< Genesis 45 >

1 Tsono Yosefe sanathenso kuwugwira mtima kuti asalire pamaso pa antchito ake ndipo anafuwula kuti, “Aliyense achoke pamaso panga!” Motero panalibe wina aliyense pamene Yosefe anadziwulula kwa abale ake.
Tada Josif ne moguæi se uzdržati pred ostalima koji stajahu oko njega, povika: izaðite svi napolje. Tako ne osta niko kod njega kad se Josif pokaza braæi svojoj.
2 Ndipo analira mokweza mwakuti Aigupto anamva. Onse a ku nyumba kwa Farao anamvanso za zimenezi.
Pa briznu plakati tako da èuše Misirci, èu i dom Faraonov.
3 Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndine Yosefe! Kodi abambo anga akanali ndi moyo?” Koma abale ake sanathe kumuyankha chifukwa anali ndi mantha kwambiri pamaso pake.
I reèe Josif braæi svojoj: ja sam Josif; je li mi otac još u životu? Ali mu braæa ne mogahu odgovoriti, jer se prepadoše od njega.
4 Ndipo Yosefe anati kwa abale ake, “Senderani pafupi nane.” Atasendera iye anati, “Ine ndine mʼbale wanu Yosefe amene munamugulitsa ku Igupto!
A Josif reèe braæi svojoj: pristupite bliže k meni. I pristupiše; a on reèe: ja sam Josif brat vaš, kojega prodadoste u Misir.
5 Ndipo tsopano, musawawidwe mtima kapena kudzipsera mtima chifukwa choti munandigulitsa ine kuno, popeza Mulungu ananditsogoza ine kuti adzapulumutse miyoyo yanu.
A sada nemojte žaliti niti se kajati što me prodadoste ovamo, jer Bog mene posla pred vama radi života vašega.
6 Kwa zaka ziwiri tsopano, kwakhala kuli njala mʼdziko muno, ndipo kwa zaka zisanu zikubwerazi, anthu sadzalima kapena kukolola.
Jer je veæ dvije godine dana glad u zemlji, a biæe još pet godina, gdje neæe biti ni oranja ni žetve.
7 Koma Mulungu ananditsogoza kuti adzakusungeni ndi moyo ndi kuti mudzakhale ndi zidzukulu pa dziko lapansi.
A Bog me posla pred vama, da vas saèuva na zemlji i da vam izbavi život izbavljanjem prevelikim.
8 “Motero, si inu amene munanditumiza kuno koma Mulungu. Iye anandisandutsa kukhala nduna yayikulu ya Farao, ndipo zonse za mʼnyumba mwake zili mʼmanja mwangamu. Komanso amene akulamulira dziko lonse la Igupto ndi ine.
I tako nijeste me vi opravili ovamo nego sam Bog, koji me postavi ocem Faraonu i gospodarem od svega doma njegova i starješinom nad svom zemljom Misirskom.
9 Tsono fulumirani mubwerere kwa abambo anga ndi kuwawuza kuti, ‘Mwana wanu Yosefe akuti, Mulungu anandisandutsa kukhala mbuye wa dziko lonse la Igupto. Ndiye bwerani kuno musachedwe.
Vratite se brže k ocu mojemu i kažite mu: ovako veli sin tvoj Josif: Bog me je postavio gospodarem svemu Misiru, hodi k meni, nemoj oklijevati.
10 Ndipo inu, ana anu, zidzukulu zanu, pamodzi ndi nkhosa ndi ngʼombe zanu ndi antchito anu amene muli nawo muzidzakhala mʼdziko la Goseni pafupi ndi ine.
Sjedjeæeš u zemlji Gesemskoj i biæeš blizu mene, ti i sinovi tvoji i sinovi sinova tvojih, i ovce tvoje i goveda tvoja i što je god tvoje.
11 Ine ndizidzakupatsani zakudya kumeneko chifukwa zaka zisanu za njala zikubwera ndithu. Kupanda kutero, inu ndi mabanja anu pamodzi ndi anthu anu onse mudzasowa chakudya.’
I ja æu te hraniti ondje, jer æe još pet godina biti glad, da ne pogineš od gladi ti i dom tvoj i što je god tvoje.
12 “Tsono inu nonse pamodzi ndi mʼbale wangayu Benjamini, mukuona kuti ndi inedi amene ndikuyankhula nanu.
A eto vidite oèima svojima, i brat moj Venijamin svojima oèima, da vam ja iz usta govorim.
13 Mukawawuze abambo anga kuti ndili pa ulemerero ku dziko la Igupto kuno ndi zonse zimene mwaziona. Tsopano fulumirani kuti mukabwere nawo kuno abambo anga.”
Kažite ocu mojemu svu slavu moju u Misiru i što ste god vidjeli; pohitajte i dovedite ovamo oca mojega.
14 Kenaka Yosefe anakhumbatira Benjamini, mngʼono wake uja nayamba kulira. Nayenso Benjamini anayamba kulira atamukumbatira.
Tada pade oko vrata Venijaminu bratu svojemu i plaka. I Venijamin plaka o vratu njegovu.
15 Atatero, Yosefe anapsompsona abale ake onse aja, akulira. Pambuyo pake abale ake aja anacheza ndi Yosefe.
I izljubi svu braæu svoju i isplaka se nad njima. Potom se braæa njegova razgovarahu s njim.
16 Akunyumba kwa Farao atamva kuti abale ake a Yosefe abwera, Farao pamodzi ndi nduna zake zonse anakondwera.
I èu se glas u kuæi Faraonovoj, i rekoše: doðoše braæa Josifu. I milo bi Faraonu i slugama njegovijem;
17 Farao anati kwa Yosefe, “Uwawuze abale ako kuti, ‘Senzetsani nyama zanu katundu ndi kubwerera ku dziko la Kanaani.
I reèe Faraon Josifu: kaži braæi svojoj: ovako uèinite: natovarite magarce svoje, pa idite i vratite se u zemlju Hanansku,
18 Mukabwere nawo abambo anu ndi mabanja anu kuno, ndipo ine ndidzakupatsani dera lachonde kwambiri mʼdziko la Igupto. Mudzadya zokoma za mʼdzikoli.’”
Pa uzmite oca svojega i èeljad svoju, i doðite k meni, i daæu vam najbolje što ima u zemlji Misirskoj, i ješæete najbolje obilje ove zemlje.
19 “Uwawuzenso kuti, ‘Tengani ngolo zingapo za kuno ku Igupto kuti mukakwezepo ana anu, akazi anu pamodzi ndi abambo ako ndi kubwera nawo kuno.
A ti im zapovjedi: ovako uèinite: uzmite sa sobom iz zemlje Misirske kola za djecu svoju i za žene svoje, i povezite oca svojega i doðite ovamo;
20 Musadandaule zosiya katundu komweko chifukwa dziko lachonde la kuno ku Igupto lidzakhala lanu.’”
A na pokuæstvo svoje ne gledajte, jer što ima najbolje u svoj zemlji Misirskoj vaše je.
21 Choncho ana a Israeli anachita zimenezo. Yosefe anawapatsa ngolo monga Farao analamulira, ndipo anawapatsanso chakudya cha paulendo wawo.
I sinovi Izrailjevi uèiniše tako; i Josif im dade kola po zapovijesti Faraonovoj; dade im i brašnjenice na put.
22 Anaperekanso kwa aliyense zovala zatsopano, koma kwa Benjamini anapereka siliva wolemera pafupifupi makilogalamu anayi ndi zovala zisanu.
I svakome dade po dvoje haljine, a Venijaminu dade trista srebrnika i petore haljine.
23 Ndipo abambo ake anawatumizira izi: abulu khumi osenza zinthu zabwino kwambiri za ku Igupto, ndi abulu aakazi khumi osenza tirigu, buledi ndi zakudya zina za pa ulendo wake.
A ocu svojemu posla još deset magaraca natovarenijeh najljepšijeh stvari što ima u Misiru, i deset magarica natovarenijeh žita i hljeba i jestiva ocu na put.
24 Kenaka anawalola abale ake aja kuti azipita, ndipo akunyamuka, iye anawawuza kuti, “Osakangana mʼnjira!”
Tako opravi braæu svoju, i poðoše; i reèe im: nemojte se koriti putem.
25 Ndipo anachoka ku Igupto nafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani.
Tako se vratiše iz Misira, i doðoše u zemlju Hanansku k Jakovu ocu svojemu.
26 Iwo anawuza abambo awo kuti, “Yosefe akanali ndi moyo! Ndiponsotu, ndiye akulamulira dziko la Igupto.” Yakobo anangoti kakasi osankhulupirira.
I javiše mu i rekoše: još je živ Josif, i zapovjeda nad svom zemljom Misirskom. A u njemu srce prenemože, jer im ne vjerovaše.
27 Komabe atamufotokozera zonse zimene Yosefe anawawuza ndipo ataona ngolo zimene Yosefe anatumiza kuti adzakweremo popita ku Igupto, mtima wa Yakobo, abambo awo unatsitsimuka.
Ali kad mu kazaše sve rijeèi Josifove, koje im je Josif rekao, i vidje kola, koja posla Josif po oca, tada oživje duh Jakova oca njihova;
28 Ndipo Israeli anati, “Ndatsimikizadi! Mwana wanga Yosefe akanali ndi moyodi. Ndipita ndikamuone ndisanafe.”
I reèe Izrailj: dosta mi je kad je još živ sin moj Josif; idem da ga vidim dokle nijesam umro.

< Genesis 45 >