< Genesis 21 >

1 Yehova anakomera mtima Sara monga ananenera, ndipo Yehovayo anachita monga momwe analonjezera.
I Gospod pohodi Saru, kao što bješe rekao, i uèini Gospod Sari kao što bješe kazao.
2 Sara anakhala ndi pathupi ndipo anamuberekera Abrahamu mwana wamwamuna mu ukalamba wake, pa nyengo imene Mulungu anamulonjeza.
Jer zatrudnje i rodi Sara Avramu sina u starosti njegovoj u isto vrijeme kad kaza Gospod.
3 Abrahamu anapereka dzina loti Isake kwa mwana wamwamuna amene Sara anamuberekera.
I Avram nadjede ime sinu koji mu se rodi, kojega mu rodi Sara, Isak.
4 Isake atakwanitsa masiku asanu ndi atatu, Abrahamu anamuchita mdulidwe monga Mulungu anamulamulira.
I obreza Avram sina svojega Isaka kad bi od osam dana, kao što mu zapovjedi Bog.
5 Abrahamu anali ndi 100 pamene mwana wake Isake anabadwa.
A Avramu bješe sto godina kad mu se rodi sin Isak.
6 Sara anati, “Mulungu wandibweretsera mseko, ndipo aliyense amene adzamva zimenezi adzaseka nane pamodzi.”
A Sara reèe: Bog mi uèini smijeh; ko god èuje, smijaæe mi se.
7 Ndipo anawonjezera kuti, “Ndani akanamuwuza Abrahamu kuti Sara nʼkudzayamwitsako ana? Chonsecho ndamubalira mwana wamwamuna kuwukalamba wake.”
I reèe: ko bi rekao Avramu da æe Sara dojiti djecu? ipak mu rodih sina u starosti njegovoj.
8 Mwana uja anakula mpaka kumuletsa kuyamwa. Tsiku lomuletsa Isake kuyamwa, Abrahamu anakonza phwando lalikulu.
A kad dijete doraste da se odbije od sise, uèini Avram veliku gozbu onaj dan kad odbiše Isaka od sise.
9 Koma Sara anaona kuti mwana wamwamuna amene Hagara Mwigupto anamuberekera Abrahamu amamuseka,
I Sara vidje sina Agare Misirke, koja ga rodi Avramu, gdje se potsmijeva;
10 ndipo anati kwa Abrahamu, “Muchotse mdzakazi ndi mwana wake wamwamunayu, pakuti mwana wa kapolo sadzagawana chuma ndi mwana wanga Isake.”
Pa reèe Avramu: otjeraj ovu robinju sa sinom njezinijem, jer sin ove robinje neæe biti našljednik s mojim sinom, s Isakom.
11 Nkhaniyi inamumvetsa chisoni kwambiri Abrahamu chifukwa imakhudza mwana wake.
A to Avramu bi vrlo krivo radi sina njegova.
12 Koma Mulungu anamuwuza Abrahamu kuti, “Usamve chisoni motero ndi mnyamatayu ndi mdzakazi wakoyu. Mvetsera chilichonse chomwe Sara akukuwuza, chifukwa zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake.
Ali Bog reèe Avramu: nemoj da ti je krivo radi djeteta i radi robinje tvoje. Što ti je god kazala Sara, poslušaj; jer æe ti se u Isaku sjeme prozvati.
13 Mwana wa mdzakazi wakoyu ndidzamusandutsa mtundu wa anthu chifukwa ndi mwana wako.”
Ali æu i od sina robinjina uèiniti narod, jer je tvoje sjeme.
14 Mmamawa wake, Abrahamu anatenga chakudya ndi botolo la madzi nazipereka kwa Hagara. Anasenzetsa Hagara nawaperekeza pangʼono ndi mnyamatayo. Hagara ananyamuka nayendayenda mʼchipululu cha Beeriseba.
I Avram ustav ujutru rano, uze hljeba i mješinu vode, i dade Agari metnuvši joj na leða, i dijete, i otpusti je. A ona otišavši lutaše po pustinji Virsavskoj.
15 Madzi atatha mʼbotolo muja, anamuyika mnyamatayo pansi pa zitsamba.
A kad nesta vode u mješini, ona baci dijete pod jedno drvo,
16 Kenaka Hagara anachoka nakakhala pansi cha pakatalipo, pafupifupi mamita makumi asanu ndi anayi, popeza mʼmaganizo mwake amati, “Sindingaonerere mwanayu akufa.” Ndipo anakhala pansi cha poteropo nʼkumalira.
Pa otide koliko se može strijelom dobaciti, i sjede prema njemu; jer govoraše: da ne gledam kako æe umrijeti dijete. I sjedeæi prema njemu stade iza glasa plakati.
17 Mulungu anamva mnyamatayo akulira ndipo mngelo wa Mulungu anayankhula kwa Hagara kuchokera kumwamba nati, “Chavuta nʼchiyani Hagara? Usachite mantha; Mulungu wamva kulira kwa mnyamatayo pamene wagonapo.
A Bog èu glas djetinji, i anðeo Božji viknu s neba Agaru, i reèe joj: što ti je, Agaro? ne boj se, jer Bog èu glas djetinji odande gdje je.
18 Munyamule mnyamatayo ndipo umugwire dzanja pakuti ndidzamupanga kukhala mtundu waukulu.”
Ustani, digni dijete i uzmi ga u naruèje; jer æu od njega uèiniti velik narod.
19 Kenaka Mulungu anatsekula maso a Hagara ndipo anaona chitsime cha madzi. Choncho anapita nadzaza botolo lija ndi madzi ndi kumupatsa mnyamatayo kuti amwe.
I Bog joj otvori oèi, te ugleda studenac; i otišavši napuni mješinu vode, i napoji dijete.
20 Mulungu anali ndi mnyamatayo pamene ankakula. Anakhala ku chipululu nakhala katswiri wolasa uta.
I Bog bijaše s djetetom, te odraste, i življaše u pustinji, i posta strijelac.
21 Akukhala ku chipululu cha Parani, mayi ake anamupezera mkazi wochokera ku Igupto.
A življaše u pustinji Faranu. I mati ga oženi iz zemlje Misirske.
22 Pa nthawiyo, Abimeleki ndi Fikolo wamkulu wankhondo wake anati kwa Abrahamu, “Mulungu ali nawe pa chilichonse umachita.
U to vrijeme reèe Avimeleh i Fihol vojvoda njegov Avramu govoreæi: Bog je s tobom u svemu što radiš.
23 Tsopano undilumbirire ine pano pamaso pa Mulungu kuti sudzachita mwa chinyengo ndi ine kapena ana anga kapena zidzukulu zanga. Undionetse ine pamodzi ndi dziko limene ukukhalamo ngati mlendo, kukoma mtima kokhala ngati kumene ndinakuonetsa ine.”
Zakuni mi se sada Bogom da neæeš prevariti mene ni sina mojega ni unuka mojega, nego da æeš dobro onako kako sam ja tebi èinio i ti èiniti meni i zemlji u kojoj si došljak.
24 Abrahamu anati, “Ine ndikulumbira.”
A Avram reèe: hoæu se zakleti.
25 Kenaka Abrahamu anadandaula kwa Abimeleki pa za chitsime chimene antchito a Abimeleki analanda.
Ali Avram prekori Avimeleha za studenac, koji uzeše na silu sluge Avimelehove.
26 Koma Abimeleki anati, “Ine sindikudziwa amene anachita zimenezi. Iwe sunandiwuze, ndipo ndazimva lero zimenezi.”
A Avimeleh reèe: ne znam ko je to uèinio; niti mi ti kaza, niti èuh do danas.
27 Choncho Abrahamu anabweretsa nkhosa ndi ngʼombe nazipereka kwa Abimeleki, ndipo anthu awiriwo anachita pangano.
Tada Avram uze ovaca i goveda, i dade Avimelehu, i uhvatiše vjeru meðu sobom.
28 Abrahamu anapatulako ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri kuchoka pagulu la nkhosa zina,
I Avram odluèi sedam jaganjaca iz stada.
29 ndipo Abimeleki anafunsa Abrahamu, “Kodi tanthauzo lake la ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri amene wawapatula pawokhawa nʼchiyani?”
A Avimeleh reèe Avramu: šta æe ono sedam jaganjaca što si odluèio?
30 Iye anayankha kuti, “Landirani ana ankhosa aakazi kuchokera mʼdzanja langa ngati umboni kuti ndinakumba chitsime ichi.”
A on odgovori: da primiš iz moje ruke ono sedam jaganjaca, da mi bude svjedoèanstvo da sam ja iskopao ovaj studenac.
31 Kotero malo amenewo anatchedwa Beeriseba, chifukwa anthu awiriwo analumbirirapo malumbiro.
Otuda se prozva ono mjesto Vir-Saveja, jer se ondje zakleše obojica.
32 Atatha kuchita pangano pa Beeriseba, Abimeleki ndi Fikolo mkulu wankhondo wake anabwerera ku dziko la Afilisti.
Tako uhvatiše vjeru na Virsaveji. Tada se diže Avimeleh i Fihol vojvoda njegov, i vratiše se u zemlju Filistejsku.
33 Abrahamu anadzala mtengo wa bwemba ku Beeriseba, ndipo anapemphera pamenepo mʼdzina la Yehova, Mulungu Wamuyaya.
A Avram posadi lug na Virsaveji, i ondje prizva ime Gospoda Boga vjeènoga.
34 Ndipo Abrahamu anakhala mʼdziko la Afilisti kwa nthawi yayitali.
I Avram življaše kao došljak u zemlji Filistejskoj mnogo vremena.

< Genesis 21 >