< Ezara 3 >

1 Utafika mwezi wa chisanu ndi chiwiri Aisraeli atakhala kale mʼmidzi yawo, anthu anasonkhana ku Yerusalemu ndi cholinga chimodzi.
A kad doðe sedmi mjesec i sinovi Izrailjevi bijahu u svojim gradovima, sabra se narod jednodušno u Jerusalim.
2 Kenaka Yesuwa mwana wa Yozadaki ndi ansembe anzake pamodzi ndi Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi abale ake anayamba kumanga guwa lansembe la Mulungu wa Israeli. Anatero pofuna kuti aziperekapo nsembe zopsereza monga analembera mʼbuku la Mose, munthu wa Mulungu uja.
Tada usta Isus sin Josedekov s braæom svojom sveštenicima i Zorovavelj sin Salatilov s braæom svojom, i zgradiše oltar Boga Izrailjeva da prinose na njemu žrtve paljenice kako piše u zakonu Mojsija èovjeka Božijega.
3 Ndi mantha ndi mantha chifukwa cha anthu a mʼmayikomo, iwo anamanga guwalo pa maziko ake akale, ndipo anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu pa guwapo mmawa ndi madzulo.
I podigoše oltar na mjestu njegovu, ako i bijahu u strahu od naroda zemaljskih; i prinosiše na njemu žrtve paljenice Gospodu, žrtve paljenice jutrom i veèerom;
4 Ankasunga tsiku la chikondwerero cha misasa monga momwe zinalembedwera. Ankaperekanso nsembe za tsiku ndi tsiku monga mwa chiwerengero chake potsata mwambo wake wa tsiku ndi tsiku monga zinalembedwa.
I praznovaše praznik sjenica, kako je pisano, prinoseæi žrtve paljenice svaki dan na broj kako je ureðeno za svaki dan.
5 Pambuyo pake, ankapereka nsembe zopsereza, nsembe zopereka pa nthawi ya mwezi watsopano ndi za pa masiku onse a chikondwerero oyikidwa kutamandira Yehova, kudzanso nsembe zaufulu zopereka kwa Yehova.
A potom prinosiše žrtvu paljenicu svagdašnju, i na mladine i na sve praznike Gospodnje osveæene i od svakoga koji dragovoljno prinošaše prinos Gospodu.
6 Kuyambira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, iwo anayambanso kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova, ngakhale kuti maziko a Nyumba ya Yehova anali asanamangidwe.
Od prvoga dana mjeseca sedmoga poèeše prinositi žrtve paljenice Gospodu, a dom Gospodnji još ne bješe osnovan.
7 Ndipo anapereka ndalama kwa amisiri a miyala ndi kwa amisiri a matabwa, ndi chakudya, chakumwa ndi mafuta kwa anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo, kuti abweretse mitengo ya mkungudza pa nyanja kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Yopa. Zonsezi anachita malinga ndi chilolezo chimene analandira kuchokera kwa Koresi, mfumu ya Peresiya.
I dadoše novce kamenarima i drvodjeljama, i hranu i piæe i ulje Sidonjanima i Tircima da dovoze drva kedrova s Livana u more Jopsko, kako im bješe dopustio Kir car Persijski.
8 Tsono mu chaka chachiwiri atabwera ku Yerusalemu, ku malo akale a Nyumba ya Yehova, mwezi wachiwiri Zerubabeli mwana wa Sealatieli, Yesuwa mwana wa Yozadaki pamodzi ndi abale awo onse, ansembe, Alevi ndi onse amene anabwera ku Yerusalemu kuchokera ku ukapolo, anayamba kugwira ntchito. Iwo anasankha Alevi a zaka zoyambira makumi awiri kuti aziyangʼanira ntchito ya kumanga Nyumba ya Yehova.
I druge godine po povratku njihovu k domu Božijemu u Jerusalim, drugoga mjeseca poèeše Zorovavelj sin Salatilov i Isus sin Josedekov i ostala braæa njihova, sveštenici i Leviti, i svi koji doðoše iz ropstva u Jerusalim, i postaviše Levite od dvadeset godina i više da nastoje nad poslom oko doma Gospodnjega.
9 Yesuwa ndi ana ake aamuna kudzanso abale ake, Kadimieli ndi ana ake (ana a Yuda) onse pamodzi anasenza udindo woyangʼanira antchito ku Nyumba ya Mulungu, kuphatikizanso ana a Henadadi komanso Alevi, ana awo ndi abale awo.
I bi postavljen Isus i sinovi njegovi i braæa njegova, i Kadmilo i sinovi njegovi, sinovi Judini, zajedno da nastoje nad poslenicima u domu Božijem, i sinovi Inadadovi i njihovi sinovi i braæa njihova Leviti.
10 Amisiri omanga nyumba atamanga maziko a Nyumba ya Yehova, ansembe anabwera akuyimba malipenga, atavala zovala zaunsembe. Ndipo Alevi, zidzukulu za Asafu, anadza akuyimba matambolini ndi kutenga udindo wawo wotamanda Yehova, potsata malangizo a Davide mfumu ya Aisraeli.
I kad zidari polagahu temelj crkvi Gospodnjoj, postaviše sveštenike obuèene s trubama i Levite sinove Asafove s kimvalima da hvale Gospoda po uredbi Davida cara Izrailjeva.
11 Iwo ankayimba motamanda ndi mothokoza Yehova nyimbo iyi: “Yehova ndi wabwino; chikondi chake pa Israeli ndi chamuyaya.” Ndipo anthu onse ankafuwula kwambiri kumutamanda Yehova, chifukwa maziko a Nyumba ya Yehova anali kumangidwa.
I pjevahu naizmjence hvaleæi i slaveæi Gospoda: jer je dovijeka milost njegova nad Izrailjem. I sav narod podvikivaše iza glasa hvaleæi Gospoda što se osnivaše dom Gospodnji.
12 Koma ambiri mwa ansembe, Alevi ndiponso atsogoleri amabanja, akuluakulu amene anaona Nyumba ya Yehova yakale, analira mokweza pamene anaona maziko a nyumbayi akumangidwa. Komanso ena ambiri ankafuwula mosangalala.
A mnogi od sveštenika i Levita i glavara domova otaèkih, starci koji bijahu vidjeli preðašnji dom, plakahu iza glasa gledajuæi ovaj dom koji se osnivaše, a mnogi opet podvikivahu od radosti,
13 Choncho panalibe amene ankatha kusiyanitsa liwu lofuwula mokondwerera ndi liwu la anthu olira, chifukwa anthuwo ankafuwula kwambiri. Ndipo liwu lofuwulalo limamveka kutali.
Te narod ne mogaše razaznati vike radosne od vike plaène u narodu, jer narod podvikivaše iza glasa, i vika se èujaše daleko.

< Ezara 3 >