< Ezekieli 45 >

1 “‘Mukamadzagawa dziko kuti fuko lililonse lilandire cholowa chake, mudzapatuleko chigawo chimodzi kuti chikhale cha Yehova. Mulitali mwake mudzakhale makilomita khumi ndi awiri ndi theka ndipo mulifupi mwake makilomita khumi. Malo onsewo adzakhale opatulika.
A kad stanete dijeliti zemlju u našljedstvo, prinesite prinos Gospodu, svet dio od zemlje, u dužinu dvadeset i pet tisuæa lakata, i u širinu deset tisuæa, to neka bude sveto po svijem meðama svojim unaokolo.
2 Mʼkati mwa chigawo chimenechi, malo a mamita 250 mbali iliyonse adzakhala malo a Nyumba ya Mulungu. Pozungulira pake ponse padzakhala malo a mamita 25.
Od toga neka bude za svetinju pet stotina lakata u dužinu i pet stotina u širinu, èetvrtasto otsvuda, i pedeset lakata unaokolo za podgraða.
3 Mʼchigawo chopatulikacho muyeze malo a makilomita 12 ndi theka mulitali mwake, makilomita asanu mulifupi mwake. Pamenepo padzakhala malo opatulika kwambiri.
Po toj mjeri izmjeri u dužinu dvadeset i pet tisuæa i u širinu deset tisuæa, i tu neka bude svetinja i svetinja nad svetinjama.
4 Malo opatulika amenewa adzakhalanso a ansembe amene amatumikira ku malo opatulika, amene amayandikira Yehova kuti amutumikire. Pamenepo padzakhala malo omangapo nyumba zawo ndi malo omangapo Nyumba ya Mulungu.
To neka bude svet dio od zemlje sveštenicima, koji služe u svetinji, koji pristupaju da služe Gospodu, i neka im bude mjesto za kuæe i sveto mjesto za svetinju.
5 Alevi otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzakhala ndi malo a makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake ndi makilomita asanu mulifupi mwake. Kumeneko ndiko kudzakhale midzi yawo.
A dvadeset i pet tisuæa lakata u dužinu i deset tisuæa u širinu neka bude Levitima koji služe u domu u državu s dvadeset klijeti.
6 “‘Moyandikana ndi malo opatulika, padzakhale malo a makilomita awiri ndi theka mulifupi mwake ndi makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake; kuti akhale malo a mzinda. Malo amenewa adzakhala a Aisraeli onse.
I gradu podajte dostojanje pet tisuæa lakata u širinu i dvadeset i pet tisuæa u dužinu prema svetom dijelu; to neka je za sav dom Izrailjev.
7 “‘Mfumu idzakhale ndi malo okhudzana ndi chigawo cha malo opatulika ndi cha mzinda. Malowo ayandikane ndi zigawozo chakummawa ndi chakumadzulo. Malowo atalike ngati chigawo chimodzi cha fuko la Israeli kuyambira ku malire akummawa mpaka ku malire akumadzulo.
A knezu neka bude s obje strane svetoga dijela i dostojanja gradskoga pred svetijem dijelom i pred gradskim dostojanjem, sa zapadne strane na zapad i s istoène strane na istok, a dužina da bude prema svakom od tijeh dijelova od zapadne meðe do istoène meðe.
8 Malowa adzakhala chigawo cha mfumu mu Israeli. Choncho mafumu anga sadzazunzanso anthu anga, koma adzidzalola Aisraeli kuti akhale ndi zigawo zawozawo.
Ta zemlja da mu je dostojanje u Izrailju, da više ne otimaju knezovi moji od naroda mojega, nego ostalu zemlju da dadu domu Izrailjevu po plemenima njihovijem.
9 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsono pakwana, inu akalonga a Israeli. Lekani nkhanza zanu ndi kupondereza anthu anga. Muzitsata chilungamo ndi kuchita zokomera anthu. Musapirikitse anthu anga mʼdzikomo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Ovako veli Gospod Gospod: dosta je, knezovi Izrailjevi; proðite se nasilja i otimanja, i tvorite sud i pravdu, i skinite teške poslove svoje s mojega naroda, govori Gospod Gospod.
10 Miyeso yanu yoyezera zinthu monga efa ndi bati zizikhala zokhulupirika.
Mjerila da su vam prava, i efa prava, i vat prav.
11 Efa ndi bati ikhale miyeso yolingana kukula kwake. Muyeso wa homeri ukhale wokwanira mabati khumi, ukhalenso wokwanira maefa khumi. Ndiye kuti kukula kwa miyeso iwiriyo kuzidzatsata kukula kwa homeriyo.
Efa i vat da su jedne mjere, da vat bere desetinu homora, i efa desetinu homora; mjera da im je prema homoru.
12 Muyeso wa sekeli ukhale wokwanira magera makumi awiri. Muyeso wa mina ukhale wolemera masekeli 60.
I sikal da je dvadeset gera, a mina da vam je dvadeset sikala, dvadeset i pet sikala, i petnaest sikala.
13 “‘Zopereka zomwe mudzidzapereka ndi izi: chimodzi mwa zigawo 60 za tirigu, barelenso chimodzimodzi ndiponso gawo limodzi la magawo asanu ndi limodzi la efa, kulitapa pa barele wa homeri.
Ovo je prinos što æete prinositi: šestina efe od homora pšenice, tako i od jeèma dajite šestinu efe od homora.
14 Gawo loyenera la mafuta, loyezedwa ndi bati, ndiponso chigawo mwa zigawo 100 za mafuta. Miyeso yake ili motere: mabati khumi afanana ndi homeri imodzi kapena kori imodzi.
A za ulje je uredba ova: vat je mjera za ulje; desetina vata od jednoga kora, koji je homor od deset vata, jer je deset vata homor.
15 Muperekenso nkhosa imodzi pa gulu lankhosa 200 za pa msipu wabwino wa mu Israeli. Izi zidzagwiritsidwa ntchito monga nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano ndi nsembe zopepesera milandu ya anthu. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
A od sitne stoke jedno od dvije stotine s dobrijeh pasišta sinova Izrailjevijeh za dar i za žrtvu paljenicu i za žrtvu zahvalnu, da se èini oèišæenje za njih, govori Gospod Gospod.
16 Anthu onse a mʼdzikomo azidzapereka zimenezi kwa mfumu ya Israeli.
Sav narod zemaljski da daje ovaj prinos knezu Izrailjevu.
17 Udzakhala udindo wa mfumu kupereka zofunikira ku nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, ndi nsembe za zakumwa pa nthawi ya zikondwerero, chikondwerero cha mwezi watsopano ndi cha masabata, nthawi yonse ya zikondwerero zoyikika za Aisraeli. Mfumuyo idzapereka nsembe zopepesera machimo, nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano kuti zikhale nsembe zopepesera machimo a Aisraeli.
A knez je dužan davati žrtve paljenice s darom i naljevom na praznike i na mladine i u subote, o svijem svetkovinama doma Izrailjeva; on neka prinosi žrtvu za grijeh s darom i žrtvu paljenicu i zahvalnu da èini oèišæenje za dom Izrailjev.
18 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba muzitenga mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndi kuchita mwambo woyeretsa malo opatulika.
Ovako veli Gospod Gospod: prvoga dana prvoga mjeseca uzmi junca zdrava, i oèisti svetinju njim.
19 Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera machimoyo ndipo awapake pa mphuthu za Nyumba ya Mulungu, pa ngodya zinayi za pamwamba pa guwa lansembe ndi pa mphuthu za pa chipata cha bwalo la mʼkati.
I neka sveštenik uzme krvi od te žrtve za grijeh, i pomaže njom dovratnike na domu i èetiri ugla od pojasa na oltaru i dovratnike od vrata na unutrašnjem trijemu.
20 Muzichita chimodzimodzi pa tsiku la chisanu ndi chiwiri la mwezi, kuchitira aliyense amene wachimwa mosafuna kapena mosadziwa. Motero Nyumba ya Mulungu idzakhala yoyera.
Tako uèini i sedmoga dana istoga mjeseca za svakoga koji zgriješi iz neznanja i za prostoga; tako æete oèistiti dom.
21 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita chikondwerero cha Paska, chikondwerero chake cha masiku asanu ndi awiri. Pa masiku amenewo muzidzadya buledi wopanda yisiti.
Prvoga mjeseca èetrnaestoga dana da vam je pasha, praznik sedam dana, hljebovi prijesni da se jedu.
22 Pa tsiku loyamba la chikondwererocho, mfumu ipereke nsembe ya ngʼombe yayimuna monga nsembe yopepesera machimo ake ndi machimo a anthu onse a mʼdziko.
I taj dan neka prinese knez za se i za sav narod zemaljski junca na žrtvu za grijeh.
23 Pa masiku asanu ndi awiri a chikondwererocho, mfumu ipereke kwa Yehova nsembe zopsereza izi: ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, zonsezi zopanda chilema. Pa masikuwa mfumu iziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
A za sedam dana praznika neka prinosi na žrtvu paljenicu Gospodu po sedam junaca i sedam ovnova zdravijeh na dan, za onijeh sedam dana, i na žrtvu za grijeh jarca na dan.
24 Pamodzi ndi ngʼombe iliyonse yayimuna ndi nkhosa iliyonse yayimuna, mfumu ipereke chopereka cha chakudya chokwanira efa imodzi ndiponso mafuta okwanira hini imodzi pa efa iliyonse.
I za dar po efu na junca i efu na ovna neka prinosi, i in ulja na svaku efu.
25 “‘Pa nthawi ya chikondwerero cha masiku asanu ndi awiri, chimene chimayamba pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mfumuyo iziperekanso nsembe za mtundu womwewo: nsembe zopepesera machimo, nsembe zopsereza, nsembe za chakudya ndi za mafuta.’”
Sedmoga mjeseca petnaestoga dana na praznik neka prinosi isto tako za sedam dana i žrtvu za grijeh i žrtvu paljenicu i dar i ulje.

< Ezekieli 45 >