< Ezekieli 45 >

1 “‘Mukamadzagawa dziko kuti fuko lililonse lilandire cholowa chake, mudzapatuleko chigawo chimodzi kuti chikhale cha Yehova. Mulitali mwake mudzakhale makilomita khumi ndi awiri ndi theka ndipo mulifupi mwake makilomita khumi. Malo onsewo adzakhale opatulika.
And whanne ye schulen bigynne to departe the lond bi partis, departe ye the firste thingis to the Lord, an halewid thing of the lond, fyue and twenti thousynde of rehedis in lengthe, and ten thousynde of rehedis in breede; it schal be halewid in al the coost therof by cumpas.
2 Mʼkati mwa chigawo chimenechi, malo a mamita 250 mbali iliyonse adzakhala malo a Nyumba ya Mulungu. Pozungulira pake ponse padzakhala malo a mamita 25.
And it schal be halewid on ech part in fyue hundrid rehedis bi fyue hundrid, in foure sidis bi cumpas, and in fifti cubitis in to the subarbis therof bi cumpas.
3 Mʼchigawo chopatulikacho muyeze malo a makilomita 12 ndi theka mulitali mwake, makilomita asanu mulifupi mwake. Pamenepo padzakhala malo opatulika kwambiri.
And fro this mesure thou schalt mete the lengthe of fyue and twenti thousynde of rehedis, and the breede of ten thousynde; and the temple and the hooli of hooli thingis schal be in it.
4 Malo opatulika amenewa adzakhalanso a ansembe amene amatumikira ku malo opatulika, amene amayandikira Yehova kuti amutumikire. Pamenepo padzakhala malo omangapo nyumba zawo ndi malo omangapo Nyumba ya Mulungu.
An halewid thing of the lond schal be to prestis, the mynystris of seyntuarie, that neiyen to the seruyce of the Lord; and a place schal be to hem in to housis, and in to the seyntuarie of hoolynesse.
5 Alevi otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzakhala ndi malo a makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake ndi makilomita asanu mulifupi mwake. Kumeneko ndiko kudzakhale midzi yawo.
Sotheli fyue and twenti thousynde of lengthe schulen be, and ten thousynde of breede; but the dekenes that mynystren to the hous, thei schulen haue in possessioun twenti treseries.
6 “‘Moyandikana ndi malo opatulika, padzakhale malo a makilomita awiri ndi theka mulifupi mwake ndi makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake; kuti akhale malo a mzinda. Malo amenewa adzakhala a Aisraeli onse.
And ye schulen yyue the possessioun of the citee, fyue thousynde rehedis of breede, and fyue and twenti thousynde of lengthe, bi the departyng of the seyntuarie, to al the hous of Israel.
7 “‘Mfumu idzakhale ndi malo okhudzana ndi chigawo cha malo opatulika ndi cha mzinda. Malowo ayandikane ndi zigawozo chakummawa ndi chakumadzulo. Malowo atalike ngati chigawo chimodzi cha fuko la Israeli kuyambira ku malire akummawa mpaka ku malire akumadzulo.
And ye schulen yyue a porcioun to the prince on this side and on that side, bisidis the departyng of the seyntuarie, and bisidis the possessioun of the citee, ayens the face of departynge of seyntuarie, and ayens the face of possessioun of the citee; fro the side of the se til to the see, and fro the side of the eest `til to the eest, schal be of the possessioun of the prince. Forsothe the lengthe bi ech of the partis, fro the west ende til to the eest ende of the lond,
8 Malowa adzakhala chigawo cha mfumu mu Israeli. Choncho mafumu anga sadzazunzanso anthu anga, koma adzidzalola Aisraeli kuti akhale ndi zigawo zawozawo.
schal be possessioun to hym in Israel; and the princes schulen no more robbe my puple, but thei schulen yyue the lond to the hous of Israel, bi the lynagis of hem.
9 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsono pakwana, inu akalonga a Israeli. Lekani nkhanza zanu ndi kupondereza anthu anga. Muzitsata chilungamo ndi kuchita zokomera anthu. Musapirikitse anthu anga mʼdzikomo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
The Lord God seith these thingis, O! princes of Israel, suffice it to you, leue ye wickidnesse `and raueyns, and do ye doom and riytfulnesse; departe ye youre niy coostis fro my puple, seith the Lord God.
10 Miyeso yanu yoyezera zinthu monga efa ndi bati zizikhala zokhulupirika.
A iust balaunce, and a iust mesure clepid ephi, and a iust mesure clepid bathus, schulen be to you.
11 Efa ndi bati ikhale miyeso yolingana kukula kwake. Muyeso wa homeri ukhale wokwanira mabati khumi, ukhalenso wokwanira maefa khumi. Ndiye kuti kukula kwa miyeso iwiriyo kuzidzatsata kukula kwa homeriyo.
Ephi and bathus schulen be euene, and of o mesure, that bathus take the tenthe part of the mesure clepid corus, and that ephi take the tenthe part of the mesure corus; bi the mesure of corus schal be euene weiynge of tho.
12 Muyeso wa sekeli ukhale wokwanira magera makumi awiri. Muyeso wa mina ukhale wolemera masekeli 60.
Forsothe a sicle schal haue twenti halpens; certis twenti siclis, and fyue and twenti siclis, and fiftene siclis maken a besaunt.
13 “‘Zopereka zomwe mudzidzapereka ndi izi: chimodzi mwa zigawo 60 za tirigu, barelenso chimodzimodzi ndiponso gawo limodzi la magawo asanu ndi limodzi la efa, kulitapa pa barele wa homeri.
And these ben the firste fruytis whiche ye schulen take awei; the sixte part of ephi of a corus of wheete, and the sixte part of ephi of a corus of barli.
14 Gawo loyenera la mafuta, loyezedwa ndi bati, ndiponso chigawo mwa zigawo 100 za mafuta. Miyeso yake ili motere: mabati khumi afanana ndi homeri imodzi kapena kori imodzi.
Also the mesure of oile; a bathus of oile is the tenthe part of corus, and ten bathus maken o corus; for ten bathus fillen o corus.
15 Muperekenso nkhosa imodzi pa gulu lankhosa 200 za pa msipu wabwino wa mu Israeli. Izi zidzagwiritsidwa ntchito monga nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano ndi nsembe zopepesera milandu ya anthu. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
And `a ram of the floc of twei hundrid, of these whiche the men of Israel nurschen, in to sacrifice, and in to brent sacrifice, and in to pesible sacrifices, to clense for hem, seith the Lord God.
16 Anthu onse a mʼdzikomo azidzapereka zimenezi kwa mfumu ya Israeli.
Al the puple of the lond schal be boundun in these firste fruytis to the prince of Israel.
17 Udzakhala udindo wa mfumu kupereka zofunikira ku nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, ndi nsembe za zakumwa pa nthawi ya zikondwerero, chikondwerero cha mwezi watsopano ndi cha masabata, nthawi yonse ya zikondwerero zoyikika za Aisraeli. Mfumuyo idzapereka nsembe zopepesera machimo, nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano kuti zikhale nsembe zopepesera machimo a Aisraeli.
And on the prince schulen be brent sacrifices, and sacrifice, and moiste sacrifices, in solempnytees, and in kalendis, ether bigynnyngis of monethis, and in sabatis, and in alle the solempnytees of the hous of Israel; he schal make sacrifice, for synne, and brent sacrifice, and pesible sacrifices, to clense for the hous of Israel.
18 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba muzitenga mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndi kuchita mwambo woyeretsa malo opatulika.
The Lord God seith these thingis, In the firste moneth, in the firste dai of the monethe, thou schalt take a calf with out wem of the drooue, and thou schalt clense the seyntuarie.
19 Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera machimoyo ndipo awapake pa mphuthu za Nyumba ya Mulungu, pa ngodya zinayi za pamwamba pa guwa lansembe ndi pa mphuthu za pa chipata cha bwalo la mʼkati.
And the preest schal take of the blood of the beeste, that schal be for synne; and he schal putte in the postis of the hous, and in foure corneris of the heiythe of the auter, and in the postis of the yate of the ynnere halle.
20 Muzichita chimodzimodzi pa tsiku la chisanu ndi chiwiri la mwezi, kuchitira aliyense amene wachimwa mosafuna kapena mosadziwa. Motero Nyumba ya Mulungu idzakhala yoyera.
And thus thou schalt do in the seuenthe dai of the monethe, for ech that knew not, and was disseyued bi errour, and thou schalt clense for the hous.
21 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita chikondwerero cha Paska, chikondwerero chake cha masiku asanu ndi awiri. Pa masiku amenewo muzidzadya buledi wopanda yisiti.
In the firste monethe, in the fourtenthe dai of the monethe, the solempnytee of pask schal be to you; therf looues schulen be etun bi seuene daies.
22 Pa tsiku loyamba la chikondwererocho, mfumu ipereke nsembe ya ngʼombe yayimuna monga nsembe yopepesera machimo ake ndi machimo a anthu onse a mʼdziko.
And the prince schal make a calf for synne in that dai, for hym silf and for al the puple of the lond.
23 Pa masiku asanu ndi awiri a chikondwererocho, mfumu ipereke kwa Yehova nsembe zopsereza izi: ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, zonsezi zopanda chilema. Pa masikuwa mfumu iziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
And in the solempnytee of seuene daies he schal make brent sacrifice to the Lord; he schal offre seuene caluys and seuene wetheris with out wem ech dai, bi seuene daies, and ech dai a buc of geet, for synne.
24 Pamodzi ndi ngʼombe iliyonse yayimuna ndi nkhosa iliyonse yayimuna, mfumu ipereke chopereka cha chakudya chokwanira efa imodzi ndiponso mafuta okwanira hini imodzi pa efa iliyonse.
And he schal make the sacrifice of ephi by a calf, and of ephi by a wether, and of oile the mesure hyn, bi ech ephi.
25 “‘Pa nthawi ya chikondwerero cha masiku asanu ndi awiri, chimene chimayamba pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mfumuyo iziperekanso nsembe za mtundu womwewo: nsembe zopepesera machimo, nsembe zopsereza, nsembe za chakudya ndi za mafuta.’”
In the seuenthe monethe, in the fiftenthe dai of the monethe, in the solempnytee, he schal make as tho ben biforseid, bi seuene daies, as wel for synne as for brent sacrifice, and in sacrifice, and in oile.

< Ezekieli 45 >