< Ezekieli 44 >

1 Munthu uja anabwerera nane ku chipata chakunja kwa malo opatulika, chomwe chimayangʼana kummawa. Chipatacho chinali chotseka.
I odvede me opet k vratima spoljašnjim od svetinje, koja gledaju na istok, a ona bjehu zatvorena.
2 Yehova anandiwuza kuti, “Chipata ichi chikhale chotseka, chisatsekulidwe. Wina asalowerepo chifukwa Yehova, Mulungu wa Israeli walowera pomwepa.
I reèe mi Gospod: ova vrata neka budu zatvorena i da se ne otvoraju, i niko da ne ulazi na njih, jer je Gospod Bog Izrailjev ušao na njih; zato neka budu zatvorena.
3 Kalonga yekha angathe kukhala mʼmenemo ndi kumadya chakudya pamaso pa Yehova. Iye adzalowere pa njira ya ku khonde lamʼkati ndi kutulukiranso njira yomweyo.”
Za kneza su; sam knez neka sjeda na njima da jede hljeb pred Gospodom; kroz trijem od ovijeh vrata neka ulazi i istijem putem neka izlazi.
4 Kenaka munthuyo anandidzeretsa pa chipata chakumpoto ndipo tinafika kumaso kwa Nyumba ya Mulungu. Nditapenyetsetsa ndinangoona ulemerero wa Yehova utadzaza mʼNyumba ya Mulungu, ndipo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba.
I odvede me k sjevernijem vratima pred dom; i vidjeh, i gle, dom Gospodnji bješe pun slave Gospodnje, i padoh na lice svoje.
5 Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, samala bwino ndipo uyangʼanitsitse ndi kumvetsa bwino zonse zimene ndikuwuze zokhudza malamulo ndi malangizo a Nyumbayi. Usamalitse za amene angalowe ndi kutuluka mʼNyumbayi.
I reèe mi Gospod: sine èovjeèji, pazi srcem svojim i vidi oèima svojim i slušaj ušima svojim, što æu ti kazati za sve uredbe doma Gospodnjega i za sve zakone njegove; pazi srcem svojim na sve ulaze u dom i na sve izlaze iz svetinje.
6 Uwuze mtundu wopanduka wa Israeli kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu Aisraeli, andikwana machitidwe anu onyansawo!
I reci odmetnièkom domu Izrailjevu: ovako veli Gospod Gospod: dosta je gadova vaših, dome Izrailjev,
7 Munalowetsa alendo osachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi momwe mʼNyumba yanga ndipotu anayipitsa Nyumba yanga. Pamene inu munkandipatsa chakudya changa ndi magazi omwe kuwonjezera pa zonyansa zanu zonse ndiye kuti munaphwanya pangano langa.
Što uvodiste tuðince neobrezana srca i neobrezana tijela da budu u mojoj svetinji da skvrne dom moj, i prinosiste moj hljeb, pretilinu i krv, i tako prestupaše moj zavjet osim svijeh gadova vaših;
8 Mʼmalo moti muzisamalira zinthu zanga zopatulika, mwayika alendo kuti aziyangʼanira malo anga opatulika.
I ne izvršivaste što treba za moju svetinju, nego postaviste ljude po svojoj volji da izvršuju što treba u mojoj svetinji.
9 Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Palibe mlendo wosachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi ngakhalenso mlendo amene amakhala pakati pa Aisraeli amene adzalowe mʼmalo anga opatulika.
Ovako veli Gospod Gospod: nijedan tuðin neobrezana srca i neobrezana tijela da ne dolazi u moju svetinju, nijedan od svijeh tuðinaca koji su meðu sinovima Izrailjevijem.
10 “Ndiponso Alevi amene anandisiya kutali pa nthawi imene Israeli anasochera potsata mafano, adzalangidwa chifukwa cha tchimo lawo.
A Leviti koji otstupiše od mene kad zaðe Izrailj, koji zaðoše od mene za gadnijem bogovima svojim, nosiæe bezakonje svoje.
11 Adzangokhala atumiki chabe mʼmalo anga opatulika. Azidzayangʼanira zipata za Nyumba ya Mulungu ndi kugwira ntchito kumeneko. Azidzapha nyama za nsembe zopsereza ndi za nsembe zina za anthu. Choncho azidzayimirira pamaso pa anthu nʼkumawatumikira.
I biæe sluge u mojoj svetinji u službi na vratima od doma služeæi domu; oni æe klati žrtve paljenice i druge žrtve narodu, i stajaæe pred njima služeæi im.
12 Iwowa ankatumikira anthu popembedza mafano awo, ndipo anachititsa Aisraeli kugwa mu uchimo. Nʼchifukwa chake Ine ndikulumbira kuti iwowa ayenera kulangidwa chifukwa cha machimo awo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Što im služiše pred gadnijem bogovima njihovijem i biše domu Izrailjevu spoticanje na bezakonje, zato podigoh ruku svoju na njih, govori Gospod Gospod, da æe nositi bezakonje svoje,
13 Iwo sayenera kufika pafupi ndi Ine ndi kunditumikira ngati ansembe, kapena kuyandikira chilichonse cha zinthu zanga zopatulika, kapenanso zopereka zanga zopatulika kwambiri. Iwo adzachititsidwa manyazi chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
I neæe pristupati k meni da mi vrše sveštenièku službu, niti kojoj svetinji mojoj, ni svetinji nad svetinjama neæe pristupati, nego æe nositi sramotu svoju i gadove svoje, koje èiniše.
14 Komabe ndidzawayika kuti aziyangʼanira Nyumba yanga ndi kutumikira pa ntchito zake zonse zoyenera kuti zigwiridwe mʼmenemo.
Nego æu ih postaviti za èuvare domu na svaku službu njegovu i na sve što biva u njemu.
15 “Koma ansembe, a fuko la Levi, a banja la Zadoki amene ankatumikira mokhulupirika ku malo anga opatulika pa nthawi imene Aisraeli anasochera ndi kundisiya Ine; iwowa adzasendera kwa Ine kudzanditumikira. Adzafika pamaso panga kuti apereke nsembe za mafuta ndi magazi. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
A sveštenici Leviti sinovi Sadokovi, koji izvršivahu što treba u mojoj svetinji, kad sinovi Izrailjevi zaðoše od mene, oni æe pristupati k meni da mi služe, i stajaæe preda mnom prinoseæi mi pretilinu i krv, govori Gospod Gospod.
16 Okhawa ndiwo adzalowe ku malo anga opatulika ndi kudzayandikira tebulo langa kuti adzanditumikire. Amenewa okha ndiwo adzasamalire zinthu zanga.
Oni neka ulaze u moju svetinju i oni neka pristupaju k stolu mojemu da mi služe i neka izvršuju što sam zapovjedio da se izvršuje.
17 “Pamene alowa ku zipata za bwalo lamʼkati azivala zovala zabafuta. Asamavale chovala china chilichonse cha ubweya wankhosa pamene akutumikira pa zipata za bwalo la mʼkati kapena kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
I kad ulaze na vrata unutrašnjega trijema, neka obuku lanene haljine, i ništa da ne bude na njima vuneno kad služe na vratima unutrašnjega trijema i u njemu.
18 Azivala nduwira za bafuta ndi kabudula wabafuta mʼkati. Asavale chilichonse chowachititsa thukuta.
Na glavama neka im budu kape lanene i gaæe lanene po bedrima, i da se ne pašu nièim oda šta bi se znojili.
19 Pamene atuluka ndi kupita ku bwalo lakunja kumene kuli anthu, azivula zovala zimene amatumikira nazo, ndipo azisiye zovalazo mu zipinda zopatulika. Pambuyo pake avale zovala zina, kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu enawo ndi zovala zawozo.
A kad izlaze u trijem spoljašnji, u spoljašnji trijem k narodu, neka svuku sa sebe haljine u kojima služe, i ostave ih u klijetima svetijem, pa neka obuku druge haljine, da ne osveæuju naroda haljinama svojim.
20 “‘Ansembe asamamete mpala kapena kusunga tsitsi lalitali kwambiri, koma azingoliyepula.
I glave svoje da ne briju, a ni kose da ne ostavljaju, nego neka strigu glave svoje.
21 Wansembe asamwe vinyo pamene ali pafupi kulowa mʼbwalo la mʼkati.
I vina da ne pije nijedan sveštenik kad hoæe da uðe u unutrašnji trijem.
22 Iwo asakwatire akazi amasiye kapena osudzulidwa; koma azikwatira anamwali osadziwa mwamuna a fuko la Israeli kapena akazi amasiye a ansembe anzawo.
I udovicom ni puštenicom da se ne žene, nego djevojkom od sjemena doma Izrailjeva ili udovicom sveštenièkom neka se žene.
23 Ansembe aziphunzitsa anthu anga kusiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, ndiponso pakati pa zinthu zoyenera ndi zosayenera kuperekedwa nsembe.
I narod moj neka uèe što je sveto što li nije sveto, i neka ih uèe raspoznavati neèisto od èistoga.
24 “‘Pakakhala milandu, ansembe azikhala oweruza ndipo agamule milanduyo potsata malamulo anga. Atsate malamulo anga ndi malangizo anga pa za masiku anga onse a chikondwerero. Asamalirenso kuti masiku anga a Sabata akhale oyera.
A u raspri neka stanu da sude, po mojim zakonima neka sude, i zakone moje i uredbe moje neka drže o svijem praznicima mojim, i subote moje neka svetkuju.
25 “‘Wansembe asadziyipitse pokhudza munthu wakufa, pokhapokha ngati wakufayo ndi abambo ake kapena amayi ake, mwana wake wamwamuna kapena wamkazi, mʼbale wake kapena mlongo wake wosakwatiwa.
I k mrtvacu da ne idu da se ne oskvrne; samo za ocem i za materom i za sinom i za kæerju, za bratom i za sestrom neudatom mogu se oskvrniti.
26 Atatha kuyeretsedwa adikirebe masiku asanu ndi awiri kuti ayere ndithu.
A kad se oèisti, neka mu se broji sedam dana.
27 Pa tsiku lomwe akukalowa mʼbwalo la mʼkati la malo opatulika kuti akatumikire, apereke nsembe yopepesera machimo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
I u koji bi dan ušao u svetinju, u trijem unutrašnji, da služi u svetinji, neka prinese žrtvu za grijeh svoj, govori Gospod Gospod.
28 “‘Ansembe asadzakhale ndi cholowa chilichonse ayi. Cholowa chawo ndi Ine. Musadzawapatse chuma mu Israeli; Ine ndidzakhala chuma chawo.
A našljedstvo što æe imati, ja sam njihovo našljedstvo; i vi im ne dajte dostojanja u Izrailju, ja sam njihovo dostojanje.
29 Iwo azidzadya nsembe ya chakudya, nsembe yopereka chifukwa cha tchimo ndi nsembe yopepesera machimo. Zinthu zonse zoperekedwa kwa Yehova mu Israeli zidzakhala zawo.
Dar i žrtvu za grijeh i žrtvu za krivicu oni æe jesti; i sve zavjetovano u Izrailju njihovo æe biti.
30 Zabwino za zipatso zanu zoyambirira kucha ndiponso mphatso zanu zonse zapadera zidzakhala za ansembe. Inu muziwapatsa chigawo choyamba cha ufa wanu kuti pa nyumba panu pakhale madalitso.
I prvine od svakoga prvoga roda i svi prinosi podizani od svega izmeðu svijeh prinosa vaših biæe sveštenicima; i prvine od tijesta svojega davaæete svešteniku da bi poèivao blagoslov na domovima vašim.
31 Ansembe sayenera kudya kalikonse kofa kokha, kaya mbalame, kapena nyama. Kapena yochita kujiwa.’”
Sveštenici da ne jedu mrcinoga ni što zvjerka raskine, bilo ptica ili što od stoke.

< Ezekieli 44 >