< Genesis 44 >

1 Pambuyo pake Yosefe analamulira wantchito wa mʼnyumba mwake kuti, “Adzazire chakudya anthuwa mʼmatumba mwawo monga mmene anganyamulire, ndipo uwayikire ndalama zawo pakamwa pa matumba awowo.
I zapovjedi Josif èovjeku što upravljaše kuæom njegovom govoreæi: naspi ovijem ljudima u vreæe žita koliko mogu ponijeti, i svakome u vreæu metni ozgo novce njegove.
2 Tsono uyike chikho changa cha siliva chija, pakamwa pa thumba la wamngʼono kwambiriyu pamodzi ndi ndalama zake za chakudya” Ndipo iye anachita monga Yosefe ananenera.
I èašu moju, èašu srebrnu, metni najmlaðemu u vreæu ozgo i novce za njegovo žito. I uèini kako mu Josif reèe.
3 Mmawa kutacha anthu aja analoledwa kuti apite ndi abulu awo.
A ujutru kad svanu, otpustiše ljude s magarcima njihovijem.
4 Atangotuluka mu mzinda muja, koma asanapite patali, Yosefe anati kwa wantchito wake, “Nyamuka atsatire anthu aja msanga. Ndipo ukawapeza, uwafunse kuti, ‘Bwanji mwabwezera zoyipa ndi zabwino?
A kad izaðoše iz mjesta i još ne bijahu daleko, reèe Josif èovjeku što upravljaše kuæom njegovom: ustani, idi brže za onijem ljudima, i kad ih stigneš reci im: zašto vraæate zlo za dobro?
5 Mwaberanji chikho chimene mbuye wanga amamweramo ndi kugwiritsa ntchito akafuna kuwombeza? Chimene mwachitachi ndi chinthu choyipa.’”
Nije li to èaša iz koje pije moj gospodar? i neæe li po njoj zacijelo poznati kakvi ste? zlo ste radili što ste to uèinili.
6 Wantchito uja atawapeza ananena mawu anawuzidwa aja.
I on ih stiže, i reèe im tako.
7 Koma iwo anati kwa iye, “Kodi mbuye wanga mukuneneranji zimenezi? Sizingatheke ndi pangʼono pomwe kuti antchito anufe nʼkuchita zoterozo ayi!
A oni mu rekoše: zašto govoriš, gospodaru, take rijeèi? Saèuvaj Bože da sluge tvoje uèine tako što!
8 Paja ife pobwera kuchokera ku Kanaani tinatenga ndalama kubwezera zimene tinazipeza mʼmatumba mwathu. Ndiye pali chifukwa chanji kuti tikabe siliva kapena golide mʼnyumba mwa mbuye wanu?
Eno smo ti donijeli natrag iz zemlje Hananske novce koje naðosmo ozgo u vreæama svojim, pa kako bismo ukrali iz kuæe gospodara tvojega srebro ili zlato?
9 Ngati wantchito wanu wina pano atapezeka nacho chikhocho, ameneyo aphedwe ndipo ena tonsefe tidzakhala akapolo anu, mbuye wathu.”
U kojega se izmeðu sluga tvojih naðe, onaj neka pogine, i svrh toga mi æemo biti robovi gospodaru mojemu.
10 Iye anati, “Chabwino, tsono zikhale monga mwaneneramu. Komatu aliyense amene angapezeke nacho chikhocho adzakhala kapolo wanga, ndipo ena nonsenu muzipita mwaufulu.”
A on reèe: neka bude kako rekoste; ali u koga se naðe, onaj da mi bude rob, a vi ostali neæete biti krivi.
11 Tsono onse anafulumira kutsitsa pansi aliyense thumba lake ndi kulitsekula.
I brže poskidaše svi na zemlju vreæe svoje, i razdriješiše svaki svoju vreæu.
12 Kenaka anayamba kufufuza, kuyambira pa wamkulu mpaka pa wamngʼono. Ndipo chikhocho chinapezeka mʼthumba mwa Benjamini.
A on stade tražiti poèev od najstarijega, i kad doðe na najmlaðega, naðe se èaša u vreæi Venijaminovoj.
13 Apo onse anangʼamba zovala zawo ndi chisoni. Ndipo anasenzetsa abulu katundu wawo nabwerera ku mzinda konkuja.
Tada razdriješe haljine svoje, i natovarivši svaki svoj tovar na svojega magarca vratiše se u grad.
14 Pamene Yuda ndi abale ake ankafika ku nyumba kwa Yosefe nʼkuti Yosefe akanali komweko. Ndipo anadzigwetsa pansi pamaso pake.
I doðe Juda s braæom svojom Josifu u kuæu, dok on još bijaše kod kuæe, i padoše pred njim na zemlju.
15 Yosefe anafunsa kuti, “Nʼchiyani mwachitachi? Kodi simudziwa kuti munthu ngati ine ndikhoza kuona zinthu mwakuwombeza?”
A Josif im reèe: šta ste to uèinili? zar nijeste znali da èovjek kao što sam ja može zacijelo doznati?
16 Yuda anayankha, “Kodi tinganenenji kwa mbuye wanga? Tinena chiyani? Tingadzilungamitse bwanji? Mulungu waulula kulakwa kwa antchito anu. Ndipo tsopano ndife akapolo a mbuye wanga, ife tonse pamodzi ndi amene wapezeka ndi chikhocho.”
Tada reèe Juda: šta da ti reèemo, gospodaru? šta da govorimo? kako li da se pravdamo? Bog je otkrio zloèinstvo tvojih sluga. Evo, mi smo svi robovi tvoji, gospodaru, i mi i ovaj u koga se našla èaša.
17 Koma Yosefe anati, “Sindingachite choncho ayi! Yekhayo amene wapezeka ndi chikhocho ndi amene akhale kapolo wanga. Ena nonsenu, bwererani kwa abambo anu mu mtendere.”
A Josif reèe: Bože saèuvaj! neæu ja to; u koga se našla èaša on neka mi bude rob, a vi idite s mirom ocu svojemu.
18 Ndipo Yuda anamuyandikira iye nati, “Chonde mbuye wanga mulole kapolo wanune ndinene mawu pangʼono kwa mbuye wanga. Musandipsere mtima, kapolo wanune, popeza inu muli ngati Farao yemwe.
Ali Juda pristupiv k njemu reèe: èuj me, gospodaru; dopusti da progovori sluga tvoj gospodaru svojemu, i neka se gnjev tvoj ne raspali na slugu tvojega, jer si ti kao sam Faraon.
19 Mbuye wanga munafunsa akapolo anufe kuti, ‘Kodi muli ndi abambo anu kapena mʼbale wanu?’
Gospodar moj zapita sluge svoje govoreæi: imate li oca ili brata?
20 Ndipo ife tinayankha, ‘Inde mbuye wathu, ife tili ndi abambo athu wokalamba, ndipo pali mwana wamwamuna wamngʼono amene anabadwa abambo athu atakalamba kale. Mʼbale wake anafa ndipo ndi yekhayo mʼmimba mwa amayi ake amene watsala ndipo abambo ake amamukonda.’
A mi rekosmo gospodaru svojemu: imamo stara oca i brata najmlaðega, koji mu se rodi u starosti; a njegov je brat umro, i on osta sam od matere svoje, i otac ga pazi.
21 “Ndipo inu munatiwuza kuti, ‘Mubwere naye kwa ine kuti ndidzamuone ndekha.’
A ti reèe slugama svojim: dovedite mi ga da ga vidim svojim oèima.
22 Ife tinati, ‘Mbuye wathu, mnyamatayo sangasiye abambo ake, akawasiya ndiye kuti abambo akewo adzafa.’
I rekosmo gospodaru svojemu: neæe moæi dijete ostaviti oca svojega; da ostavi oca svojega, odmah æe otac umrijeti.
23 Koma inu munatichenjeza kuti, ‘Pokhapokha mutabwera naye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri, simudzandionanso.’
A ti reèe slugama svojim: ako ne doðe s vama brat vaš najmlaði, neæete više vidjeti lica mojega.
24 Ndiye pamene tinafika kwa kapolo wanu, abambo athu tinawawuza zonse zimene munanena.
A kad se vratismo k sluzi tvojemu a ocu mojemu, kazasmo mu rijeèi gospodara mojega.
25 “Abambo athu anatiwuza kuti, ‘Pitaninso mukagule kachakudya pangʼono.’
Poslije reèe nam otac: idite opet, kupite nam hrane.
26 Koma tinati, ‘Sitingathe kupitanso. Sitingapite pokhapokha mngʼono wathuyu apite nafe chifukwa munthu uja anati sitingaonane naye ngati mngʼono wathuyu sakhala nafe.’
A mi rekosmo: ne možemo iæi, osim ako bude brat naš najmlaði s nama, onda æemo iæi, jer ne možemo vidjeti lica onoga èovjeka, ako ne bude s nama brat naš najmlaði.
27 “Koma kapolo wanu, abambo athu anatiwuza kuti, ‘Inu mukudziwa kuti mkazi wanga anandiberekera ana aamuna awiri.
A sluga tvoj, otac moj, reèe nam: znate da mi je žena rodila dva sina.
28 Mmodzi wa iwo anandisiya. Ine ndimati anadyedwa ndi chirombo popeza sindinamuonenso mpaka lero.
I jedan od njih otide od mene, i rekoh: zacijelo ga je raskinula zvjerka; i do sada ga ne vidjeh.
29 Tsopano mukanditengeranso uyu, nakaphedwa mu njira ndiye kuti mudzandikankhira ku manda ndi chisoni.’ (Sheol h7585)
Ako i ovoga odvedete od mene i zadesi ga kakvo zlo, svaliæete me stara u grob s tugom. (Sheol h7585)
30 “Tsono ngati tizibwerera kwa mtumiki wanu, abambo athu popanda mnyamatayu, amene moyo wa abambo ake uli pa iyeyu,
Pa sada da otidem k sluzi tvojemu, ocu svojemu, a ovo dijete da ne bude s nama, kako je duša onoga vezana za dušu ovoga,
31 ndipo akakaona kuti mnyamatayu palibe, basi akafa. Ife tidzakhala ngati takankhira abambo athu ku manda ndi chisoni. (Sheol h7585)
Umrijeæe kad vidi da nema djeteta, te æe sluge tvoje svaliti staroga slugu tvojega a oca svojega s tugom u grob. (Sheol h7585)
32 Ndiponsotu ine ndinadzipereka kwa abambo anga kukhala chikole chotsimikiza kuti mnyamatayu ndidzamuteteza, ndipo ndinati, ‘Ngati sindibwerera naye mnyamatayu kwa inu, ndiye kuti ndidzakhala wochimwira inu abambo anga moyo wanga wonse.’
A tvoj se sluga podjemèio za dijete ocu svojemu rekav: ako ti ga ne dovedem natrag, da sam kriv ocu svojemu dovijeka.
33 “Tsono, chonde mulole kuti ine kapolo wanu nditsalire kuno kukhala kapolo wa mbuye wathu mʼmalo mwa mnyamatayu. Koma iye apite pamodzi ndi abale akewa.
Zato neka sluga tvoj ostane mjesto djeteta da bude rob gospodaru mojemu a dijete neka ide s braæom svojom.
34 Ndingabwerere bwanji kwa abambo anga ngati sindingapite ndi mnyamatayu? Ayi! Sindifuna kukaona tsoka limene lingakagwere abambo anga.”
Jer kako bih se vratio k ocu svojemu bez djeteta, da gledam jade koji bi mi oca zadesili?

< Genesis 44 >