< Genesis 28 >

1 Choncho Isake anayitanitsa Yakobo namudalitsa nʼkumuwuzitsa kuti, “Usakwatire mkazi wa kuno ku Kanaani.
And so Isaac clepide Jacob, and blesside hym, and comaundide to hym, and seide, Nyle thou take a wijf of the kyn of Canaan; but go thou,
2 Panopo upite ku Padanaramu, ku nyumba kwa Betueli abambo a amayi akowa, kumeneko ukakwatire mmodzi mwa ana aakazi a Labani, mlongo wa amayi akowa.
and walke forth in to Mesopotanye of Sirie, to the hows of Batuel, fadir of thi modir, and take to thee of thennus a wijf of the douytris of Laban, thin vncle.
3 Mulungu Wamphamvuzonse akudalitse iwe nakupatse ana ambiri mpaka udzasanduke gulu lalikulu la mitundu ya anthu.
Sotheli Almyyti God blesse thee, and make thee to encreesse, and multiplie thee, that thou be in to cumpanyes of puplis;
4 Mulunguyo akudalitse iwe monga mmene anamudalitsira Abrahamu kuti zidzukulu zako zidzalandira dziko limene ukukhalamo ngati mlendo kuti lidzakhale lawo. Ili ndi dziko limene Mulungu anapereka kwa Abrahamu.”
and God yyue to thee the blessyngis of Abraham, and to thi seed aftir thee, that thou welde the lond of thi pilgrymage, which he bihiyte to thi grauntsir.
5 Ndipo Isake anamulola Yakobo kuti anyamuke kupita ku Padanaramu kwa Labani mwana wa Betueli Mwaramu. Labani anali mlongo wa Rebeka, mayi wa Yakobo ndi Esau.
And whanne Ysaac hadde left hym, he yede forth, and cam in to Mesopotanye of Sirie, to Laban, the sone of Batuel of Sirie, the brother of Rebecca, his modir.
6 Tsopano Esau anadziwa kuti Isake anadalitsa Yakobo ndi kumutumiza ku Padanaramu kuti akakwatire kumeneko. Anawuzidwanso kuti, “Usakwatire mkazi wa ku Kanaani.”
Forsothe Esau seiy that his fadir hadde blessid Jacob, and hadde sent him in to Mesopotanye of Sirie, that he schulde wedde a wijf of thennus, and that aftir the blessyng he comaundide to Jacob, and seide, Thou schalt not take a wijf of the douytris of Canaan;
7 Yakobo anamvera abambo ake ndi amayi ake ndi kupita ku Padanaramu.
and that Jacob obeiede to his fadir `and modir, and yede in to Sirie;
8 Ndiye pamenepo Esau anazindikira kuti abambo ake Isake sankakondwera ndi akazi a ku Kanaani;
also Esau preuyde that his fadir bihelde not gladli the douytris of Canaan.
9 anapita kwa Ismaeli mwana wa Abrahamu nakwatira Mahalati mwana wa Ismaeli, mlongo wake wa Nebayoti. Anatero kuwonjezera akazi amene anali nawo kale.
And he yede to Ismael, and weddide a wijf, with out these whiche he hadde bifore, Melech, the douyter of Ismael, sone of Abraham, the sistir of Nabaioth.
10 Yakobo ananyamuka pa ulendo kuchoka ku Beeriseba kupita ku Harani.
Therfor Jacob yede out of Bersabee, and yede to Aran.
11 Atafika pa malo pena, anayima kuti agonepo chifukwa dzuwa linali litalowa. Anatenga mwala wina pomwepo natsamiritsapo mutu wake, ndipo anagona.
And whanne he hadde come to sum place, and wolde reste ther inne aftir the goynge doun of the sunne, he took of the stoonus that laien ther, and he puttide vndur his heed, and slepte in the same place.
12 Mʼmaloto, anaona makwerero oyimikidwa pansi ndipo anakafika kumwamba. Angelo a Mulungu amakwera ndi kutsika pa makwereropo.
And he seiye in sleep a laddir stondynge on the erthe, and the cop ther of touchinge heuene; and he seiy Goddis aungels stiynge vp and goynge doun ther bi,
13 Tsono Yehova anayimirira pambali pake, nati, “Ine ndine Yehova, Mulungu wa Abrahamu kholo lake la Isake abambo ako. Ndidzakupatsa iwe ndi zidzukulu zako dziko limene ukugonamolo.
and the Lord fastned to the laddir, seiynge to hym, Y am the Lord God of Abraham, thi fadir, and God of Isaac; Y schal yyue to thee and to thi seed the lond in which thou slepist.
14 Zidzukulu zako zidzachuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi ndipo zidzabalalikira kumadzulo ndi kummawa, kumpoto ndi kummwera. Anthu onse adzalandira madalitso kudzera mwa iwe ndi zidzukulu zako.
And thi seed schal be as the dust of erthe, thou schalt be alargid to the eest, and west, and north, and south; and alle lynagis of erthe schulen be blessid in thee and in thi seed.
15 Ine ndili nawe pamodzi ndipo ndidzakuyangʼanira kulikonse upiteko, ndipo ndidzakubwezera ku dziko lino. Sindidzakusiya mpaka nditachita zimene ndakulonjezazi.”
And Y schal be thi kepere, whidur euer thou schalt go; and Y schal lede thee ayen in to this lond, and Y schal not leeue no but Y schal fil alle thingis whiche Y seide.
16 Yakobo atadzidzimuka, anati, “Zoonadi Yehova ali pa malo ano, ndipo ine sindinadziwe.”
And whanne Jacob hadde wakyd of sleep, he seide, Verili the Lord is in this place, and Y wiste not.
17 Tsono anachita mantha ndipo anati, “Malo ano ndi woopsa ndithu. Zoonadi pano ndi pa nyumba ya Mulungu ndi khomo la kumwamba.”
And he seide dredynge, Hou worschipful is this place! Here is noon other thing no but the hows of God, and the yate of heuene.
18 Mmamawa mwake Yakobo anatenga mwala umene anatsamira mutu wake uja nawuyimika ngati chipilala ndi kuthira mafuta pamwamba pake
Therfor Jacob roos eerli, and took the stoon which he hadde put vndur his heed, and reiside in to a title, and helde oile aboue.
19 Iye anawatcha malowo Beteli, ngakhale kuti poyamba mzindawo ankawutcha Luzi.
And he clepide the name of that citee Bethel, which was clepid Lusa bifore.
20 Pamenepo Yakobo analumbira kwa Yehova nati, “Ngati inu Mulungu mukhala ndi ine, kundiyangʼanira pa ulendo wangawu ndi kundipatsa chakudya ndi chovala;
Also he auowide a vow, and seide, If God is with me, and kepith me in the weie in which Y go, and yyueth to me looues to ete, and clothis to be clothid,
21 ngati inu mudzandibweretsa kwathu mu mtendere, ndiye kuti mudzakhala Mulungu wanga,
and Y turne ayen in prosperite to the hows of my fadir, the Lord schal be in to God to me.
22 ndipo mwala uwu ndawuyimikawu udzakhala Nyumba ya Mulungu. Ine ndidzakupatsani chakhumi cha zinthu zonse zimene mudzandipatse.”
And this stoon, which Y reiside in to a title, schal be clepid the hows of God, and Y schal offre tithis to thee of alle thingis whiche thou schalt yyue to me.

< Genesis 28 >