< Ezara 4 >

1 Adani a Yuda ndi Benjamini anamva kuti anthu obwera ku ukapolo aja akumangira Nyumba Yehova, Mulungu wa Israeli.
A kad èuše neprijatelji Judini i Venijaminovi da oni koji se vratiše iz ropstva zidaju crkvu Gospodu Bogu Izrailjevu,
2 Tsono anapita kwa Zerubabeli ndi kwa atsogoleri a mabanja awo ndi kunena kuti, “Mutilole kuti tikuthandizeni kumangaku chifukwa ife timapembedza Mulungu wanu monga momwe mumachitira inu, ndipo takhala tikupereka nsembe kwa Iye kuyambira nthawi ya Esrahadoni, mfumu ya ku Asiriya, amene anabwera nafe kuno.”
Doðoše k Zorovavelju i ka glavarima domova otaèkih, i rekoše im: da i mi zidamo s vama, jer æemo kao i vi tražiti Boga vašega, i njemu prinosimo žrtve od vremena Esaradona cara Asirskoga, koji nas je doveo ovamo.
3 Koma Zerubabeli, Yesuwa ndi atsogoleri ena otsala a mabanja a Aisraeli anayankha kuti, “Inu simungatithandize kumangira Nyumba Yehova, Mulungu wathu. Tokha tidzamumangira Nyumba Yehova, Mulungu wa Aisraeli, monga mfumu Koresi, mfumu ya Perisiya inatilamulira.”
A Zorovavelj i Isus i ostali glavari domova otaèkih u Izrailju rekoše im: ne možete vi s nama zidati doma Bogu našemu, nego æemo mi sami zidati Gospodu Bogu Izrailjevu, kako nam je zapovjedio Kir car Persijski.
4 Tsono anthu a mʼdzikomo anayamba kuchititsa ulesi anthu a ku Yuda, ndi kuwachititsa mantha kuti aleke ntchito yomangayo.
Tada narod zemaljski dosaðivaše narodu Judinu i smetaše ih u zidanju;
5 Analemba alangizi ena kuti alepheretse cholinga chawo pa ntchitoyo pa nthawi yonse ya Koresi, mfumu ya ku Perisiya, ndiponso mpaka pamene Dariyo mfumu ya ku Perisiya ankalamulira dzikolo.
I naimahu savjetnike suprot njima da rasipaju namjeru njihovu svega vremena Kira cara Persijskoga do vlade Darija cara Persijskoga.
6 Mfumu Ahasiwero atangoyamba kulamulira dzikolo, adani aja analemba kalata yoneneza anthu a Yuda ndi Yerusalemu.
A kad se zacari Asvir, u poèetku njegova carovanja napisaše tužbu na stanovnike Judejske i Jerusalimske.
7 Ndiponso mʼnthawi ya Aritasasita mfumu ya Perisiya, Bisilamu, Mitiredati, Tabeeli ndi anzawo ena analemba kalata inanso kwa Aritasasita. Kalatayo inalembedwa mʼChiaramu ndipo ankatanthauzira poyiwerenga.
I za vremena Artakserksova pisa Vislam, Mitredat, Taveilo i ostali drugovi njegovi Artakserksu caru Persijskom; a knjiga bješe pisana Sirskim pismom i Sirskim jezikom.
8 Rehumu mkulu wankhondo ndi Simisai mlembi, nawonso analemba kalata yawo yoneneza anthu a ku Yerusalemu kwa mfumu Aritasasita. Anayilemba motere:
Reum starješina u vijeæu i Simsaj pisar napisaše jednu knjigu protiv Jerusalima caru Artakserksu ovako:
9 Kalata yochokera kwa Rehumu, mkulu wa gulu lankhondo, mlembi Simisai ndi anzawo awa: oweruza, nduna, akuluakulu ena, anthu a ku Peresiya, Ereki, Babuloni, Susa mʼdziko la Elamu,
Reum starješina u vijeæu i Simsaj pisar i ostali drugovi njihovi, Dinjani, Afarsašani, Tarfaljani, Afaršani, Arhevljani, Vavilonjani, Susanašani, Deavljani, Elamljani,
10 ndi mitundu ina imene mkulu wolemekezeka, Osanipara anayisamutsa ndi kuyikhazika mʼmizinda ya Samariya ndi mʼmadera ena apatsidya la Yufurate.
I ostali narodi koje preseli veliki i slavni Asenafar i naseli po gradovima Samarijskim, i ostali s ove strane rijeke, tada i tada.
11 Mawu a mʼkalata ya kwa Aritasasita anali awa: Kwa mfumu Aritasasita: Kuchokera kwa atumiki anu, anthu a kutsidya kwa Yufurate:
Ovo je prijepis od knjige koju mu poslaše: Caru Artakserksu. Sluge tvoje, ljudi s ove strane rijeke, tada i tada.
12 Amfumu tati mudziwe kuti Ayuda amene anabwera kuno kuchokera kwanuko apita ku Yerusalemu ndipo akumanganso mzinda wa anthu owukira ndi oyipa uja. Akumaliza makoma ake ndipo akukonzanso maziko.
Da je na znanje caru da Judejci koji poðoše od tebe k nama, doðoše u Jerusalim, i grad odmetnièki i opaki zidaju, zidove opravljaju i iz temelja podižu.
13 Kuwonjeza apo amfumu mudziwe kuti ngati amalize kumanganso mzindawu ndi kukonzanso makoma ake, adzaleka kukhoma msonkho, kulipira ndalama zakatundu olowa mʼdziko kapena msonkho wina uliwonse, ndipo chuma cha thumba la ufumu chidzachepa.
Nego da je na znanje caru: ako se ovaj grad sazida i zidovi oprave, oni neæe davati danka ni poreze ni carine, te æe biti šteta riznici carskoj.
14 Popeza tsono ife timadya nawo kwa mfumu sitiyenera tizingoonerera zinthu zochititsa mfumu manyazi. Nʼchifukwa chake tikutumiza uthenga kwa inu a mfumu kuti mudziwe zonse.
Što dakle platu od dvora primamo, te nam ne prilièi da gledamo štetu carevu, toga radi šaljemo i javljamo caru,
15 Choncho pachitike kafukufuku mʼbuku la mbiri yakale ya makolo anu. Mʼbuku la mbiri zakale mudzapezamo ndi kuwerenga kuti mzinda umenewu ndi waupandu, wosautsa mafumu ndi nduna zamʼmadera zomwe. Kuyambira kale wakhala ukuwukira ulamuliro uliwonse. Nʼchifukwa chake mzinda umenewu anawuwononga.
Da se potraži u knjizi dnevnika otaca tvojih, pa æeš naæi u knjizi dnevnika i doznati da je ovaj grad odmetnièki i da je na štetu carevima i zemljama i da su se u njemu dizale bune od davnina, te zato bi raskopan ovaj grad.
16 Tsono tikukudziwitsani amfumu kuti ngati mzinda umenewu umangidwanso ndi makoma ake nʼkutsirizidwanso ndiye kuti inu simudzalamuliranso chigawo cha patsidya pa Yufurate.
Dajemo na znanje caru: ako se ovaj grad sazida i zidovi se njegovi oprave, onda ovaj dio preko rijeke neæe više biti tvoj.
17 Mfumu inatumiza yankho ili: Mkulu wa gulu lankhondo Rehumu, mlembi Simisai ndi anzanu onse amene akukhala ku Samariya ndi mʼzigawo zina zonse za Patsidya pa Yufurate. Landirani moni.
Tada car posla odgovor Reumu starješini u vijeæu i Simsaju pisaru i ostalijem drugovima njihovijem koji seðahu u Samariji i ostalijem s onu stranu rijeke: Pozdravlje, tada i tada.
18 Kalata imene munatumiza ija yawerengedwa bwino lomwe pamaso panga.
Knjiga koju nam poslaste razgovijetno bi proèitana preda mnom.
19 Ine nditalamula kuti afufuze nkhaniyi kwapezekadi kuti mzinda umenewu uli ndi mbiri yowukira mafumu ndi kuti zaupandu ndi zowukira zinkachitikadi mʼmenemo.
I zapovjedih te potražiše i naðoše da je taj grad od davnina ustajao na careve i da su u njemu bivali odmeti i bune,
20 Mafumu amphamvu akhala akulamulira Yerusalemu ndi chigawo chonse cha Patsidya pa Yufurate. Iwo ankalandira msonkho ndi kulipira ndalama zakatundu olowa mʼdziko pa kanthu kena kalikonse.
I da su silni carevi bivali u Jerusalimu, koji vladahu svijem što je preko rijeke, i davahu im se danci i poreze i carine.
21 Tsopano inu khazikitsani lamulo kuti anthu amenewo asiye ntchitoyo, asamangenso mzindawo mpaka ine nditalamula
Zato naredite da se zabrani onijem ljudima da se onaj grad ne zida dokle ja ne zapovjedim.
22 Musachedwe kuchita zimenezi. Kodi ine ndingalole bwanji kuti zowononga zotere zikule ndi kupweteka ine mfumu?
I pazite da ne pogriješite u tom. Jer zašto bi zlo raslo na štetu carevima?
23 Kalata ya mfumu Aritasasitayi itangowerengedwa pamaso pa Rehumu ndi Simisai mlembi uja, ndi anzawo onse, iwo anapita msangamsanga ku Yerusalemu kukawaletsa Ayuda aja mwamphamvu kuti asapitirire ntchito yawo.
A kad se prijepis od knjige cara Artakserksa proèita pred Reumom i Simsajem pisarem i pred drugovima njihovijem, oni brže otidoše u Jerusalim k Judejcima, te im zabraniše oružanom silom.
24 Motero ntchito yomanga Nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu inayimitsidwa mpaka chaka cha chiwiri cha ulamuliro wa Dariyo mfumu ya ku Perisiya.
Tada stade posao oko doma Božijega u Jerusalimu, i staja do druge godine carovanja Darija cara Persijskoga.

< Ezara 4 >