynde; tweyne and tweyne of alle schulen entre with thee, that thei moun lyue.
21 Udzatengenso chakudya cha mtundu uliwonse ndi kuchisunga kuti inu ndi nyamazo muzidzadya.”
Therfore thou schalt take with thee of alle metis that moun be etun, and thou schalt bere to gidre at thee, and tho schulen be as well to thee as to the beestis in to mete.
22 Nowa anachita zonse monga Mulungu anamulamulira.
Therfor Noe dide alle thingis whiche God comaundide to hym.

< Genesis 6 >

The World is Destroyed by Water
The World is Destroyed by Water